< Ezekieli 21 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
I doðe mi rijeè Gospodnja govoreæi:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
Sine èovjeèji, okreni lice svoje prema Jerusalimu, i pokaplji prema svetijem mjestima, i prorokuj protiv zemlje Izrailjeve.
3 Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
I reci zemlji Izrailjevoj: ovako veli Gospod: evo me na te; izvuæi æu maè svoj iz korica, i istrijebiæu iz tebe pravednoga i bezbožnoga.
4 Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
Da istrijebim iz tebe pravednoga i bezbožnoga, zato æe izaæi maè moj iz korica svojih na svako tijelo od juga do sjevera.
5 Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
I poznaæe svako tijelo da sam ja Gospod izvukao maè svoj iz korica njegovijeh, neæe se više vratiti.
6 “Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
A ti, sine èovjeèji, uzdiši kao da su ti bedra polomljena, i gorko uzdiši pred njima.
7 Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
A kada ti reku: zašto uzdišeš? ti reci: za glas što ide, od kojega æe se rastopiti svako srce i klonuti sve ruke i svakoga æe duha nestati, i svaka æe koljena postati kao voda; evo, ide, i navršiæe se, govori Gospod Gospod.
8 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Potom doðe mi rijeè Gospodnja govoreæi:
9 “Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
Sine èovjeèji, prorokuj i reci: ovako veli Gospod Gospod: reci: maè, maè je naoštren, i uglaðen je.
10 Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
Naoštren je da kolje, uglaðen je da sijeva; hoæemo li se radovati kad prut sina mojega ne haje ni za kako drvo?
11 “‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
Dao ga je da se ugladi da se uzme u ruku; maè je naoštren i uglaðen, da se da u ruku ubici.
12 Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
Vièi i ridaj, sine èovjeèji; jer on ide na narod moj, na sve knezove Izrailjeve; pod maè æe biti okrenuti s narodom mojim, zato udri se po bedru.
13 “‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
Kad bješe karanje, šta bi? eda li ni od pruta koji ne haje neæe biti ništa? govori Gospod Gospod.
14 “Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
Ti dakle, sine èovjeèji, prorokuj i pljeskaj rukama, jer æe maè doæi i drugom i treæom, maè koji ubija, maè koji velike ubija, koji prodire u klijeti.
15 Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
Da se rastope srca i umnoži pogibao, metnuo sam na sva vrata njihova strah od maèa; jaoh! pripravljen je da sijeva, naoštren da kolje.
16 Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
Stegni se, udri nadesno, nalijevo, kuda se god obrneš.
17 Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
Jer æu i ja pljeskati rukama, i namiriæu gnjev svoj. Ja Gospod rekoh.
18 Yehova anandiyankhulanso kuti,
Još mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
19 “Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
A ti, sine èovjeèji, naèini dva puta, kuda æe doæi maè cara Vavilonskoga; iz jedne zemlje neka izlaze oba; i izberi stranu, gdje se poèinje put gradski, izberi.
20 Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
Naèini put, kojim æe doæi maè na Ravu sinova Amonovijeh, i u Judeju na tvrdi Jerusalim.
21 Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
Jer æe car Vavilonski stati na rasputici, gdje poèinju dva puta, te æe vraèati, gladiæe strijele, pitaæe likove, gledaæe u jetru.
22 Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
Nadesno æe mu vraèanje pokazati Jerusalim da namjesti ubojne sprave, da otvori usta na klanje, da podigne glas podvikujuæi, da namjesti ubojne sprave prema vratima, da naèini opkope, da pogradi kule.
23 Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
I uèiniæe se vraèanje zaludno zakletima, a to æe napomenuti bezakonje da se uhvate.
24 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
Zato ovako veli Gospod Gospod: što napominjete svoje bezakonje, te se otkriva nevjera vaša i grijesi se vaši vide u svijem djelima vašim, zato što doðoste na pamet, biæete pohvatani rukom.
25 “‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
A ti, neèisti bezbožnièe, kneže Izrailjev, kome doðe dan kad bi na kraju bezakonje,
26 Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
Ovako veli Gospod Gospod: skini tu kapu i svrzi taj vijenac, neæe ga biti; niskoga æu uzvisiti a visokoga æu poniziti.
27 Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
Uništiæu, uništiæu, uništiæu ga, i neæe ga biti, dokle ne doðe onaj kome pripada, i njemu æu ga dati.
28 “Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
A ti, sine èovjeèji, prorokuj i reci: ovako veli Gospod Gospod za sinove Amonove i za njihovu sramotu; reci dakle: maè, maè je izvuèen, uglaðen da kolje, da zatire, da sijeva,
29 Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
Dokle ti viðaju taštinu, dokle ti gataju laž, da te metnu na vratove pobijenijem bezbožnicima, kojima doðe dan kad bi kraj bezakonju.
30 “‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
Ostavi maè u korice; na mjestu gdje si se rodio, u zemlji gdje si postao, sudiæu ti;
31 Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
I izliæu na te gnjev svoj, ognjem gnjeva svojega dunuæu na te i predaæu te u ruke žestokim ljudma, vještim u zatiranju.
32 Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”
Ognju æeš biti hrana, krv æe ti biti posred zemlje, neæeš se spominjati, jer ja Gospod rekoh.

< Ezekieli 21 >