< Deuteronomo 21 >

1 Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha,
Kad se naðe ubijen èovjek u zemlji koju ti daje Gospod Bog tvoj da je naslijediš, gdje leži u polju, a ne zna se ko ga je ubio,
2 akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira.
Tada neka izidu starješine tvoje i sudije tvoje, i neka izmjere od ubijenoga do gradova koji su oko njega.
3 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli
Pa koji grad bude najbliže ubijenoga, starješine onoga grada neka uzmu junicu iz goveda, na kojoj se još nije radilo, koja nije vukla u jarmu,
4 ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo.
I neka odvedu starješine onoga grada tu junicu u pustu dolinu gdje se ne kopa ni sije, i neka zakolju junicu ondje u dolini.
5 Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana.
Potom neka pristupe sveštenici, sinovi Levijevi; jer njih izabra Gospod Bog tvoj da mu služe i da blagosiljaju u ime Gospodnje, i na njihovijem rijeèima da ostaje svaka raspra i svaka šteta;
6 Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija,
I sve starješine onoga grada koji budu najbliže ubijenoga neka operu ruke svoje nad zaklanom junicom u onoj dolini,
7 nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako.
I tvrdeæi neka reku: ruke naše nijesu prolile ove krvi niti su oèi naše vidjele;
8 Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa.
Milostiv budi narodu svojemu Izrailju, koji si iskupio, Gospode, i ne meæi prave krvi na narod svoj Izrailja. Tako æe se oèistiti od one krvi.
9 Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.
I ti æeš skinuti pravu krv sa sebe kad uèiniš što je pravo pred Gospodom.
10 Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo,
Kad otideš na vojsku na neprijatelje svoje, i preda ih Gospod Bog tvoj u ruke tvoje i zarobiš ih mnogo,
11 ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu.
I ugledaš u roblju lijepu ženu, i omili ti da bi je htio uzeti za ženu,
12 Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake
Odvedi je kuæi svojoj; i neka obrije glavu svoju i sreže nokte svoje;
13 ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu.
I neka skine sa sebe haljine svoje u kojima je zarobljena, i neka sjedi u kuæi tvojoj, i žali za ocem svojim i za materom svojom cio mjesec dana; potom lezi s njom, i budi joj muž i ona nek ti bude žena.
14 Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.
Ako ti poslije ne bi bila po volji, pusti je neka ide kuda joj drago, ali nikako da je ne prodaš za novce ni da njom trguješ, jer si je osramotio.
15 Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo,
Ko bi imao dvije žene, jednu milu a drugu nemilu, pa bi rodile sinove, i mila i nemila, i prvenac bi bio od nemile,
16 akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda.
Onda kad doðe vrijeme da podijeli sinovima svojim što ima, ne može prvencem uèiniti sina od mile preko sina od nemile koji je prvenac;
17 Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.
Nego za prvenca neka prizna sina od nemile i dade mu dva dijela od svega što ima, jer je on poèetak sile njegove, njegovo je pravo prvenaèko.
18 Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza,
Ko bi imao sina samovoljna i nepokorna, koji ne sluša oca svojega ni matere svoje, i kojega oni i karaše pa opet ne sluša,
19 abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo
Neka ga uzmu otac i mati, i neka ga dovedu k starješinama grada svojega na vrata mjesta svojega,
20 akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.”
I neka kažu starješinama grada svojega: ovaj sin naš samovoljan je i nepokoran, ne sluša nas, izjelica je i pijanica.
21 Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.
Tada svi ljudi onoga mjesta neka ga zaspu kamenjem da pogine; i tako izvadi zlo iz sebe, da sav Izrailj èuje i boji se.
22 Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo,
Ko zgriješi tako da zasluži smrt, te bude osuðen na smrt i objesiš ga na drvo,
23 musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.
Neka ne prenoæi tijelo njegovo na drvetu, nego ga isti dan pogrebi, jer je proklet pred Bogom ko je obješen; zato ne skvrni zemlje koju ti Gospod Bog tvoj daje u našljedstvo.

< Deuteronomo 21 >