< Deuteronomo 14 >

1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
Be ye the sones of youre Lord God; ye schulen not kitte you, nether ye schulen make ballidnesse,
2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
on a deed man, for thou art an hooli puple to thi Lord God, and he chees thee that thou be to hym in to a special puple, of alle folkis that ben on erthe.
3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
Ete ye not tho thingis that ben vncleene.
4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
This is a beeste which ye schulen ete; an oxe, and a scheep, and a goet, an hert,
5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
a capret, a `wielde oxe, tregelafun, `that is, a beeste in parti lijk `a buk of geet, and in parti liik an hert, a figarde, an ostrich, a camelioun, `that is, a beeste lijk in the heed to a camel, and hath white spottis in the bodi as a parde, and `is lijk an hors in the necke, and in the feet is lijc a `wilde oxe, and a parde.
6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
Ye schulen ete ech beeste that departith the clee `in to twei partis, and chewith code.
7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
Sotheli ye schulen not ete these beestis, of these that chewen code, and departen not the clee; a camel, an hare, and a cirogrille, `that is, a beeste ful of prickis, and is more than an irchoun; for tho chewen code, and departen not the clee, tho schulen be vncleene to you;
8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
also a swyn, for it departith the clee, and chewith not code, schal be vncleene; ye schulen not ete the fleischis of tho, and ye schulen not touche the deed bodies.
9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
Ye schulen ete these thingis, of alle that dwellen in watris; ete ye tho thingis that han fynnes and scalis;
10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
ete ye not tho thingis that ben with out fynnes and scalis, for tho ben vncleene.
11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
Ete ye alle clene briddis;
12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
ete ye not vncleene briddis, that is, an egle, and a gripe,
13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
and an aliete, ixon, `that is, a whijt brid lesse than a vultur, and is of the `kynde of vultris, and a vultur, and a kite bi his kynde,
14 mtundu uliwonse wa khwangwala,
and al thing of rauenys kynde,
15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
and a strucioun, and a nyyt crowe, and a lare,
16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
and an hauk bi his kynde, a fawcun,
17 tsekwe, vuwo, dembo,
and a swan, and a siconye, and a dippere, a pursirioun, and a reremous, a cormeraunt,
18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
and a caladrie, alle in her kynde; also a lapwynke and a backe.
19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
And al thing that crepith, and hath fynnes, schal be vncleene, and schal not be etun.
20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
Ete ye al thing that is cleene; sotheli what euer thing is deed bi it silf, ete ye not therof.
21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
Yyue thou to the pilgrym which is with ynne thi yatis, that he ete, ether sille thou to hym, for thou art the hooli puple of thi Lord God. Thou schalt not sethe a kyde in `the mylk of his modir.
22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
Thou schalt departe the tenthe part of alle thi fruytis that comen forth in the lond bi ech yeer;
23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
and thou schal ete in the siyt of thi Lord God, in the place which he chees, that his name be clepid therynne; thou schalt offre the tithe of thi wheete, wyn, and oile, and the firste gendryd thingis of thi droues, and scheep, that thou lerne to drede thi Lord God in al tyme.
24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
Sotheli whanne the wei is lengere, and the place which thi Lord God chees is fer, and he hath blessid thee, and thou maist not bere alle these thingis to that place,
25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
thou schalt sille alle thingis, and schalt turne in to prijs, and thou schalt bere in thin hond, and thou schalt go to the place which thi Lord God chees;
26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
and thou schalt bie of the same money what euer thing plesith to thee, ethir of droues, ether of scheep; also thou schalt bie wyn, and sidur, and al thing that thi soule desirith; and thou schalt ete bifor thi Lord God, and thou schalt make feeste,
27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
thou, and thin hows, and the dekene which is withynne thi yatis; be thou war lest thou forsake hym, for he hath not other part in possessioun.
28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
In the thridde yeer thou schalt departe another dyme of alle thingis that growen to thee in that yeer, and thou schalt kepe withynne thi yatis.
29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.
And the dekene schal come, whych hath noon other part nether possessioun with thee, and the pilgrym, and the fadirles, ether modirles child, and widue, that ben withynne thi yatis, `schulen come, and schulen ete, and be fillid, that thi Lord God blesse thee, in alle werkis of thin hondis whiche thou schalt do.

< Deuteronomo 14 >