< Deuteronomo 20 >

1 Pamene mukupita kokachita nkhondo ndi adani anu, mukaona akavalo kapena magaleta kapena gulu la ankhondo kuposa inuyo musamaope chifukwa Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto adzakhala nanu.
Kad otideš na vojsku na neprijatelja svojega i vidiš konje i kola i narod veæi od sebe, nemoj se uplašiti od njih, jer je s tobom Gospod Bog tvoj, koji te je izveo iz zemlje Misirske.
2 Pamene mwatsala pangʼono kuyamba nkhondo, wansembe azibwera kutsogolo ndipo aziyankhula ku gulu lonse lankhondolo.
I kad poðete da se pobijete, neka pristupi sveštenik i progovori narodu,
3 Iye aziti, “Tamverani inu Aisraeli, mukupita kukachita nkhondo ndi adani anu lero. Musataye mitima kapena kuchita mantha ayi. Musaopsedwe kapena kunjenjemera pamaso pawo,
I neka im reèe: slušaj Izrailju! vi polazite danas u boj na neprijatelje svoje, neka ne trne srce vaše, ne bojte se i ne plašite se, niti se prepadajte od njih.
4 pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye amene apite nanu kukakumenyerani nkhondo ndi kugonjetsa adani anu.”
Jer Gospod Bog vaš ide s vama i biæe se za vas s neprijateljima vašim da vas saèuva.
5 Akuluakulu ankhondo adzati kwa gulu la ankhondolo, “Kodi pali wina amene wangomanga nyumba kumene ndipo sanayitsekulire? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondoko ndipo wina ndi kudzayitsekulira.
Potom i vojvode neka progovore narodu, i reku: ko je sagradio novu kuæu a nije poèeo sjedjeti u njoj? neka ide, nek se vrati kuæi svojoj, da ne bi poginuo u boju, i drugi poèeo sjedjeti u njoj.
6 Kodi pali wina amene analima munda wamphesa ndipo sanayambe kudyerera? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzadyerera mundawo.
I ko je posadio vinograd a još ga nije brao? neka ide, nek se vrati kuæi svojoj, da ne bi poginuo u boju, i drugi ga brao.
7 Kodi pali amene wachita chinkhoswe ndi mkazi ndipo sanamukwatire mkaziyo? Ayambe wabwerera ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzakwatira mkaziyo.”
I ko je isprosio djevojku a još je nije odveo? neka ide, nek se vrati kuæi svojoj, da ne bi poginuo u boju, i drugi je odveo.
8 Ndipo akuluakulu ankhondowo akapitirize kuti, “Kodi pali amene akuchita mantha kapena kutaya mtima? Abwerere ku mudzi kuopa kuti abale ake angatayenso mtima.”
Još i ovo neka kažu vojvode narodu i reku: ko je strašiv i trne mu srce? neka ide, nek se vrati kuæi svojoj, da ne bi trnulo srce braæi njegovoj kao njemu.
9 Akuluakuluwo akatsiriza kuyankhula ndi gulu la ankhondolo, adzasankhe olilamulira.
I kad vojvode izgovore narodu, onda neka namjeste glavare od èeta pred narod.
10 Pamene mukuyandikira kuphwanya mzinda, muyambe mwafunsa anthu a mu mzindawo ngati afuna zamtendere.
Kad doðeš pod koji grad da ga biješ, prvo ga ponudi mirom.
11 Akavomera natsekula zipata zawo, anthu wonse mu mzindawo adzagwidwa ukapolo nakugwirirani ntchito.
Ako ti odgovori mirom i otvori ti vrata, sav narod koji se naðe u njemu neka ti plaæa danak i bude ti pokoran.
12 Koma akakana za mtendere nachita nanu nkhondo, muwuphwanye mzindawo.
Ako li ne uèini mira s tobom nego se stane biti s tobom, tada ga bij.
13 Yehova Mulungu wanu akakupatsani mzindawo, muwaphe amuna onse.
I kad ga Gospod Bog tvoj preda u ruke tvoje, pobij sve muškinje u njemu maèem.
14 Akazi, ana, ziweto ndi china chilichonse mu mzindamo, mukhoza kuzitenga kuti zikhale zanu monga katundu wolanda ku nkhondo. Katundu wa adani anuyu amene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, mukhoza kumugwiritsa ntchito.
A žene i djecu i stoku i što god bude u gradu, sav plijen u njemu, otmi, i jedi plijen od neprijatelja svojih, koji ti da Gospod Bog tvoj.
15 Mizinda yonse yakutali osati ya mitundu yapafupi, muzichita nayo chomwechi.
Tako èini sa svijem gradovima, koji su daleko od tebe i nijesu od gradova ovijeh naroda.
16 Komabe mʼmizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, musasiyemo chamoyo chilichonse.
A u gradovima ovijeh naroda, koje ti Gospod Bog tvoj daje u našljedstvo, ne ostavi u životu nijedne duše žive.
17 Muwawononge kwathunthu Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi monga momwe Yehova Mulungu wanu anakulamulirani.
Nego ih zatri sasvijem, Heteje i Amoreje i Hananeje i Ferezeje i Jeveje i Jevuseje, kao što ti je zapovjedio Gospod Bog tvoj.
18 Mukapanda kutero adzakuphunzitsani kuti mutengere zinthu zonyansa zimene amachita popembedza milungu yawo ndipo mudzachimwira Yehova Mulungu wanu.
Da vas ne nauèe èiniti gadna djela koja èiniše bogovima svojim, i da ne zgriješite Gospodu Bogu svojemu.
19 Mukalimbana ndi mzinda nthawi yayitali, kuchita nawo nkhondo pofuna kuwugonjetsa, musawononge podula mitengo yake ndi nkhwangwa, osayidula chifukwa zipatso zakezo mukhoza kudya. Kodi mitengo ya ku munda ndi anthu kuti mukalimbane nayo?
Kad opkoliš kakav grad i budeš dugo pod njim bijuæi ga da bi ga uzeo, ne kvari drveta njegovijeh sjekirom; jer možeš s njih jesti, zato ih ne sijeci; jer drvo poljsko je li èovjek da uðe u grad ispred tebe?
20 Komabe mukhoza kudula mitengo imene mukudziwa kuti si ya zipatso ndi kuyigwiritsa ntchito pa nkhondo mpaka mzinda umene mukumenyana nawowo utagwetsedwa.
Nego drveta koja znaš da im se rod ne jede, njih obaljuj i sijeci i gradi zaklon od grada koji se bije s tobom, dokle ne padne.

< Deuteronomo 20 >