< Danieli 8 >

1 Chaka chachitatu cha ulamuliro wa mfumu Belisazara, Ine Danieli, ndinaonanso masomphenya, ena atatha amene anandionekera poyamba.
In the thridde yeer of the rewme of Balthasar, the king, a visioun apperide to me. Y, Danyel, after that thing that Y hadde seyn in the bigynnyng,
2 Ndinaona mʼmasomphenya kuti ndinali mu mzinda wotetezedwa wa Susa mʼchigawo cha Elamu. Mʼmasomphenyawo ndinaona nditayima pafupi ndi mtsinje wa Ulai.
siy in my visioun, whanne Y was in the castel of Susis, which is in the cuntrei of Helam; sotheli Y siy in the visioun that Y was on the yate Vlay.
3 Nditakweza maso ndinaona nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri, itayima pafupi ndi mtsinje. Nyanga zakezo zinali zazitali. Nyanga imodzi inali yotalika kuposa inzake, ndipo iyi inaphuka inzakeyo itamera kale.
And Y reiside myn iyen, and Y siy; and lo! o ram stood bifor the mareis, and hadde hiy hornes, and oon hiyere than the tother, and vndurwexynge.
4 Ndinaona nkhosa yayimunayo ikuthamanga mwaukali kupita kumadzulo, kumpoto ndi kummwera. Palibe chirombo chimene chikanatha kulimbana nayo, ndipo palibe akanatha kulanditsa kanthu kwa iyo. Iyo inachita monga inafunira ndipo inali ndi mphamvu zambiri.
Aftirward Y siy the ram wyndewynge with hornes ayens the eest, and ayens the west, and ayens the north, and ayens the south; and alle beestis myyten not ayenstonde it, nether be delyuered fro the hondis of it. And it dide bi his wille, and was magnefied.
5 Pamene ndinali kulingalira za zinthu zimenezi, mwadzidzidzi mbuzi yayimuna inatulukira cha kumadzulo, kudutsa dziko lonse lapansi mwaliwiro ikuyenda mʼmalele mokhamokha. Mbuzi yayimunayo inali ndi nyanga yayikulu pakati pa maso ake.
And Y vndurstood. Lo! forsothe a buk of geet cam fro the west on the face of al erthe, and touchide not the erthe; forsothe the buk of geet hadde a noble horn bitwixe hise iyen;
6 Inabwera molunjika nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri ija imene ndinaona itayima pafupi ndi mtsinje. Ndipo inayithamangira mwaukali.
and he cam til to that horned ram, which Y hadde seyn stondynge bifore the yate, and he ran in the fersnesse of his strengthe to that ram.
7 Inafika pafupi ndipo inalimbana nayo mwaukali nkhosa yayimuna ija nʼkuthyola nyanga zake ziwiri. Nkhosa yayimunayo inalibenso mphamvu zogonjetsera mbuziyo; choncho mbuzi ija inagwetsa nkhosayo pansi nʼkuyipondaponda, ndipo palibe akanatha kulanditsa nkhosayo kwa mbuziyo.
And whanne he hadde neiyid niy the ram, he hurlide fersly on hym, and he smoot the ram, and al to-brak tweyne hornes of hym, and the ram miyte not ayenstonde hym. And whanne he hadde sent that ram in to erthe, he defoulide; and no man miyte delyuere the ram fro his hond.
8 Mbuziyo inayamba kudzikuza kwambiri chifukwa cha mphamvu zake koma pamene mphamvuzo zinakula kwambiri nyanga yake yayikulu inathyoka, ndipo mʼmalo mwake panamera nyanga zinayi moloza mbali zonse zinayi.
Forsothe the buk of geet was maad ful greet; and whanne he hadde encreessid, the greet horn was brokun, and foure hornes risiden vndur it, bi foure wyndis of heuene.
9 Pa imodzi mwa nyangazo panatuluka nyanga imene inali yocheperapo koma inakula kwambiri kuloza kummwera ndi kummawa ndi kuloza dziko lokongola.
Forsothe of oon of hem yede out o litil horn, and it was maad greet ayens the south, and ayens the eest, and ayens the strengthe.
10 Inakula mpaka inafikira gulu lankhondo la kumwamba, ndipo inagwetsera ena a gulu lankhondolo ndi ena a gulu la nyenyezi ku dziko lapansi ndi kuwapondaponda.
And it was magnefied til to the strengthe of heuene, and it castide doun of the strengthe and of sterris, and defoulide tho.
11 Inadzikuza yokha mpaka kufikira kwa mfumu ya gululo: inathetsa nsembe zimene zinkaperekedwa tsiku ndi tsiku, ndipo inagwetsa nyumba yake yopatulika.
And he was magnefied til to the prince of strengthe, and he took awei fro hym the contynuel sacrifice, and castide doun the place of his halewyng.
12 Gulu lake la nkhondo linathetsa nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku; chipembedzo choonadi chinaponderezedwa pansi. Nyangayi inapambana mu zonse zimene inachita.
Forsothe strengthe was youun to hym ayens the contynuel sacrifice for synnes, and treuthe schal be cast doun in erthe; and he schal haue prosperite, and schal do.
13 Kenaka ndinamva wina akuyankhula; ndipo woyera winanso anamufunsa kuti, “Kodi zimene ndikuziona mʼmasomphenyazi zidzatha liti? Nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku zidzakhala zoletsedwa mpaka liti? Nanga chonyansa chosokoneza chidzakhalapo mpaka liti? Kodi gulu la ankhondo lidzapondereza malo opatulika mpaka liti?”
And Y herde oon of hooli aungels spekynge; and oon hooli aungel seide to another, Y noot to whom spekinge, Hou long the visioun, and the contynuel sacrifice, and the synne of desolacioun, which is maad, and the seyntuarie, and the strengthe schal be defoulid?
14 Iye anandiyankha kuti, “Zidzachitika patapita masiku 2,300; pambuyo pake malo opatulika adzabwezeretsedwa monga kale.”
And he seide to hym, Til to the euentid and morewtid, two thousynde daies and thre hundrid; and the seyntuarie schal be clensid.
15 Ine Danieli ndikuyangʼanitsitsa masomphenyawa ndi kuyesa kuwazindikira, kuwamvetsa, ndinangoona wina wooneka ngati munthu atayima patsogolo panga.
Forsothe it was doon, whanne Y, Danyel, siy the visioun, and axide the vndurstondyng, lo! as the licnesse of a man stood in my siyt.
16 Ndipo ndinamva mawu a munthu kuchokera mʼmbali mwa mtsinje wa Ulai akuyitana kuti, “Gabrieli, muwuze munthuyu tanthauzo la masomphenyawo.”
And Y herde the voys of a man bitwixe Vlai, and he criede, and seide, Gabriel, make thou Danyel to vndurstonde this visioun.
17 Atayandikira kumene ndinayima, ndinachita mantha ndi kugwa chafufumimba. Iye anati, “Mwana wa munthu, zindikira kuti masomphenyawa akunena za nthawi yachimaliziro.”
And he cam, and stood bisidis where Y stood; and whanne he was comun, Y dredde, and felle on my face. And he seide to me, Thou, sone of man, vndurstonde, for the visioun schal be fillid in the tyme of ende.
18 Pamene ankandiyankhula ndinadzigwetsa pansi chafufumimba, nʼkugona tulo tofa nato. Kenaka anandikhudza ndi kundiyimiritsa.
And whanne he spak to me, Y slood doun `plat to the erthe. And he touchide me, and settide me in my degree.
19 Iye anati, “Ine ndikuwuza zimene zidzachitike ukadzatha mkwiyo, chifukwa masomphenyawa ndi a nthawi ya chimaliziro.”
And he seide to me, Y schal schewe to thee what thingis schulen come in the laste of cursing, for the tyme hath his ende.
20 Nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri imene unayiona, ikuyimira mafumu a Amedi ndi Aperezi.
The ram, whom thou siyest haue hornes, is the kyng of Medeis and of Perseis.
21 Mbuzi yayimuna ija ndi mfumu ya Agriki, ndipo nyanga yayikulu pakati pa maso ake aja ndi mfumu yoyamba.
Forsothe the buc of geet is the kyng of Grekis; and the greet horn that was bitwixe hise iyen, he is the firste kyng.
22 Kunena za nyanga inathyoka ija ndi nyanga zinayi zimene zinaphuka mʼmalo mwake zikutanthauza maufumu anayi amene adzatuluka mʼdziko lake; koma sizidzafanana mphamvu ndi ufumu woyambawo.
Forsothe that whanne that horn was brokun, foure hornes risiden for it, foure kyngis schulen rise of the folc of hym, but not in the strengthe of hym.
23 “Pa masiku otsiriza a maufumuwa, machimo awo atachulukitsa, padzadzuka mfumu yaukali ndi yochenjera kwambiri.
And after the rewme of hem, whanne `wickidnessis han encreessid, a kyng schal rise vnschamefast in face, and vndurstondyng proposisiouns, ether resouns set forth; and his strengthe schal be maad stalworthe,
24 Idzakhala yamphamvu kwambiri koma osati mphamvu za iyo yokha. Idzawononga koopsa ndipo idzapambana mu chilichonse chimene idzachite. Mfumuyi idzawononga anthu amphamvu ndi anthu oyera omwe.
but not in hise strengthis. And more than it mai be bileuyd he schal waste alle thingis, and he schal haue prosperite, and schal do. And he schal sle stronge men, and the puple of seyntis,
25 Chifukwa cha kuchenjera kwake chinyengo chidzachuluka pa nthawi ya ulamuliro wake, ndipo idzadzikuza kuposa onse. Pamene oyera mtima adzaona ngati kuti ali otetezedwa, iyo idzawononga ambiri ndi kuwukira ngakhale Mfumu ya mafumu. Komabe idzawonongedwa, koma osati ndi mphamvu za munthu.
bi his wille, and gile schal be dressid in his hond. And he schal magnefie his herte, and in abundaunce of alle thingis he schal sle ful many men. And he schal rise ayens the prince of princes, and withouten hond he schal be al to-brokun.
26 “Masomphenya okhudza madzulo ndi mmawa amene unawaona aja ndi woona, koma uwasunge masomphenyawa mwachinsinsi popeza ndi onena za masiku a mʼtsogolo kwambiri.”
And the visioun, which is seid in the morewtid and euentid, is trewe. Therfor seele thou the visioun, for it schal be after many daies.
27 Ine Danieli ndinafowoka ndipo ndinadwala masiku angapo. Kenaka ndinadzuka ndi kupitiriza ntchito za mfumu. Ndinada nkhawa ndi masomphenyawo; ndipo sindinathe kuwamvetsa.
And Y, Danyel, was astonyed, and was sijk bi ful many daies; and whanne Y hadde rise, Y dide the werkis of the kyng; and Y was astonyed at the visioun, and `noon was that interpretide.

< Danieli 8 >