< Ezekieli 38 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
Sine èovjeèji, okreni lice svoje prema Gogu u zemlji Magogu, knezu i glavi u Mesehu i Tuvalu, i prorokuj na nj;
3 Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
I reci: ovako veli Gospod Gospod: evo me na tebe, Gože, kneže i glavo Mesehu i Tuvalu;
4 Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
I vratiæu te natrag, i metnuæu ti žvale u èeljusti, i izvešæu tebe i svu vojsku tvoju, konje i konjike, sve dobro odjevene, zbor veliki sa štitovima i štitiæima, sve koji maèem mašu,
5 Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
S njima Persijance, Etiopljane i Puteje, sve sa štitovima i pod šljemovima,
6 Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
Gomera i sve èete njegove, dom Togarmin sa sjevernoga kraja i sve èete njegove, mnoge narode s tobom.
7 “‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
Pripravi se i spremi se ti i sve ljudstvo tvoje, što se sabralo kod tebe, i budi im stražar.
8 Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
Poslije mnogo vremena biæeš pohoðen, i pošljednjih godina doæi æeš u zemlju izbavljenu od maèa i sabranu iz mnogih naroda, u gore Izrailjeve, koje bjehu jednako puste, a oni æe izvedeni iz naroda svi živjeti bez straha.
9 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
I podignuæeš se, i doæi æeš kao bura, biæeš kao oblak da pokriješ zemlju ti i sve èete tvoje i mnogi narodi s tobom.
10 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
Ovako veli Gospod Gospod: i tada æe ti doæi u srce stvari, i smišljaæeš zle misli.
11 Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
I reæi æeš: idem na zemlju gdje su sela, i udariæu na mirni narod koji živi bez straha, koji svi žive u mjestima bez zidova i nemaju ni prijevornica ni vrata,
12 Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
Da naplijeniš plijena i nagrabiš grabeža, da posegneš rukom svojom na pustinje naseljene i na narod sabrani iz naroda, koji se bavi stokom i imanjem, i živi usred zemlje.
13 Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
Sava i Dedan i trgovci Tarsiski i svi laviæi njegovi kazaæe ti: jesi li došao da plijeniš plijen? jesi li skupio ljudstvo svoje da grabiš grabež? da odneseš srebro i zlato, da uzmeš stoku i trg, da naplijeniš mnogo plijena?
14 “Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
Zato prorokuj, sine èovjeèji, i reci Gogu: ovako veli Gospod Gospod: u ono vrijeme, kad æe moj narod Izrailj živjeti bez straha, neæeš li znati?
15 Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
I doæi æeš iz svoga mjesta, sa sjevernoga kraja, ti i mnogi narodi s tobom, svi jašuæi na konjma, mnoštvo veliko i vojska velika.
16 Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
I podignuæeš se na moj narod Izrailja kao oblak da pokriješ zemlju; u pošljednje vrijeme dovešæu te na zemlju svoju da me poznadu narodi kad se posvetim u tebi pred njima, Gože!
17 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
Ovako veli Gospod Gospod: nijesi li ti onaj o kom govorih u staro vrijeme preko sluga svojih, proroka Izrailjevijeh, koji prorokovaše u ono vrijeme godinama da æu te dovesti na njih.
18 Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
A kad doðe Gog na zemlju Izrailjevu, govori Gospod Gospod, onda æe se podignuti jarost moja u gnjevu mom.
19 Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
I u revnosti svojoj, u ognju gnjeva svojega govoriæu: doista, tada æe biti drhat veliki u zemlji Izrailjevoj.
20 Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
I ribe morske i ptice nebeske i zvijeri poljske i sve što gamiže po zemlji, i svi ljudi po zemlji zadrhtaæe od mene, i gore æe se razvaliti i vrleti popadati, i svi æe zidovi popadati na zemlju.
21 Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
I dozvaæu na nj maè po svijem gorama svojim, govori Gospod Gospod: maè æe se svakoga obratiti na brata njegova.
22 Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
I sudiæu mu pomorom i krvlju; i pustiæu na nj i na èete njegove i na mnoge narode, koji budu s njim, silan dažd, kamenje od grada, oganj i sumpor.
23 Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”
I proslaviæu se i posvetiæu se i biæu poznat pred mnogim narodima, i poznaæe da sam ja Gospod.

< Ezekieli 38 >