< Deuteronomo 22 >

1 Ngati uwona ngʼombe kapena nkhosa ya mʼbale wako ikusochera, usayilekerere koma uyesetse kuyibwezera kwa iye.
Kad vidiš vola ili ovcu brata svojega gdje luta, nemoj proæi mimo njih, nego ih odvedi bratu svojemu.
2 Ngati mʼbale wakoyo sakhala pafupi kapena sukudziwa kuti ndi yandani, uyitengere ku nyumba kwako ndi kuyisamala mpaka mwini wake atayilondola ndipo umubwezere.
Ako li ti brat tvoj nije blizu ili ga ne znaš, odvedi ih svojoj kuæi neka budu kod tebe dokle ih ne potraži brat tvoj, i tada mu ih vrati.
3 Uzitero ndithu ngati upeza bulu kapena mkanjo kapena chilichonse chimene chatayika. Osachilekerera.
Tako uèini i s magarcem njegovijem i s haljinom njegovom; i tako uèini sa svakom stvarju brata svojega izgubljenom, kad je izgubi a ti je naðeš, nemoj proæi mimo nju.
4 Ngati wapeza bulu kapena ngʼombe ya mʼbale wako itagwa panjira, usayilekerere. Ithandize kuti idzuke.
Kad vidiš magarca ili vola brata svojega gdje je pao na putu, nemoj ih proæi, nego ih podigni s njim.
5 Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi.
Žena da ne nosi muškoga odijela niti èovjek da se oblaèi u ženske haljine, jer je gad pred Gospodom Bogom tvojim ko god tako èini.
6 Ukapeza chisa cha mbalame mʼmphepete mwa msewu, kaya ndi mu mtengo kapena pansi, mbalame yayikazi itafungatira ana kapena mazira, usatenge mbalameyo pamodzi ndi ana ake omwe.
Kad naiðeš putem na gnijezdo ptièije, na drvetu ili na zemlji, sa ptiæima ili sa jajcima, a majka leži na ptiæima ili na jajcima, nemoj uzeti majke s ptiæima.
7 Anawo mukhoza kutenga koma onetsetsani kuti mayi wawo mwamutaya kuti apite, kuti zinthu zizikuyenderani bwino ndiponso kuti mukhale ndi moyo wautali.
Nego pusti majku a ptiæe uzmi, da bi ti dobro bilo i da bi ti se produljili dani.
8 Mukamanga nyumba yatsopano, mutchingire khonde lake la pa denga kuti inu musapezeke ndi mlandu wopha munthu ngati wina agwa kuchokera pa khonde la pa dengalo.
Kad gradiš novu kuæu, naèini ogradu oko strehe svoje, da ne bi navukao krvi na dom svoj, kad bi ko pao s njega.
9 Musadzale mbewu zamitundu iwiri mʼmunda wanu wa mpesa, ngati mutero, si mbewu zanu zokha zimene zidzakhale zodetsedwa, komanso zipatso za mʼmunda wamphesawo.
Ne sij u vinogradu svojem drugoga sjemena da ne bi oskvrnio i rod od sjemena koje posiješ i rod vinogradski.
10 Musatipule pogwiritsa ntchito ngʼombe ndi bulu pa goli limodzi.
Ne ori na volu i na magarcu zajedno.
11 Musamavale chovala chopangidwa mophatikiza ubweya ndi thonje.
Ne oblaèi haljine tkane od vune i od lana zajedno.
12 Muzipanga mphonje mʼngodya za mkanjo umene mumavala.
Naèini sebi rese na èetiri kraja od haljine koju oblaèiš.
13 Ngati munthu akwatira mkazi, ndipo atagona naye nʼkusamufunanso
Ko se oženi, pa mu žena omrzne pošto legne s njom,
14 namunyoza ndi kumuyipitsira dzina nʼkumati, “Ine ndinakwatira mkazi uyu, koma pamene ndinakhala naye, sindinachione chizindikiro cha unamwali wake,”
Pa da priliku da se govori o njoj i prospe rðav glas o njoj govoreæi: oženih se ovom, ali legavši s njom ne naðoh u nje djevojaštva;
15 zikatero abambo ndi amayi ake ayenera kubweretsa chitsimikizo chakuti anali namwali kwa akuluakulu a mzinda ku chipata.
Tada otac djevojèin i mati neka uzmu i donesu znake djevojaštva njezina pred starješine grada svojega na vrata,
16 Abambo ake a mtsikanayo adzanene kwa akuluakuluwo kuti, “Ine ndinamupatsa munthu uyu mwana wanga wamkazi kuti amukwatire, koma sakumufunanso.
I neka reèe otac djevojèin starješinama: ovu kæer svoju dadoh ovomu èovjeku za ženu, a on mrzi na nju,
17 Tsopano wamunyoza ndipo wanena kuti, ‘Ine sindinapeze kuti mwana wanu wamkaziyu ndi namwali.’ Koma tsopano onani chitsimikizo ichi cha unamwali wa mwana wanga wamkazi.” Kenaka makolo a mtsikanayo adzaonetse kansalu kwa akuluakulu aja,
I dade priliku da se govori o njoj rekav: ne naðoh u tvoje kæeri djevojaštva; a evo znaka djevojaštva kæeri moje. I neka razastru haljinu pred starješinama gradskim.
18 ndipo akuluakuluwo adzamugwire munthuyo namupatsa chilango.
Tada starješine grada onoga neka uzmu muža njezina i nakaraju ga,
19 Iwo adzamulipitse ndalama zasiliva zokwana 100 nazipereka kwa abambo a mtsikana, chifukwa munthu uyu wayipitsa dzina la mtsikana wa Chiisraeli. Ayenera kukhalabe mkazi wake ndipo asadzamuleke moyo wake wonse.
I neka ga oglobe sto sikala srebra, koje neka dadu ocu djevojèinu zato što je iznio rðav glas na djevojku Izrailjku, i neka mu bude žena; da je ne može pustiti dok je živ.
20 Koma ngati zomunenerazo ndi zoona, ndipo kuti chitsimikizo cha unamwali wa mtsikanayo sichinapezeke,
Ali ako bude ono istina, da se nije našlo djevojaštvo u djevojke,
21 iyeyu ayenera kumutengera pa khomo pa abambo ake pamene anthu a mu mzinda wake akamuphere ndi miyala. Iyeyo wachita chinthu chochititsa manyazi mu Israeli pochita chiwerewere akanali pa khomo pa abambo ake. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu.
Tada neka izvedu djevojku na vrata oca njezina, i neka je zaspu kamenjem ljudi onoga mjesta da pogine, zato što uèini sramotu u Izrailju kurvavši se u domu oca svojega. Tako izvadi zlo iz sebe.
22 Ngati munthu apezeka akugona ndi mkazi wa mwini wake, ayenera kuphedwa munthuyo pamodzi ndi mkazi yemwe wagona nayeyo. Muyenera kuchotsa zoyipa mu Israeli.
Ako se ko uhvati gdje leži sa ženom udatom, neka se pogube oboje, èovjek koji je ležao sa ženom i žena. Tako izvadi zlo iz Izrailja.
23 Ngati munthu mu mzinda akumana ndi mkazi yemwe anachita kale chinkhoswe nagona naye,
Kad djevojka bude isprošena za koga, pa je naðe kogod u mjestu i obleži je,
24 muwatengere awiriwo ku chipata cha mzinda ndi kuwapha ndi miyala. Aphedwe chifukwa mtsikanayo anali pafupi ndi anthu ndipo sanakuwe kuti ena amuthandize ndipo mwamunayo chifukwa anayipitsa mkazi wa mwini. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
Izvedite ih oboje na vrata onoga mjesta, i zaspite ih kamenjem da poginu, djevojku što nije vikala u mjestu, a èovjeka što je osramotio ženu bližnjega svojega. Tako izvadi zlo iz sebe.
25 Koma ngati munthu akumana ndi mkazi kutchire yemwe anachita kale chinkhoswe namugwiririra, mwamuna yekhayo ndiye woyenera kuphedwa.
Ako li u polju naðe èovjek djevojku isprošenu, i silom je obleži, tada da se pogubi samo èovjek koji je obleža;
26 Mtsikanayo musamuchite chilichonse, palibe tchimo limene wachita loti ayenera kuphedwa. Mlandu uwu ufanana ndi wa munthu amene alimbana ndi kupha mnzake woyandikana naye,
A djevojci ne èini ništa, nije uèinila grijeha koji zaslužuje smrt, jer kao kad ko skoèi na bližnjega svojega i ubije ga, takva je i ta stvar;
27 pakuti mwamunayo anamupeza mtsikanayo kutchire, ndipo ngakhale mtsikana wachinkhosweyo anakuwa, panalibe anamulanditsa.
Jer naðe je u polju, i djevojka isprošena vika, ali ne bi nikoga da je odbrani.
28 Ngati munthu apezana ndi namwali woti sanachite chinkhoswe, namugwiririra, munthuyo nʼkupezeka,
Ako ko naðe djevojku koja nije isprošena i uhvati je i legne s njom, i zateku se,
29 ayenera kuwalipira abambo ake a namwaliyo ndalama za siliva makumi asanu. Iye ayenera kumukwatira mkaziyo chifukwa wamuyipitsa, ndipo sadzamulekanso moyo wake wonse.
Tada èovjek onaj koji je legao s njom da da ocu djevojèinu pedeset sikala srebra, i neka mu ona bude žena zato što je osramoti; da je ne može pustiti dok je živ.
30 Munthu asakwatire mkazi wa abambo ake pakuti ayenera kuchitira ulemu pogona pa abambo ake.
Niko da se ne ženi ženom oca svojega, ni da otkrije skuta oca svojega.

< Deuteronomo 22 >