< Amosi 4 >

1 Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
Èujte ovu rijeè, krave Vasanske, koje ste u gori Samarijskoj, koje krivo èinite ubogima i satirete siromahe, koje govorite gospodarima svojim: donesite da pijemo.
2 Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
Zakle se Gospod Gospod svetošæu svojom da æe vam evo doæi dani, te æe vas izvlaèiti kukama, i ostatak vaš udicama ribarskim.
3 Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
I kroz prolome æete ižljesti, svaka na prema se, i pobacaæete što bude u dvorovima, govori Gospod.
4 “Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
Idite u Vetilj, i èinite bezakonje, u Galgalu množite bezakonje svoje, i prinosite svako jutro žrtve svoje, treæe godine desetke svoje;
5 Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
I palite žrtvu zahvalnu od hljeba kiseloga, i oglasite žrtve dragovoljne i razglasite, jer vam je tako milo, sinovi Izrailjevi, govori Gospod Gospod.
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I zato vam ja dadoh da su vam èisti zubi po svijem gradovima vašim i da nema hljeba nigdje po svijem mjestima vašim; ali se ne obratiste k meni, govori Gospod.
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
A ja vam ustegoh dažd, kad još tri mjeseca bijahu do žetve, i pustih dažd na jedan grad, a na drugi grad ne pustih dažda, jedan se kraj nakvasi, a drugi kraj, na koji ne daždje, posuši se.
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Tako dva i tri grada iðahu u jedan grad da piju vode, i ne mogahu se napiti; ipak se ne obratiste k meni, govori Gospod.
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Bih vas sušom i medljikom; gusjenice izjedoše obilje u vrtovima vašim i u vinogradima vašim i na smokvama vašim i na maslinama vašim; ipak se ne obratiste k meni, govori Gospod.
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Poslah u vas pomor kao u Misir, pobih maèem mladiæe vaše i odvedoh konje vaše, i uèinih te se podizaše smrad iz okola vašega i u nozdrve vaše; ipak se ne obratiste k meni, govori Gospod.
11 “Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Zatirah vas kao što Gospod zatr Sodom i Gomor, i bijaste kao glavnja istrgnuta iz ognja; ipak se ne obratiste k meni, govori Gospod.
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
Zato æu ti tako uèiniti, Izrailju; i što æu ti tako uèiniti, pripravi se, Izrailju, da sreteš Boga svojega.
13 Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Jer eto onoga koji je sazdao gore i koji je stvorio vjetar i javlja èovjeku što misli, èini od zore tamu, i hodi po visinama zemaljskim; ime mu je Gospod Bog nad vojskama.

< Amosi 4 >