< Ezekieli 20 >

1 Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
A sedme godine, petoga mjeseca, dana desetoga, doðoše neki od starješina Izrailjevijeh da upitaju Gospoda, i sjedoše preda mnom.
2 Tsono Yehova anandiyankhula nati:
I doðe mi rijeè Gospodnja govoreæi:
3 “Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
Sine èovjeèji, kaži starješinama Izrailjevijem i reci im: ovako veli Gospod Gospod: doðoste li da me pitate? Tako ja živ bio, neæete me pitati, govori Gospod Gospod.
4 “Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
Hoæeš li da im sudiš? hoæeš li da im sudiš? sine èovjeèji. Pokaži im gadove otaca njihovijeh.
5 ‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
I reci im: ovako veli Gospod Gospod: kojega dana izabrah Izrailja i podigoh ruku svoju sjemenu doma Jakovljeva, i pokazah im se u zemlji Misirskoj, i podigoh im ruku svoju govoreæi: ja sam Gospod Bog vaš;
6 Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
Onoga dana podigoh im ruku svoju da æu ih odvesti iz zemlje Misirske u zemlju koju sam pronašao za njih, gdje teèe mlijeko i med, koja je dika svijem zemljama.
7 Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
I rekoh im: odbacite svaki gadove ispred svojih oèiju, i nemojte se skvrniti o gadne bogove Misirske, ja sam Gospod Bog vaš.
8 “‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
Ali se odvrgoše od mene, i ne htješe me poslušati, nijedan ih ne odbaci gadova ispred oèiju svojih, i gadnijeh bogova Misirskih ne ostaviše; zato rekoh da æu izliti jarost svoju na njih da izvršim gnjev svoj na njima usred zemlje Misirske.
9 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
Ali imena svojega radi, da se ne oskvrni pred onijem narodima meðu kojima bijahu, pred kojima im se pokazah, uèinih da ih izvedem iz zemlje Misirske.
10 Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
I izvedoh ih iz zemlje Misirske, i dovedoh ih u pustinju.
11 Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
I dadoh im uredbe svoje, i objavih im zakone svoje, koje ko vrši živ æe biti kroz njih.
12 Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
I subote svoje dadoh im da su znak izmeðu mene i njih da bi znali da sam ja Gospod koji ih posveæujem.
13 “‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
Ali se odvrže od mene dom Izrailjev u pustinji; ne hodiše po mojim uredbama, i zakone moje odbaciše, koje ko vrši živi kroz njih, i subote moje grdno oskvrniše; zato rekoh da æu izliti gnjev svoj na njih u pustinji da ih istrijebim.
14 Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
Ali uèinih imena svojega radi da se ne oskvrni pred narodima pred kojima ih izvedoh.
15 Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
I ja im još podigoh ruku svoju u pustinji da ih neæu odvesti u zemlju koju im dadoh, gdje teèe mlijeko i med, koja je dika svijem zemljama;
16 Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
Jer odbaciše moje zakone i po uredbama mojim ne hodiše, i subote moje oskvrniše, jer srce njihovo iðaše za gadnijem bogovima njihovijem.
17 Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
Ali ih požali oko moje, te ih ne istrijebih, i ne zatrh ih u pustinji.
18 Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
Nego rekoh sinovima njihovijem u pustinji: ne idite po uredbama otaca svojih i ne držite njihovijeh zakona, i ne skvrnite se gadnijem bogovima njihovijem.
19 Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
Ja sam Gospod Bog vaš, po mojim uredbama hodite, i moje zakone držite i izvršujte;
20 Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
I subote moje svetkujte da su znak izmeðu mene i vas, da znate da sam ja Gospod Bog vaš.
21 “‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
Ali se odvrgoše od mene i sinovi, ne hodiše po mojim uredbama, i zakona mojih ne držaše da ih izvršuju, koje ko vrši živi kroz njih; subote moje oskvrniše; zato rekoh da æu izliti jarost svoju na njih i navršiti gnjev svoj na njima u pustinji.
22 Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
Ali povratih ruku svoju i uèinih imena svojega radi da se ne oskvrni pred narodima pred kojima ih izvedoh.
23 Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
I ja im još podigoh ruku svoju u pustinji da æu ih rasijati po narodima i razasuti po zemljama.
24 chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
Jer zakona mojih ne izvršivaše i uredbe moje odbaciše i subote moje oskvrniše, i oèi im gledahu za gadnijem bogovima otaca njihovijeh.
25 Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
Zato im i ja dadoh uredbe ne dobre i zakone kroz koje neæe živjeti.
26 Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
I oskvrnih ih darovima njihovijem što propuštahu kroz oganj sve što otvori matericu, da ih potrem, da poznadu da sam ja Gospod.
27 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
Zato govori domu Izrailjevu, sine èovjeèji, i kaži im: ovako veli Gospod Gospod: još me i ovijem ružiše oci vaši èineæi mi bezakonje:
28 Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
Kad ih odvedoh u zemlju, za koju podigoh ruku svoju da æu im je dati, gdje god vidješe visok hum i drvo granato, ondje prinosiše svoje žrtve i stavljaše svoje dare, kojima dražahu, i metaše mirise svoje ugodne, i ondje ljevaše naljeve svoje.
29 Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
I rekoh im: šta je visina, na koju idete? I opet se zove visina do danas.
30 “Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
Zato reci domu Izrailjevu: ovako veli Gospod Gospod: ne skvrnite li se na putu otaca svojih? i za gadovima njihovijem ne kurvate li se?
31 Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
I prinoseæi dare svoje, provodeæi sinove svoje kroz oganj ne skvrnite li se o sve gadne bogove svoje do danas, i mene li æete pitati, dome Izrailjev? Tako ja živ bio, govori Gospod Gospod, neæete me pitati.
32 “‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
A šta mislite, neæe biti nikako, što govorite: biæemo kao narodi, kao plemena po zemljama, služeæi drvetu i kamenu.
33 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
Tako ja bio živ, govori Gospod Gospod, rukom krjepkom i mišicom podignutom i izlivenijem gnjevom carovaæu nad vama.
34 Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
I izvešæu vas iz naroda, i sabraæu vas iz zemalja po kojima ste rasijani, rukom krjepkom i mišicom podignutom i izlivenijem gnjevom.
35 Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
I odvešæu vas u pustinju tijeh naroda, i ondje æu se suditi s vama licem k licu.
36 Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
Kako sam se sudio s ocima vašim u pustinji zemlje Misirske, tako æu se suditi s vama, govori Gospod Gospod.
37 Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
I propustiæu vas ispod štapa i dovesti vas u sveze zavjetne.
38 Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I odluèiæu izmeðu vas odmetnike i koji odustaju mene; izvešæu ih iz zemlje gdje su došljaci, ali neæe uæi u zemlju Izrailjevu, i poznaæete da sam ja Gospod.
39 “‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
Vi dakle, dome Izrailjev, ovako veli Gospod Gospod: idite, služite svaki gadnijem bogovima svojim i unapredak, kad neæete da me slušate; ali imena mojega svetoga ne skvrnite više darovima svojim i gadnijem bogovima svojim.
40 Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
Jer na mojoj gori svetoj, na visokoj gori Izrailjevoj, govori Gospod Gospod, ondje æe mi služiti sav dom Izrailjev, koliko ih god bude u zemlji, ondje æe mi biti mili i ondje æu iskati prinose vaše i prvine od darova vaših sa svijem svetijem stvarima vašim.
41 Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
Mili æete mi biti s ugodnijem mirisom, kad vas izvedem iz naroda i saberem vas iz zemalja u koje ste rasijani; i biæu posveæen u vama pred narodima.
42 Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
I poznaæete da sam ja Gospod kad vas dovedem u zemlju Izrailjevu, u zemlju za koju podigoh ruku svoju da æu je dati ocima vašim.
43 Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
I ondje æete se opomenuti putova svojih i svijeh djela svojih, kojima se oskvrniste, i sami æete sebi biti mrski za sva zla svoja koja èiniste.
44 Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
I poznaæete da sam ja Gospod kad vam uèinim radi imena svojega; ne po vašim zlijem putovima niti po opakim djelima vašim, dome Izrailjev, govori Gospod Gospod.
45 Yehova anandiyankhula nati:
Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
46 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
Sine èovjeèji, okreni lice svoje na jug i pokaplji prema jugu, i prorokuj na šumu u južnom polju.
47 Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
I reci šumi južnoj: èuj rijeè Gospodnju, ovako veli Gospod Gospod: evo ja æu raspaliti u tebi oganj koji æe proždrijeti u tebi svako drvo zeleno i svako drvo suho; plamen razgorjeli neæe se ugasiti, i izgorjeæe od njega sve od juga do sjevera.
48 Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
I svako æe tijelo vidjeti da sam ja zapalio; neæe se ugasiti.
49 Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”
A ja rekoh: jaoh Gospode Gospode, oni govore za me: ne govori li taj same prièe?

< Ezekieli 20 >