< Deuteronomo 25 >

1 Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa.
Kad je raspra meðu ljudima, pa doðu na sud da im sude, tada pravoga neka opravdaju a krivoga neka osude.
2 Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake,
I ako krivi zaslužuje boj, tada sudija neka zapovjedi da ga povale i biju pred njim, na broj prema krivici njegovoj.
3 koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.
Do èetrdeset udaraca neka zapovjedi da mu udare, ne više, da se ne bi poništio brat tvoj u tvojim oèima, kad bi mu se udarilo više udaraca.
4 Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.
Nemoj zavezati usta volu kad vrše.
5 Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo.
Kad braæa žive zajedno pa umre jedan od njih bez djece, onda žena umrloga da se ne uda iz kuæe za drugoga; brat njegov neka otide k njoj i uzme je za ženu i uèini joj dužnost djeversku.
6 Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.
I prvi sin kojega ona rodi neka se nazove imenom brata njegova umrloga, da ne pogine ime njegovo u Izrailju.
7 Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.”
Ako li onaj èovjek ne bi htio uzeti snahe svoje, onda snaha njegova neka doðe na vrata pred starješine, i reèe: neæe djever moj da podigne bratu svojemu sjemena u Izrailju, neæe da mi uèini dužnosti djeverske.
8 Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,”
Tada neka ga dozovu starješine mjesta onoga i razgovore se s njim; pa ako se on upre i reèe: neæu da je uzmem;
9 mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.”
Onda neka pristupi k njemu snaha njegova pred starješinama, i neka mu izuje obuæu s noge njegove i pljune mu u lice, i progovorivši neka reèe: tako valja da bude èovjeku koji neæe da zida kuæe brata svojega.
10 Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.
I on neka se zove u Izrailju: dom bosoga.
11 Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo,
Ako bi se svadili ljudi, jedan s drugim, pa bi došla žena jednoga da otme muža svojega iz ruke drugoga koji ga bije, i pruživši ruku svoju uhvatila bi ga za mošnice,
12 muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.
Otsijeci joj ruku; neka ne žali oko tvoje.
13 Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka.
Nemoj imati u torbi svojoj dvojaku mjeru, veliku i malu.
14 Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono.
Nemoj imati u kuæi svojoj dvojaku efu, veliku i malu.
15 Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Mjera potpuna i prava neka ti je; efa potpuna i prava neka ti je, da bi ti se produljili dani tvoji u zemlji koju ti daje Gospod Bog tvoj.
16 Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.
Jer je gad pred Gospodom Bogom tvojim ko god èini tako, ko god èini krivo.
17 Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto.
Opominji se šta ti je uèinio Amalik na putu kad iðaste iz Misira,
18 Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu.
Kako te doèeka na putu i pobi na kraju sve umorne koji iðahu za tobom, kad si bio sustao i iznemogao, i ne boja se Boga.
19 Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!
Zato kad te Gospod Bog tvoj smiri od svijeh neprijatelja tvojih unaokolo u zemlji koju ti daje Gospod Bog tvoj da je naslijediš, tada zatri spomen Amaliku pod nebom; ne zaboravi.

< Deuteronomo 25 >