< Deuteronomo 17 >

1 Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.
Ne prinosi Gospodu Bogu svojemu ni vola ni jagnjeta ni jareta na kom ima mana ili kako god zlo; jer je gadno pred Gospodom Bogom tvojim.
2 Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake,
Ako se naðe kod tebe u kojem od mjesta tvojih, koja ti da Gospod Bog tvoj, èovjek ili žena da uèini zlo pred Gospodom Bogom tvojim prestupajuæi zavjet njegov,
3 ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba,
I otide te služi drugim bogovima i klanja im se, ili suncu ili mjesecu ili èemu god iz vojske nebeske, što nijesam zapovjedio,
4 ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli,
I tebi se to javi i ti èuješ, onda raspitaj dobro; pa ako bude istina i doista se uèinila ona gadna stvar u Izrailju,
5 mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala.
Izvedi onoga èovjeka ili onu ženu, koji uèiniše ono zlo, na vrata svoja, èovjeka onoga ili ženu, i zaspi ih kamenjem da poginu.
6 Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi.
Na svjedoèanstvo dva ili tri èovjeka da se pogubi onaj koga valja pogubiti; ali na svjedoèanstvo jednoga èovjeka da se ne pogubi.
7 Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
Svjedoci neka prvi dignu ruke na nj da ga ubiju; a potom sav narod; tako izvadi zlo iz sebe.
8 Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
Kad ti bude teško rasuditi izmeðu krvi i krvi, izmeðu raspre i raspre, ili izmeðu rane i rane, oko kojih bude parnica u tvojem mjestu, tada ustani i idi u mjesto koje izbere Gospod Bog tvoj;
9 Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita.
I otidi k sveštenicima Levitima ili k sudiji koji onda bude, pa ih upitaj, i oni æe ti kazati kako valja presuditi.
10 Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo.
I uèini onako kako ti kažu u mjestu koje izbere Gospod, i gledaj da uèiniš sasvijem onako kako te nauèe.
11 Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere.
Po zakonu kojemu te nauèe, i po presudi, koju ti kažu, uèini; ne otstupi od onoga što ti kažu ni nadesno ni nalijevo.
12 Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli.
Ako li bi se ko upro te ne bi htio poslušati sveštenika koji ondje stoji te služi Gospodu Bogu tvojemu, ili sudije, taki èovjek da se pogubi; i izvadi zlo iz Izrailja,
13 Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.
Da sav narod èuje i boji se, i unapredak da ne radi uporno.
14 Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,”
Kad uðeš u zemlju koju ti daje Gospod Bog tvoj da je naslijediš, i naseliš se u njoj, ako reèeš: da postavim sebi cara, kao što imaju svi narodi oko mene,
15 mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli.
Samo onoga postavi sebi za cara, kojega izbere Gospod Bog tvoj; izmeðu braæe svoje postavi cara sebi; a nemoj postaviti nad sobom èovjeka tuðina, koji nije brat tvoj.
16 Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.”
Ali da ne drži mnogo konja, i da ne vraæa naroda u Misir da bi imao mnogo konja, jer vam je Gospod kazao: ne vraæajte se više ovijem putem.
17 Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.
I da nema mnogo žena, da se ne bi otpadilo srce njegovo, ni srebra ni zlata da nema vrlo mnogo.
18 Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi.
A kad sjede na prijesto carstva svojega, neka prepiše sebi u knjigu ovaj zakon od sveštenika Levita;
19 Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa.
I neka ga drži kod sebe i neka ga èita dok je živ, da se uèi bojati se Gospoda Boga svojega, držati sve rijeèi ovoga zakona i ove uredbe, i tvoriti ih;
20 Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.
Da se ne bi podiglo srce njegovo iznad braæe njegove, i da ne bi otstupilo od ove zapovijesti ni nadesno ni nalijevo, da bi dugo carovao on i sinovi njegovi u Izrailju.

< Deuteronomo 17 >