< Amosi 9 >

1 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
I siy the Lord stondynge on the auter, and he seide, Smyte thou the herre, and the ouer threshfoldis be mouyd togidere; for aueryce is in the heed of alle, and Y schal sle bi swerd the laste of hem; ther schal no fliyt be to hem, and he that schal fle of hem, schal not be sauyd.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol h7585)
If thei schulen go doun til to helle, fro thennus myn hond schal lede out hem; and if thei schulen `stie til in to heuene, fro thennus Y schal drawe hem doun. (Sheol h7585)
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
And if thei schulen be hid in the cop of Carmele, fro thennus Y sekynge schal do awei hem; and if thei schulen hide hem silf fro myn iyen in the depnesse of the see, there Y shal comaunde to a serpente, and it schal bite hem.
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
And if thei schulen go awei in to caitifte bifore her enemyes, there Y schal comaunde to swerd, and it schal sle hem. And Y schal putte myn iyen on hem in to yuel, and not in to good.
5 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
And the Lord God of oostis schal do these thingis, that touchith erthe, and it schal faile, and alle men dwellynge ther ynne schulen mourene; and it schal stie vp as ech stronde, and it schal flete awei as flood of Egipt.
6 Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
He that bildith his stiyng vp in heuene, schal do these thingis, and foundide his birthun on erthe; which clepith watris of the see, and heldith out hem on the face of erthe; the Lord is name of hym.
7 “Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
Whether not as sones of Ethiopiens ye ben to me, the sones of Israel? seith the Lord God. Whether Y made not Israel for to stie vp fro the lond of Egipt, and Palestines fro Capodosie, and Siriens fro Cirenen?
8 “Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
Lo! the iyen of the Lord God ben on the rewme synnynge, and Y schal al to-breke it fro the face of erthe; netheles Y al to-brekynge schal not al to-breke the hous of Jacob, seith the Lord.
9 “Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
For lo! Y schal comaunde, and schal schake the hous of Israel in alle folkis, as wheete is in a riddil, and a litil stoon schal not falle on erthe.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
Alle synneris of my puple schulen die bi swerd, whiche seien, Yuel schal not neiy, and schal not come on vs.
11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
In that dai Y schal reise the tabernacle of Dauith, that felle doun, and Y schal ayen bilde openyngis of wallis therof, and Y schal restore the thingis that fellen doun; and Y schal ayen bilde it,
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
as in olde daies, that thei welde the remenauntis of Idume, and alle naciouns; for that my name is clepun to help on hem, seith the Lord doynge these thingis.
13 Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
Lo! daies comen, seith the Lord, and the erere schal take the repere, and `the stampere of grape schal take the man sowynge seed; and mounteyns schulen droppe swetnesse, and alle smale hillis schulen be tilid.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
And Y schal conuerte the caitifte of my puple Israel, and thei schulen bilde forsakun citees, and schulen dwelle; and schulen plaunte vyneyerdis, and thei schulen drynke wyn of hem; and schulen make gardyns, and schulen ete fruitis of hem.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.
And Y schal plaunte hem on her lond, and Y schal no more drawe out hem of her lond, which Y yaf to hem, seith the Lord thi God.

< Amosi 9 >