< Amosi 4 >

1 Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
Ye fatte kien, that ben in the hil of Samarie, here this word; whiche maken fals caleng to nedi men, and breken pore men; which seien to youre lordis, Bringe ye, and we schulen drynke.
2 Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
The Lord God swoor in his hooli, for lo! daies schulen come on you; and thei schulen reise you in schaftis, and youre remenauntis in buylynge pottis.
3 Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
And ye schulen go out bi the openyngis, oon ayens another, and ye schulen be cast forth in to Armon, seith the Lord.
4 “Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
Come ye to Bethel, and do ye wickidli; to Galgala, and multiplie ye trespassyng; and offre ye eerli youre sacrifices, in thre daies youre tithis.
5 Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
And sacrifice ye heriyng of breed maad sour, and clepe ye wilful offryngis, and telle ye; for ye, sones of Israel, wolden so, seith the Lord God.
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Wherfor and Y yaf to you astonying of teeth in alle youre citees, and nedinesse of looues in alle youre places; and ye turneden not ayen to me, seith the Lord.
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
Also Y forbeed reyn fro you, whanne thre monethis weren yit `to comyng, til to ripe corn; and Y reynede on o citee, and on another citee Y reynede not; o part was bireyned, and the part driede vp on which Y reynede not.
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
And tweyne and thre citees camen to o citee, to drynke watir, and tho weren not fillid; and ye camen not ayen to me, seith the Lord.
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Y smoot you with brennynge wynd, and with rust, the multitude of youre orcherdis, and of youre vyneris; and a wort worm eet youre olyue places, and youre fige places; and ye camen not ayen to me, seith the Lord.
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Y sente in to you deth in the weie of Egipt, Y smoot with swerd youre yonge men, `til to the caitifte of youre horsis, and Y made the stynk of youre oostis to stie in to youre nose thirlis; and ye camen not ayen to me, seith the Lord.
11 “Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Y distriede you, as God distriede Sodom and Gomorre, and ye ben maad as a brond rauyschid of brennyng; and ye turneden not ayen to me, seith the Lord.
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
Wherfor, thou Israel, Y schal do these thingis to thee; but aftir that Y schal do to thee these thingis, Israel, be maad redi in to ayen comyng of thi God.
13 Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
For lo! he fourmeth hillis, and makith wynd, and tellith to man his speche; and he makith a `morew myist, and goith on hiy thingis of erthe; the Lord God of oostis is the name of hym.

< Amosi 4 >