< Danieli 9 >

1 Mʼchaka choyamba cha Dariyo mwana wa Ahasiwero (wochokera kwa Amedi), amene anakhala mfumu ya ku Babuloni,
In the firste yeer of Darius, the sone of Assuerus, of the seed of Medeis, that was emperour on the rewme of Caldeis,
2 ine Danieli ndinazindikira powerenga mawu a Yehova opatsidwa kwa mneneri Yeremiya, kuti Yerusalemu adzakhala bwinja kwa zaka 70.
in the firste yeer of his rewme, Y, Danyel, vndurstood in bookis the noumbre of yeeris, of which noumbre the word of the Lord was maad to Jeremye, the profete, that seuenti yeer of desolacioun of Jerusalem schulde be fillid.
3 Choncho ndinatembenukira kwa Ambuye Mulungu ndipo ndinamudandaulira ndi kupempha posala kudya, ndi kuvala chiguduli ndi kudzola phulusa.
And Y settide my face to my Lord God, to preie and to biseche in fastyngis, in sak, and aische.
4 Ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kuvomereza kuti tinachimwa: Ndinati, “Inu Ambuye, Mulungu wamkulu ndi woopsa, amene mumasunga pangano lanu la chikondi kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu,
And Y preiede my Lord God, and Y knoulechide, and seide, Y biseche, thou Lord God, greet and ferdful, kepynge couenaunt and mercy to hem that louen thee, and kepen thi comaundementis.
5 tachimwa ndipo tachita zolakwa ndi zoyipa. Takuwukirani posiya malangizo ndi malamulo anu.
We han synned, we han do wickidnesse, we diden unfeithfuli, and yeden awei, and bowiden awei fro thi comaundementis and domes.
6 Sitinamvere aneneri atumiki anu, amene anayankhula mʼdzina lanu kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, makolo athu, ndi kwa anthu onse a mʼdziko.
We obeieden not to thi seruauntis, profetis, that spaken in thi name to oure kyngis, to oure princes, and to oure fadris, and to al the puple of the lond.
7 “Ambuye ndinu olungama, koma lero tili ndi manyazi, ife anthu a ku Yuda, a ku Yerusalemu ndi Israeli yense, apafupi ndi akutali omwe, ku mayiko onse kumene munatipirikitsira chifukwa cha kusakhulupirika kwathu.
Lord, riytfulnesse is to thee, forsothe schenschipe of face is to vs, as is to dai to a man of Juda, and to the dwelleris of Jerusalem, and to al Israel, to these men that ben niy, and to these men that ben afer in alle londis, to which thou castidist hem out for the wickidnessis of hem, in whiche, Lord, thei synneden ayens thee.
8 Inu Yehova, ife ndi mafumu athu, akalonga athu ndi makolo athu tili ndi manyazi chifukwa takuchimwirani.
Schame of face is to vs, to oure kyngis, to oure princes, and to oure fadris, that synneden;
9 Ambuye Mulungu wathu ndi wachifundo ndi wokhululuka, ngakhale kuti tamuwukira:
but merci and benygnytee is to thee, oure Lord God. For we yeden awei fro thee,
10 Ife sitinamvere Yehova Mulungu wathu kapena kusunga malamulo ake amene anatipatsa kudzera mwa aneneri atumiki ake.
and herden not the vois of oure Lord God, that we schulden go in the lawe of hym, whiche he settide to vs bi hise seruauntis, profetis.
11 Aisraeli onse anachimwira lamulo lanu motero anapatuka, nakana kukumverani. “Choncho matemberero ndi olumbira amene alembedwa mʼmalamulo a Mose, mtumiki wa Mulungu, atigwera chifukwa takuchimwirani.
And al Israel braken thi lawe, and bowiden awei, that thei herden not thi vois; and cursyng, and wlatyng, which is writun in the book of Moises, the seruaunt of God, droppide on vs, for we synneden to hym.
12 Inu mwakwaniritsa mawu amene munayankhula otitsutsa ife ndi otsutsa otilamulira potibweretsera tsoka lalikulu. Pa dziko lapansi sipanachitikenso zinthu ngati zimene zaonekera Yerusalemu.
And he ordeynede hise wordis, whiche he spak on vs, and on oure princes, that demyden vs, that thei schulden brynge in on vs greet yuel, what maner yuel was neuer vndur al heuene, bi that that is doon in Jerusalem,
13 Monga kunalembedwa mʼMalamulo a Mose, tsoka lililonse latifikira chikhalirecho sitinapemphe Yehova Mulungu wathu kuti atikomere mtima. Sitinasiye machimo athu, ndipo sitinasamale choonadi chanu.
as it is writun in the lawe of Moises. Al this yuel cam on vs, and, oure Lord God, we preieden not thi face, that we schulden turne ayen fro oure wickidnessis, and schulden thenke thi treuthe.
14 Choncho Yehova anakonza kuti atigwetsere tsoka limeneli, ndipo wachitadi popeza Yehova Mulungu wathu ndi wolungama mu chilichonse amachita; chikhalirecho ife sitinamumvere.
And the Lord wakide on malice, and brouyt it on vs; oure Lord God is iust in alle his werkis whiche he made, for we herden not his vois.
15 “Inu Ambuye Mulungu wathu, munatulutsa anthu anu ku Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo dzina lanu ndi lotchuka mpaka lero. Ife tachimwa, tachita zolakwa.
And now, Lord God, that leddist thi puple out of the lond of Egipt in strong hond, and madist to thee a name bi this dai, we han synnede,
16 Inu Ambuye, molingana ndi zochita zanu zolungama, tikukupemphani kuti muchotse mkwiyo ndi ukali wanu pa Yerusalemu mzinda wanu, phiri lanu loyera. Machimo athu ndi mphulupulu za makolo athu zachititsa kuti onse otizungulira atonze Yerusalemu ndi anthu anu.
we han do wickidnesse, Lord, ayens thi riytfulnesse. Y biseche, thi wraththe and thi stronge veniaunce be turned awey fro thi citee Jerusalem, and fro thi hooli hil; for whi for oure synnes, and for the wickidnessis of oure fadris, Jerusalem and thi puple ben in schenschipe, to alle men bi oure cumpas.
17 “Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.
But now, oure God, here thou the preyer of thi seruaunt, and the bisechyngis of him, and schewe thi face on thi seyntuarie, which is forsakun.
18 Tcherani khutu, Inu Mulungu, ndipo imvani; tsekulani maso anu ndipo onani mabwinja athu ndi mzinda umene umadziwika ndi dzina lanu. Sitikupempha chifukwa chakuti ndife olungama, koma chifukwa cha kukula kwa chifundo chanu.
My God, for thi silf boowe doun thin eere, and here; opene thin iyen, and se oure desolacioun, and the citee, on which thi name is clepid to help. For not in oure iustifiyngis we setten forth mekeli preiers bifor thi face, but in thi many merciful doyngis.
19 Inu Ambuye imvani mawu athu! Ambuye khululukani! Ambuye timvereni, ndipo muchitepo kanthu! Kuti anthu adziwe kuti Inu ndinu Mulungu wanga musachedwe chifukwa mzinda wanu ndi anthu anu amadziwika ndi dzina lanu.”
Lord, here thou; Lord, be thou plesid, perseyue thou, and do; my Lord God, tarie thou not, for thi silf, for thi name is clepid to help on the citee, and on thi puple.
20 Ndikuyankhula ndi kupemphera, kuvomereza machimo anga ndi machimo a anthu anga Aisraeli ndi kupempherera phiri lake loyera kwa Yehova Mulungu wanga,
And whanne Y spak yit, and preiede, and knoulechide my synnes, and the synnes of my puple Israel, that Y schulde sette forth mekeli my preieris in the siyt of my God, for the hooli hil of my God,
21 Gabrieli, munthu uja amene ndinamuona mʼmasomphenya poyambirira, anabwera kwa ine mowuluka. Iyi inali nthawi ya nsembe ya madzulo.
the while Y spak yit in my preyer, lo! the man Gabriel, whom Y hadde seyn in visioun at the bigynnyng, flei soone, and touchide me in the tyme of euentid sacrifice;
22 Anandilangiza kuti, “Danieli ndabwera tsopano kuti ndikupatse nzeru kuti uzitha kumvetsa zinthu.
and he tauyt me, and he spak to me, and seide, Danyel, now Y yede out, that Y schulde teche thee, and thou schuldist vndurstonde.
23 Utangoyamba kupemphera, Mulungu anayankha. Tsono ine ndabwera kudzakuwuza yankholo, popeza ndiwe wokondedwa kwambiri. Choncho mvetsetsa pamene ndikufotokoza za zinthu zimene unaziona mʼmasomphenya.
Fro the bigynnyng of thi preieris a word yede out. Forsothe Y cam to schewe to thee, for thou art a man of desiris; therfor perseyue thou the word, and vndurstonde thou the visioun.
24 “Zaka 490 zinayikidwa kuti anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera aleke zoyipa, asiye tchimo. Iwo adzapereka dipo kupepesera zolakwa zawo. Zikadzatero anthu adzaonetsa moyo wachilungamo nthawi zonse. Izi zidzatsimikiza zimene unaziona mʼmasomphenya zija ndi zimene ananenera aneneri. Malo opatulika adzakhazikitsidwa.
Seuenti woukis of yeeris ben abreggid on thi puple, and on thin hooli citee, that trespassyng be endid, and synne take an ende, and that wickidnesse be doon awei, and euerlastynge riytfulnesse be brouyt, and that the visioun, and prophesie be fillid, and the hooli of seyntis be anoyntid.
25 “Tsono udziwe ndipo uzindikire izi kuti kuyambira pamene lamulo linaperekedwa kuti Yerusalemu akonzedwenso mpaka pamene mfumu Yodzozedwa idzafike padzapita zaka 49. Pa zaka 434 mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso, ndipo mabwalo ndi ngalande zake zidzatetezedwa. Koma nthawiyi idzakhala ya masautso.
Therfor wite thou, and perseyue; fro the goyng out of the word, that Jerusalem be bildid eft, til to Crist, the duyk, schulen be seuene woukis of yeeris and two and sixti woukis of yeeris; and eft the street schal be bildid, and wallis, in the angwisch of tymes.
26 Patatha zaka 434, Wodzozedwayo adzaphedwa ndipo sadzakhala ndi aliyense. Anthu a wolamulira amene adzabwere adzawononga mzinda ndi Nyumba ya Mulungu. Kutha kwake kudzafika ngati chigumula. Komabe nkhondo idzapitirira mpaka chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu chitachitika.
And after two and sixti woukis `of yeeris Crist schal be slayn. And it schal not be his puple, that schal denye hym. And the puple with the duyk to comynge schal distrie the citee, and the seyntuarie; and the ende therof schal be distriyng, and after the ende of batel schal be ordeynede desolacioun.
27 Adzachita pangano lolimba ndi anthu ambiri kwa zaka zisanu ndi ziwiri. Koma pakatinʼpakati pa sabata limodzilo iye adzaletsa kupereka nsembe ndi chopereka. Chonyansa chosakaza chija adzachiyika mʼNyumba ya Mulungu, ndipo chidzakhalapobe mpaka wochita zimenezi atalangidwa ndi chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu.”
Forsothe o wouk `of yeeris schal conferme the couenaunt to many men, and the offryng and sacrifice schal faile in the myddis of the wouke of yeeris; and abhomynacioun of desolacioun schal be in the temple, and the desolacioun schal contynue til to the parformyng and ende.

< Danieli 9 >