< Ezekieli 18 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
And the word of the Lord was maad to me,
2 “Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
and he seide, What is it, that ye turnen a parable among you in to this prouerbe, in the lond of Israel, and seien, Fadris eeten a bittir grape, and the teeth of sones ben an egge, ether astonyed?
3 “Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
Y lyue, seith the Lord God, this parable schal no more be in to a prouerbe to you in Israel.
4 Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
Lo! alle soulis ben myne; as the soule of the fadir, so and the soule of the sone is myn. Thilke soule that doith synne, schal die.
5 “Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
And if a man is iust, and doith doom and riytfulnesse,
6 Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
etith not in hillis, and reisith not hise iyen to the idols of the hous of Israel; and defoulith not the wijf of his neiybore, and neiyeth not to a womman defoulid with vncleene blood;
7 Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
and makith not a man sori, yeldith the wed to the dettour, rauyschith no thing bi violence, yyueth his breed to the hungri, and hilith a nakid man with a cloth;
8 Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
leeneth not to vsure, and takith not more; turneth awei his hond fro wickidnesse, and makith trewe dom bitwixe man and man;
9 Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
and goith in my comaundementis, and kepith my domes, that he do treuthe; this is a iust man, he schal lyue in lijf, seith the Lord God.
10 “Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
That if he gendrith a sone, a theef, shedinge out blood,
11 Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
and doith oon of thes thingis, and sotheli not doing alle these thingis, but etinge in hillis, and defoulynge the wijf of his neiybore;
12 Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
makynge soreuful a nedy man and pore, rauyschynge raueyns, not yeldinge a wed, reisynge hise iyen to idols, doynge abhomynacioun; yiuynge to vsure, and takynge more;
13 Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
whether he schal lyue? he schal not lyue; whanne he hath do alle these abhomynable thingis, he schal die bi deth, his blood schal be in hym.
14 “Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
That if he gendrith a sone, which seeth alle the synnes of his fadir, whiche he dide, and dredith, and doith noon lijk tho;
15 “Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
etith not on hillis, and reisith not hise iyen to the idols of the hous of Israel; and defoulith not the wijf of his neiybore,
16 Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
and makith not sori a man, witholdith not a wed, and rauyschith not raueyn, yyueth his breed to the hungri, and hilith the nakid with a cloth;
17 Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
turneth a wei his hond fro the wrong of a pore man, takith not vsure and ouerhabundaunce, `that is, no thing more than he lente, and doith my domes, and goith in my comaundementis; this sone schal not die in the wickidnesse of his fadir, but he schal lyue in lijf.
18 Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
For his fadir made fals caleng, and dide violence to his brother, and wrouyte yuel in the myddis of his puple, lo! he is deed in his wickidnesse.
19 “Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
And ye seien, Whi berith not the sone the wickidnesse of the fadir? That is to seie, for the sone wrouyte doom and riytfulnesse, he kepte alle my comaundementis, and dide tho, he schal lyue in lijf.
20 Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
Thilke soule that doith synne, schal die; the sone schal not bere the wickidnesse of the fadir, and the fadir schal not bere the wickednesse of the sone; the riytfulnesse of a iust man schal be on hym, and the wickidnesse of a wickid man schal be on hym.
21 “‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
Forsothe if a wickid man doith penaunce of alle hise synnes whiche he wrouyte, and kepith alle myn heestis, and doith dom and riytfulnesse, he schal lyue bi lijf, and schal not die.
22 Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
Y schal not haue mynde of alle his wickidnessis whiche he wrouyte; he schal lyue in his riytfulnesse which he wrouyte.
23 Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
Whether the deth of the wickid man is of my wille, seith the Lord God, and not that he be conuertid fro his weies, and lyue?
24 “‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
Forsothe if a iust man turneth awey hym silf fro his riytfulnesse, and doith wickidnesse bi alle hise abhomynaciouns, which a wickid man is wont to worche, whether he schal lyue? Alle hise riytfulnessis whiche he dide, schulen not be had in mynde; in his trespassyng bi which he trespasside, and in his synne which he synnede, he schal die in tho.
25 “Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
And ye seiden, The weie of the Lord is not euene. Therfor, the hous of Israel, here ye, whether my weie is not euene, and not more youre weies ben schrewid?
26 Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
For whanne a riytful man turneth awei hym silf fro his riytfulnesse, and doith wickidnesse, he schal die in it, he schal die in the vnriytwisnesse which he wrouyte.
27 Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
And whanne a wickid man turneth awei him silf fro his wickidnesse which he wrouyte, and doith dom and riytfulnesse, he schal quykene his soule.
28 Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
For he biholdinge and turnynge awei hym silf fro alle hise wickidnessis which he wrouyte, schal lyue in lijf, and schal not die.
29 Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
And the sones of Israel seien, The weie of the Lord is not euene. Whether my weies ben not euene, ye hous of Israel, and not more youre weies ben schrewid?
30 “Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
Therfor, thou hous of Israel, Y schal deme ech man bi hise weies, seith the Lord God. Turne ye togidere, and do ye penaunce for alle youre wickidnessis, and wickidnesse schal not be to you in to falling.
31 Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
Caste awei fro you alle youre trespassingis, bi whiche ye trespassiden, and make ye a newe herte and a newe spirit to you, and whi schulen ye die, the hous of Israel?
32 Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”
For Y nyle the deeth of hym that dieth, seith the Lord God; turne ye ayen, and lyue ye.

< Ezekieli 18 >