< Deuteronomo 33 >

1 Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe.
A ovo je blagoslov kojim blagoslovi Mojsije èovjek Božji sinove Izrailjeve pred smrt svoju.
2 Iye anati: “Yehova anabwera kuchokera ku Sinai ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri; anawala kuchokera pa Phiri la Parani. Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.
I reèe: Gospod izide sa Sinaja, i pokaza im se sa Sira; zasja s gore Faranske, i doðe s mnoštvom tisuæa svetaca, a u desnici mu zakon ognjeni za njih.
3 Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu; opatulika ake onse ali mʼmanja mwake. Onse amagwada pansi pa mapazi anu kuchokera kwa inu amalandira malangizo,
Doista ljubi narode; svi su sveti njegovi u ruci tvojoj; i oni se slegoše k nogama tvojim da prime rijeèi tvoje.
4 malamulo amene Mose anatipatsa, chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.
Mojsije nam dade zakon, našljedstvo zboru Jakovljevu.
5 Iye anali mfumu ya Yesuruni pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, pamodzi ndi mafuko a Israeli.
Jer bijaše car u Izrailju, kad se sabirahu knezovi narodni, plemena Izrailjeva.
6 “Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe, anthu ake asachepe pa chiwerengero.”
Da živi Ruvim i ne umre, a ljudi njegovijeh da bude malo!
7 Ndipo ponena za Yuda anati: “Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda; mubweretseni kwa anthu ake. Ndi manja ake omwe adziteteze yekha. Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”
A za Judu reèe: usliši Gospode glas Judin, i dovedi ga opet k narodu njegovu; ruke njegove neka vojuju za nj, a ti mu pomaži protiv neprijatelja njegovijeh.
8 Za fuko la Alevi anati: “Tumimu wanu ndi Urimu ndi za mtumiki wanu wokhulupirika. Munamuyesa ku Masa; munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.
I za Levija reèe: tvoj Tumim i tvoj Urim neka budu u èovjeka tvojega svetoga, kojega si okušao u Masi i s kojim si se prepirao na vodi Merivi;
9 Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti, ‘Sindilabadira za iwo.’ Sanasamale za abale ake kapena ana ake, koma anayangʼanira mawu anu ndipo anateteza pangano lanu.
Koji reèe ocu svojemu i materi svojoj: ne gledam na vas; koji ne poznaje braæe svoje i za sinove svoje ne zna; jer drže rijeèi tvoje, i zavjet tvoj èuvaju.
10 Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu ndi malamulo anu kwa Israeli. Amafukiza lubani pamaso panu ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.
Oni uèe uredbama tvojim Jakova i zakonu tvojemu Izrailja, i meæu kad pod nozdrve tvoje i žrtvu što se sažiže na oltar tvoj.
11 Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake. Menyani adani awo mʼchiwuno kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”
Blagoslovi, Gospode, vojsku njegovu, i neka ti milo bude djelo ruku njegovijeh; polomi bedre onima koji ustaju na nj i koji mrze na nj, da ne ustanu.
12 Za fuko la Benjamini anati: “Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye, pakuti amamuteteza tsiku lonse, ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”
Za Venijamina reèe: mili Gospodu nastavaæe bez straha s njim; zaklanjaæe ga svaki dan, i meðu pleæima njegovijem nastavaæe.
13 Za fuko la Yosefe anati: “Yehova adalitse dziko lake ndi mame ambiri ochokera kumwamba ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;
I za Josifa reèe: blagoslovena je zemlja njegova od Gospoda blagom s neba, rosom, i iz dubine ozdo,
14 ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;
I blagom koje dolazi od sunca, i blagom koje dolazi od mjeseca,
15 ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;
I blagom starijeh brda i blagom vjeènijeh humova,
16 ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto. Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe, wapaderadera pakati pa abale ake.
I blagom na zemlji i obiljem njezinijem, i milošæu onoga koji stoji u kupini. Neka to doðe na glavu Josifu i na tjeme odvojenome izmeðu braæe svoje.
17 Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa; nyanga zake zili ngati za njati. Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina, ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi. Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu; nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”
Krasota je njegova kao u prvenca teleta, i rogovi njegovi kao rogovi u jednoroga; njima æe bosti narode sve do kraja zemlje; to je mnoštvo tisuæa Jefremovijeh i tisuæe Manasijine.
18 Za fuko la Zebuloni anati: “Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka, ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.
A za Zavulona reèe: veseli se Zavulone izlaskom svojim, i Isahare šatorima svojim.
19 Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri, kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo; kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja, chuma chobisika mu mchenga.”
Narode æe sazvati na goru, ondje æe prinijeti žrtve pravedne; jer æe obilje morsko sisati i sakriveno blago u pijesku.
20 Za fuko la Gadi anati: “Wodala amene amakulitsa malire a Gadi! Gadi amakhala kumeneko ngati mkango, kukhadzula mkono kapena mutu.
A za Gada reèe: blagosloven je koji širi Gada; on nastava kao lav, i kida ruku i glavu.
21 Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri; gawo la mtsogoleri anasungira iye. Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana, anachita chifuniro cha Yehova molungama, ndiponso malamulo onena za Israeli.”
Izabra sebi prvo, jer ondje dobi dio od onoga koji dade zakon; zato æe iæi s knezovima narodnijem, i izvršivati pravdu Gospodnju i sudove njegove s Izrailjem.
22 Za fuko la Dani anati: “Dani ndi mwana wamkango, amene akutuluka ku Basani.”
A za Dana reèe: Dan je laviæ, koji æe iskakati iz Vasana.
23 Za fuko la Nafutali anati: “Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake; cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”
I za Neftalima reèe: Neftalime, siti milosti i puni blagoslova Gospodnjega, zapad i jug uzmi.
24 Za fuko la Aseri anati: “Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri; abale ake amukomere mtima, ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.
I za Asira reèe: Asir æe biti blagosloven mimo druge sinove, biæe mio braæi svojoj, zamakaæe u ulje nogu svoju.
25 Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa, ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.
Gvožðe i mjed biæe pod obuæom tvojom; i dokle traju dani tvoji trajaæe snaga tvoja.
26 “Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni, amene amakwera pa thambo kukuthandizani ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.
Izrailju! niko nije kao Bog, koji ide po nebu tebi u pomoæ, i u velièanstvu svojem na oblacima.
27 Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu, ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha. Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu, adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’
Zaklon je Bog vjeèni i pod mišicom vjeènom; on æe odagnati ispred tebe neprijatelje tvoje, i reæi æe: zatri!
28 Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere; zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano, kumene thambo limagwetsa mame.
Da bi nastavao Izrailj sam bezbrižno, izvor Jakovljev, u zemlji obilnoj žitom i vinom; i nebo æe njegovo kropiti rosom.
29 Iwe Israeli, ndiwe wodala! Wofanana nanu ndani anthu opulumutsidwa ndi Yehova? Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu ndi lupanga lanu la ulemerero. Adani ako adzakugonjera, ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”
Blago tebi, Izrailju! ko je kao ti, narod kojega je saèuvao Gospod, štit pomoæi tvoje, i maè slave tvoje? Neprijatelji æe se tvoji poniziti, a ti æeš gaziti visine njihove.

< Deuteronomo 33 >