< Ezekieli 37 >

1 Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
Ruka Gospodnja doðe nada me, i Gospod me izvede u duhu, i postavi me usred polja, koje bijaše puno kosti.
2 Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
I provede me pokraj njih unaokolo, i gle, bijaše ih vrlo mnogo u polju, i gle, bijahu vrlo suhe.
3 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
I reèe mi: sine èovjeèji, hoæe li oživjeti ove kosti? A ja rekoh: Gospode Gospode, ti znaš.
4 Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
Tada mi reèe: prorokuj za te kosti, i kaži im: suhe kosti, èujte rijeè Gospodnju.
5 Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
Ovako govori Gospod Gospod ovijem kostima: gle, ja æu metnuti u vas duh, i oživjeæete.
6 Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
I metnuæu na vas žile, i obložiæu vas mesom, i navuæi æu na vas kožu, i metnuæu u vas duh, i oživjeæete, i poznaæete da sam ja Gospod.
7 Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
Tada stadoh prorokovati, kako mi se zapovjedi; a kad prorokovah nasta glas, i gle potres, i kosti se pribirahu svaka ka svojoj kosti.
8 Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
I pogledah, i gle, po njima izidoše žile i meso, i ozgo se koža navuèe; ali duha ne bješe u njima.
9 Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
Tada mi reèe: prorokuj duhu, prorokuj, sine èovjeèji, i reci duhu: ovako veli Gospod Gospod: od èetiri vjetra doði, duše, i duni na ove pobijene da ožive.
10 Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
I prorokovah, kako mi se zapovjedi, i uðe u njih duh, i oživješe, i stadoše na noge, bješe vojska vrlo velika.
11 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
Tada mi reèe: sine èovjeèji, ove su kosti sav dom Izrailjev; gle, govore: posahnuše kosti naše i proðe nadanje naše, propadosmo.
12 Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
Zato prorokuj, i kaži im: ovako veli Gospod Gospod: evo, ja æu otvoriti grobove vaše, i izvešæu vas iz grobova vaših, narode moj, i dovešæu vas u zemlju Izrailjevu.
13 Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
I poznaæete da sam ja Gospod, kad otvorim grobove vaše, i izvedem vas iz grobova vaših, narode moj.
14 Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
I metnuæu duh svoj u vas da oživite, i naseliæu vas u vašoj zemlji, i poznaæete da ja govorim i èinim, govori Gospod.
15 Yehova anandiyankhula kuti:
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
16 “Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
Ti, sine èovjeèji, uzmi jedno drvo, i napiši na njemu: Judi i sinovima Izrailjevijem, drugovima njegovijem. Pa onda uzmi drugo drvo, i na njemu napiši: Josifu drvo Jefremovo i svega doma Izrailjeva, drugova njegovijeh.
17 Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
I sastavi ih jedno s drugim da budu kao jedno u tvojoj ruci.
18 “Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
I kad ti reku sinovi tvoga naroda govoreæi: hoæeš li nam kazati šta ti je to?
19 iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
Reci im: ovako veli Gospod Gospod: evo, ja æu uzeti drvo Josifovo, što je u Jefremovoj ruci, i plemena Izrailjevijeh, drugova njegovijeh, i sastaviæu ga s drvetom Judinijem, i naèiniæu od njih jedno drvo, i biæe jedno u mojoj ruci.
20 Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
I drveta, na kojima napišeš, neka ti budu u ruci pred njima.
21 udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
I reci im: ovako veli Gospod Gospod: evo, ja æu uzeti sinove Izrailjeve iz naroda u koje otidoše, i sabraæu ih otsvuda, i dovešæu ih u zemlju njihovu.
22 Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
I naèiniæu od njih jedan narod u zemlji, na gorama Izrailjevijem, i jedan æe car biti car svjema njima, niti æe više biti dva naroda, niti æe više biti razdijeljeni u dva carstva.
23 Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
I neæe se više skvrniti gadnijem bogovima svojim ni gnusobama svojim niti kakijem prijestupima svojim, i izbaviæu ih iz svijeh stanova njihovijeh u kojima griješiše, i oèistiæu ih, i oni æe mi biti narod i ja æu im biti Bog.
24 “‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
I sluga moj David biæe im car, i svi æe imati jednoga pastira, i hodiæe po mojim zakonima, i uredbe æe moje držati i izvršivati.
25 Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
I sjedjeæe u zemlji koju dadoh sluzi svojemu Jakovu, u kojoj sjedješe oci vaši; u njoj æe sjedjeti oni i sinovi njihovi i sinovi sinova njihovijeh dovijeka, i David sluga moj biæe im knez dovijeka.
26 Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
I uèiniæu s njima zavjet mirni, biæe vjeèan zavjet s njima, i utvrdiæu ih i umnožiæu ih, i namjestiæu svetinju svoju usred njih navijek.
27 Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
I šator æe moj biti kod njih, i ja æu im biti Bog i oni æe mi biti narod.
28 Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”
I narod æe poznati da sam ja Gospod koji posveæujem Izrailja, kad svetinja moja bude usred njih dovijeka.

< Ezekieli 37 >