< Amosi 7 >

1 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
The Lord God schewide these thingis to me; and lo! a makere of locust in bigynnyng of buriownynge thingis of euentid reyn, and lo! euentid reyn after the clippere of the kyng.
2 Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
And it was don, whanne he hadde endid for to ete the erbe of erthe, Y seide, Lord God, Y biseche, be thou merciful; who schal reise Jacob, for he is litil?
3 Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
The Lord hadde merci on this thing; It schal not be, seide the Lord God.
4 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
The Lord God schewide to me these thingis; and lo! the Lord God schal clepe doom to fier, and it schal deuoure myche depthe of watir, and it eet togidere a part.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
And Y seide, Lord God, Y biseche, reste thou; who schal reise Jacob, for he is litil?
6 Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
The Lord hadde merci on this thing; But and this thing schal not be, seide the Lord God.
7 Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
The Lord God schewide to me these thingis; and lo! the Lord stondinge on a wal plastrid, and in the hond of hym was a trulle of a masoun.
8 Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
And the Lord seide to me, What seest thou, Amos? And Y seide, A trulle of a masoun. And the Lord seide, Lo! I schal putte a trulle in the myddil of my puple Israel; Y schal no more putte to, for to ouerlede it;
9 “Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
and the hiy thingis of idol schulen be distried, and the halewyngis of Israel schulen be desolat; and Y schal rise on the hous of Jeroboam bi swerd.
10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
And Amasie, prest of Bethel, sente to Jeroboam, kyng of Israel, and seide, Amos rebellide ayens thee, in the myddil of the hous of Israel; the lond mai not susteyne alle hise wordis.
11 Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
For Amos seith these thingis, Jeroboam schal die bi swerd, and Israel caitif schal passe fro his lond.
12 Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
And Amasie seide to Amos, Thou that seest, go; fle thou in to the lond of Juda, and ete thou there thi breed; and there thou schalt profesie.
13 Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
And thou schalt no more put to, that thou profesie in Bethel, for it is the halewyng of the king, and is the hous of the rewme.
14 Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
And Amos answeride, and seide to Amasie, Y am not a profete, and Y am not sone of profete; but an herde of neet Y am, drawyng vp sicomoris.
15 Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
And the Lord took me, whanne Y suede the floc; and the Lord seide to me, Go, and profesie thou to my puple Israel.
16 Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
And now here thou the word of the Lord. Thou seist, Thou schalt not profesie on Israel, and thou schal not droppe on the hous of idol.
17 “Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
For this thing the Lord seith these thingis, Thi wijf schal do fornicacioun in the citee, and thi sones and thi douytris schal falle bi swerd, and thi lond schal be motun with a litil coord; and thou schalt die in a pollutid lond, and Israel caitif schal passe fro his lond.

< Amosi 7 >