< Ezekieli 2 >

1 Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.”
And he seide to me, Thou, sone of man, stonde on thi feet, and Y schal speke with thee.
2 Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.
And the spirit entride in to me, after that he spak to me, and settide me on my feet. And Y herde oon spekynge to me,
3 Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino.
and seiynge, Sone of man, Y sende thee to the sones of Israel, to folkis apostatas, `ether goynge a bak fro feith, that yeden awei fro me; the fadris of hem braken my couenaunt til to this dai.
4 Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.
And the sones ben of hard face, and of vnchastisable herte, to whiche Y sende thee. And thou schalt seie to hem, The Lord God seith these thingis;
5 Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo.
if perauenture nameli thei heren, and if perauenture thei resten, for it is an hous terrynge to wraththe. And thei schulen wite, that a profete is in the myddis of hem.
6 Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu.
Therfore thou, sone of man, drede not hem, nether drede thou the wordis of hem; for vnbileueful men and distrieris ben with thee, and thou dwellist with scorpiouns. Drede thou not the wordis of hem, and drede thou not the faces of hem, for it is an hous terrynge to wraththe.
7 Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu.
Therfor thou schalt speke my wordis to hem, if perauenture thei heren, and resten, for thei ben terreris to wraththe.
8 Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”
But thou, sone of man, here what euer thingis Y schal speke to thee; and nyle thou be a terrere to wraththe, as the hows of Israel is a terrere to wraththe. Opene thi mouth, and ete what euer thingis Y yyue to thee.
9 Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa.
And Y siy, and lo! an hond was sent to me, in which a book was foldid togidere.
10 Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.
And he spredde abrood it bifor me, that was writun with ynne and with outforth. And lamentaciouns, and song, and wo, weren writun ther ynne.

< Ezekieli 2 >