< Amosi 3 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
Èujte rijeè koju govori Gospod za vas, sinovi Izrailjevi, za sve pleme koje sam izveo iz zemlje Misirske, govoreæi:
2 “Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
Samo vas poznah izmeðu svijeh plemena zemaljskih, zato æu vas pohoditi za sva bezakonja vaša.
3 Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
Hoæe li dvojica iæi zajedno, ako se ne sastanu?
4 Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
Hoæe li riknuti lav u šumi, ako nema lova? hoæe li laviæ pustiti glas svoj iz peæine svoje, ako ne uhvati što?
5 Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
Hoæe li ptica pasti u mrežu na zemlju, ako nema zamke? hoæe li se dignuti mreža sa zemlje, ako se ništa ne uhvati?
6 Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
Hoæe li truba trubiti po gradu, a narod da ne dotrèi uplašen? hoæe li biti nesreæa u gradu, a Gospod da je ne uèini?
7 Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
Jer Gospod Gospod ne èini ništa ne otkrivši tajne svoje slugama svojim prorocima.
8 Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
Kad lav rikne, ko se neæe bojati? kad Gospod reèe, ko neæe prorokovati?
9 Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
Oglasite po dvorovima Azotskim i po dvorovima u zemlji Misirskoj, i recite: skupite se na gore Samarijske i vidite velike nerede u njoj i nasilje u njoj.
10 “Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
Ne znaju èiniti pravo, govori Gospod, sabiraju blago nasiljem i grabežem u dvorima svojim.
11 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
Zato ovako veli Gospod Gospod: neprijatelj je oko zemlje i oboriæe ti silu tvoju, i oplijeniæe se dvorovi tvoji.
12 Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
Ovako veli Gospod: kao kad pastir istrgne iz usta lavu dvije golijeni ili kraj od uha, tako æe se istrgnuti sinovi Izrailjevi koji sjede u Samariji na uglu od odra i nakraj postelje.
13 “Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Èujte i zasvjedoèite u domu Jakovljevu, govori Gospod Gospod Bog nad vojskama.
14 “Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
Kad pohodim Izrailja za grijehe njegove, tada æu pohoditi i oltare Vetiljske, i odbiæe se rogovi oltaru i pašæe na zemlju.
15 Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.
I udariæu kuæu zimnu i ljetnu kuæu, i propašæe kuæe od slonove kosti, i nestaæe velikih kuæa, govori Gospod.

< Amosi 3 >