< Ezekieli 40 >

1 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
W dwudziestym piątym roku naszego wygnania, na początku roku, dziesiątego [dnia] miesiąca, czternaście lat po zburzeniu miasta, w tym właśnie dniu spoczęła na mnie ręka PANA i zaprowadził mnie tam.
2 Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
W widzeniach Bożych przywiódł mnie do ziemi Izraela i postawił na bardzo wysokiej górze, na której było coś jakby budowa miasta, na południu.
3 Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
I zaprowadził mnie tam, a oto mąż, który z wyglądu był jakby ze spiżu, miał lniany sznur w ręku i pręt mierniczy, a stał w bramie.
4 Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
I przemówił do mnie ten mąż: Synu człowieczy, popatrz swymi oczami, słuchaj swymi uszami i weź sobie do serca wszystko, co ci pokażę. Po to bowiem zostałeś tu przyprowadzony, aby ci to pokazać. Oznajmij wszystko, co widzisz, domowi Izraela.
5 Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
I oto mur otaczał dom ze wszystkich stron dokoła, a w ręku tego męża [był] pręt mierniczy na sześć łokci – liczonych jako łokieć i szerokość dłoni – i wymierzył grubość budowli – jeden pręt, i wysokość – jeden pręt.
6 Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
Potem wszedł do bramy, która była [zwrócona] ku wschodowi, wszedł po schodach i zmierzył próg bramy: jeden pręt szerokości, a drugi próg [miał] jeden pręt szerokości.
7 Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
Każda wnęka miała jeden pręt długości i jeden pręt szerokości, a między wnękami był [odstęp] na pięć łokci; próg bramy obok przedsionka bramy od wewnątrz [wynosił] jeden pręt.
8 Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
I zmierzył przedsionek bramy od wewnątrz – jeden pręt.
9 Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
Zmierzył też przedsionek bramy – osiem łokci, a jej filary – dwa łokcie. Przedsionek bramy był wewnątrz.
10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
Wnęki bramy wschodniej [były] trzy z jednej i trzy z drugiej strony; wszystkie trzy miały ten sam wymiar. Jeden wymiar miały też filary po obu stronach.
11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
Zmierzył też szerokość wejścia bramy – dziesięć łokci, [a] długość bramy – trzynaście łokci.
12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
Przed wnękami była także przegroda na jeden łokieć, jeden łokieć miała też przegroda po drugiej stronie. [Każda] wnęka miała po sześć łokci z jednej i sześć łokci z drugiej strony.
13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
Potem zmierzył bramę od dachu [jednej] wnęki aż do dachu drugiej, szerokość była na dwadzieścia pięć łokci, a drzwi [były] naprzeciwko siebie.
14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
I uczynił filary na sześćdziesiąt łokci, a każdy filar na dziedzińcu u bramy wokoło [miał jedną miarę].
15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
A od fasady bramy wejściowej do fasady przedsionka wewnątrz bramy [było] pięćdziesiąt łokci.
16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
[Były] też wąskie okna we wnękach, przy filarach wewnątrz bramy dokoła, a także przy przedsionkach. Dokoła od wewnątrz były okna, a na filarach [były] palmy.
17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
Potem przyprowadził mnie na dziedziniec zewnętrzny, a oto [znajdowały] się [tam] komory i posadzka uczyniona na dziedzińcu zewsząd dokoła: trzydzieści komór [było] na tej posadzce.
18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
A posadzka [była] wzdłuż bram, odpowiednio do długości bram. Była to posadzka dolna.
19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Potem zmierzył odległość od fasady bramy dolnej do fasady [bramy] dziedzińca wewnętrznego z zewnątrz: sto łokci w kierunku wschodnim i północnym.
20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
Zmierzył też długość i szerokość bramy północnej na dziedzińcu zewnętrznym.
21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Miała trzy wnęki z jednej i trzy z drugiej strony; jej filary i przedsionki miały taki sam wymiar jak pierwsza brama: pięćdziesiąt łokci długości i dwadzieścia pięć łokci szerokości.
22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
Jej okna, przedsionek i palmy [miały] taki sam wymiar jak brama wschodnia. Po siedmiu stopniach wchodziło się do niej, a jej przedsionek był tuż przed schodami.
23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Brama dziedzińca wewnętrznego była naprzeciwko bramy północnej, jak [brama] wschodnia; i zmierzył od bramy do bramy – sto łokci.
24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
Potem zaprowadził mnie w stronę południa, a oto była brama południowa; i zmierzył jej filary i przedsionek – [miały] te same wymiary.
25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
[Miała] ona, podobnie jak jej przedsionek, okna wokoło, tak jak tamte okna. Miała pięćdziesiąt łokci długości i dwadzieścia pięć łokci szerokości.
26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
Prowadziło do niej siedem stopni, a jej przedsionek był przed nimi. Miała ona palmy na filarach z jednej i z drugiej strony.
27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Była też brama południowa na dziedzińcu wewnętrznym; i zmierzył od bramy do bramy w stronę południa – sto łokci.
28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
Potem zaprowadził mnie na dziedziniec wewnętrzny przez bramę południową i zmierzył bramę południową: [miała] te same wymiary.
29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
A jej wnęki, jej filary i jej przedsionek [miały] te same wymiary. [Miała] ona również, jak i jej przedsionek, okna wokoło. Miała pięćdziesiąt łokci długości i dwadzieścia pięć łokci szerokości.
30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
Dokoła był przedsionek na dwadzieścia pięć łokci długości i pięć łokci szerokości.
31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
A jej przedsionek [był] na dziedzińcu zewnętrznym, a na jej filarach [były] palmy. Prowadziło do niej osiem stopni.
32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
Zaprowadził mnie też na dziedziniec wewnętrzny w stronę wschodu i zmierzył bramę: m[iała] te same wymiary.
33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Jej wnęki, jej filary i jej przedsionek miały te same wymiary. Miała ona również, tak jak jej przedsionek, okna wokoło. Miała pięćdziesiąt łokci długości, dwadzieścia pięć łokci szerokości.
34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
A jej przedsionek był na dziedzińcu zewnętrznym, a na jej filarach były palmy po obu stronach. Prowadziło do niej osiem stopni.
35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
Potem zaprowadził mnie do bramy północnej i zmierzył ją: [miała] te same wymiary;
36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Jej wnęki, jej filary i jej przedsionek, a także jej okna wokoło. Jej długość [wynosiła] pięćdziesiąt łokci, a jej szerokość – dwadzieścia pięć łokci.
37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Jej filary były na dziedzińcu zewnętrznym, a na jej filarach były palmy po obu stronach. Prowadziło do niej osiem stopni.
38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
[Były] też komory i wejście do nich przy filarach bram, tam obmywano ofiarę całopalną.
39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
W przedsionku bramy były dwa stoły po jednej stronie i dwa stoły po drugiej stronie, na których zabijano ofiarę całopalną, ofiarę za grzech i ofiarę za przewinienie.
40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
Na stronie zewnętrznej, przy wejściu bramy północnej, [były] dwa stoły, także i po drugiej stronie, która jest przy przedsionku bramy, [były] dwa stoły.
41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
Cztery stoły z jednej i cztery stoły z drugiej strony, z boku bramy; [wszystkich] stołów, na których zabijano ofiary, było osiem.
42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
Te cztery stoły do całopalenia [były] z kamienia ciosanego, długie na półtora łokcia, szerokie na półtora łokcia i wysokie na jeden łokieć. Na nich kładziono sprzęt do zabijania ofiary całopalnej i [innych] ofiar.
43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
Wokoło [były] też przymocowane haki o grubości jednej dłoni, a mięso [leżało] na stołach dla ofiar.
44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
Na zewnątrz bramy wewnętrznej, na dziedzińcu wewnętrznym, były komory dla śpiewaków. [Jeden rząd był] z boku bramy północnej, zwrócony w kierunku południa, drugi rząd był z boku bramy wschodniej, zwrócony w kierunku północy.
45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
I powiedział do mnie: Te komory, które są zwrócone w kierunku południa, są dla kapłanów, którzy pełnią straż w domu.
46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
[Te zaś] komory, które są zwrócone w kierunku północy, są dla kapłanów, którzy pełnią straż przy ołtarzu. Są to synowie Sadoka, którzy spośród synów Lewiego zbliżają się do PANA, aby mu służyć.
47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
I zmierzył dziedziniec: długość wynosiła sto łokci, szerokość – sto łokci, był to kwadrat; a ołtarz [był] przed domem.
48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
Potem wprowadził mnie do przedsionka domu i zmierzył filary przedsionka: pięć łokci z jednej i pięć łokci z drugiej strony. Szerokość bramy [wynosiła] trzy łokcie z jednej i trzy łokcie z drugiej strony.
49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.
Długość przedsionka wynosiła dwadzieścia łokci, a szerokość – jedenaście łokci. Wstępowało się do niego po stopniach; [były] też kolumny przy filarach, jedna z jednej, druga z drugiej strony.

< Ezekieli 40 >