< Hoseya 13 >

1 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
Gdy Efraim przemawiał, [panował] strach, bo był wywyższony w Izraelu; ale gdy zgrzeszył przy Baalu, wtedy umarł.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
A teraz dodają do swego grzechu, bo czynią sobie odlane posągi ze swego srebra i straszne bożki według swego pomysłu, a to wszystko jest dziełem rzemieślnika; [jednak] sami o nich mówią: Ludzie, którzy składają ofiary, niech całują cielce.
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
Dlatego staną się jak obłok poranny, jak przemijająca rosa poranna, jak plewy przez wicher porwane z klepiska i jak dym z komina.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
Ale ja jestem PAN, twój Bóg, [od wyjścia] z ziemi Egiptu, a nie będziesz znał [innego] Boga oprócz mnie. I nie ma [innego] zbawiciela oprócz mnie.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
Ja cię poznałem na pustyni, w ziemi bardzo suchej.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
Byli nasyceni dobrymi pastwiskami, ale gdy się nasycili, ich serce się wywyższyło; dlatego zapomnieli o mnie.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
Będę więc dla nich jak lew, jak lampart przy drodze [będę] czyhał.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
Napadnę na nich jak niedźwiedzica, której zabrano młode, rozerwę powłokę ich serca i pożrę ich tam jak lew, dziki zwierz ich rozszarpie.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
Zniszczyłeś się sam, Izraelu, ale we mnie jest twoja pomoc.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
Ja jestem twoim królem. Gdzież jest ten, który ma cię wybawić we wszystkich twoich miastach? I twoi sędziowie, o których mówiłeś: Daj mi króla i książąt.
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
Dałem ci [więc] króla w swoim gniewie i odebrałem [go] w swojej zapalczywości.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
Nieprawość Efraima [jest] związana, jego grzech jest ukryty.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
Ogarną go bóle rodzącej. On jest niemądrym synem, bo inaczej nie zostałby tak długo w łonie matki.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol h7585)
Wybawię ich z mocy grobu, wykupię ich od śmierci. O śmierci, będę twoją śmiercią! O grobie, będę twoim zniszczeniem! Żal się ukryje przed moimi oczami. (Sheol h7585)
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
Choćby on wśród braci przyniósł owoc, przyjdzie [jednak] wiatr ze wschodu, wiatr PANA wyruszy z pustyni i wysuszy jego źródło, i wysuszy jego zdrój. On zagarnie skarby wszelkich kosztownych naczyń.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Samaria będzie spustoszona, ponieważ sprzeciwiła się swemu Bogu. Padną od miecza, jej niemowlęta będą roztrzaskane, a jej brzemienne będą rozprute.

< Hoseya 13 >