< Machitidwe a Atumwi 8 >

1 Ndipo Saulo anavomerezana nawo pa imfa ya Stefano. Tsiku lomwelo, mpingo wa mu Yerusalemu unayamba kuzunzidwa, ndipo onse, kupatulapo atumwi, anabalalikira ku madera onse a Yudeya ndi Samariya.
Savle pak bješe pristao na njegovu smrt. A u taj dan postade veliko gonjenje na crkvu Jerusalimsku, i svi se rasijaše po krajevima Judejskijem i Samarijskijem osim apostola.
2 Anthu okonda Mulungu anayika maliro a Stefano ndipo anamulira kwambiri.
A ljudi pobožni ukopaše Stefana i veliki plaè uèiniše nad njim.
3 Koma Saulo anayamba kuwononga mpingo. Amapita nyumba ndi nyumba, ndipo amagwira amuna ndi amayi ndi kukawatsekera ku ndende.
A Savle dosaðivaše crkvi, jer iðaše po kuæama, i vucijaše ljude i žene te predavaše u tamnicu.
4 Okhulupirira amene anabalalika amalalikira konse kumene amapita.
A oni što se bijahu rasijali prolažahu propovijedajuæi rijeè.
5 Filipo anapita ku mzinda wa ku Samariya ndipo analalikira za Khristu kumeneko.
A Filip sišavši u grad Samarijski propovijedaše im Hrista.
6 Gulu la anthu litamva Filipo akulalikira komanso kuona zizindikiro zozizwitsa zimene ankazichita, onse anamvetsetsa zimene iye amanena.
A narod pažaše jednodušno na ono što govoraše Filip, slušajuæi i gledajuæi znake koje èinjaše;
7 Mizimu yoyipa inatuluka mwa anthu ambiri ikufuwula kwambiri ndipo ambiri amene anali akufa ziwalo ndi olumala anachiritsidwa.
Jer duhovi neèisti s velikom vikom izlažahu iz mnogijeh u kojima bijahu, i mnogi uzeti i hromi ozdraviše.
8 Kotero munali chimwemwe chachikulu mu mzindawo.
I bi velika radost u gradu onome.
9 Koma mu mzindawo munali munthu dzina lake Simoni, amene amachita za matsenga ndi kudabwitsa anthu a mu Samariya. Iye amadzitamandira kuti ndi wopambana,
A bješe jedan èovjek, po imenu Simon, koji prije èaraše u gradu i dovoðaše u èudo narod Samarijski, govoreæi da je on nešto veliko;
10 ndipo anthu onse, aakulu ndi aangʼono anamumvera ndi kunena kuti, “Munthu uyu ndi mphamvu ya Mulungu yotchedwa Mphamvu yayikulu.”
Na kojega gledahu svi, i malo i veliko, govoreæi: ovo je velika sila Božija.
11 Anthu amamutsata chifukwa kwa nthawi yayitali amawadabwitsa ndi matsenga akewo.
A zato gledahu na njega što ih mnogo vremena èinima udivljavaše.
12 Koma atakhulupirira Filipo akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ndiponso dzina la Yesu Khristu, anthuwo anabatizidwa amuna ndi amayi.
Kad pak vjerovaše Filipu koji propovijedaše jevanðelje o carstvu Božijemu i o imenu Isusa Hrista, kršæavahu se i ljudi i žene.
13 Nayenso Simoni anakhulupirira ndipo anabatizidwa, natsatira Filipo kulikonse, ndipo anadabwa kwambiri pamene anaona zizindikiro zazikulu ndi zozizwitsa.
Tada i Simon vjerova, i krstivši se osta kod Filipa; i videæi djela i znake velike koji se èinjahu divljaše se vrlo.
14 Atumwi a ku Yerusalemu atamva kuti anthu a ku Samariya analandira Mawu a Mulungu, anatumiza Petro ndi Yohane.
A kad èuše apostoli koji bijahu u Jerusalimu da Samarija primi rijeè Božiju, poslaše k njima Petra i Jovana.
15 Atafika anawapempherera kuti alandire Mzimu Woyera,
Koji sišavši pomoliše se Bogu za njih da prime Duha svetoga;
16 chifukwa Mzimu Woyera anali asanafike pa wina aliyense wa iwo; anali atangobatizidwa mʼdzina la Ambuye Yesu.
Jer još ni na jednoga ne bješe došao, nego bijahu samo kršteni u ime Gospoda Isusa.
17 Ndipo Petro ndi Yohane anasanjika manja awo pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.
Tada apostoli metnuše ruke na njih, i oni primiše Duha svetoga.
18 Simoni ataona kuti Mzimu anaperekedwa kwa iwo atumwi atawasanjika manja, iye anafuna kuwapatsa ndalama ndipo anati,
A kad vidje Simon da se daje Duh sveti kad apostoli metnu ruke, donese im novce
19 “Inenso ndipatseni mphamvu imeneyi kuti aliyense amene ndimusanjika manja anga azilandira Mzimu Woyera.”
Govoreæi: dajte i meni ovu vlast da kad metnem ruke na koga primi Duha svetoga.
20 Petro anayankha kuti, “Ndalama zako utayike nazo pamodzi, chifukwa unaganiza kuti ungathe kugula mphatso ya Mulungu ndi ndalama!
A Petar mu reèe: novci tvoji s tobom da budu u pogibao, što si pomislio da se dar Božij može dobiti za novce.
21 Ulibe gawo kapena mbali pa utumikiwu, chifukwa mtima wako suli wolungama pamaso pa Mulungu.
Nema tebi dijela ni iseta u ovoj rijeèi; jer srce tvoje nije pravo pred Bogom.
22 Lapa zoyipa zakozi ndipo upemphere kwa Ambuye. Mwina adzakukhululukira maganizo a mu mtima mwako.
Pokaj se dakle od ove svoje pakosti, i moli se Bogu da bi ti se oprostila pomisao srca tvoga.
23 Pakuti ine ndikuona kuti ndiwe wowawidwa mtima ndiponso kapolo wa tchimo.”
Jer te vidim da si u grkoj žuèi i u svezi nepravde.
24 Ndipo Simoni anayankha, “Mundipempherere kwa Ambuye kuti zisandigwere izi mwanenazi.”
A Simon odgovarajuæi reèe: pomolite se vi Gospodu za mene da ne naiðe na mene ništa od ovoga što rekoste.
25 Atatha kuchitira umboni ndi kulalikira mawu a Ambuye, Petro ndi Yohane anabwerera ku Yerusalemu, atalalikira Uthenga Wabwino mʼmidzi yambiri ya Asamariya.
Tako oni posvjedoèivši i govorivši rijeè Gospodnju vratiše se u Jerusalim, i mnogijem selima Samarijskijem propovjediše jevanðelje.
26 Mngelo wa Ambuye anati kwa Filipo, “Nyamuka pita chakummwera, ku msewu wa ku chipululu wopita ku Gaza kuchokera ku Yerusalemu.”
A anðeo Gospodnji reèe Filipu govoreæi: ustani i idi na podne na put koji silazi od Jerusalima u Gazu i pust je.
27 Ndipo ananyamuka napita, ndipo akuyenda anakumana ndi munthu wa ku Etiopia wa udindo waukulu woyangʼanira chuma cha Kandake, mfumu yayikazi ya ku Etiopia. Munthu ameneyu anapita ku Yerusalemu kukapembedza Mulungu,
I ustavši poðe. I gle, èovjek Arapin, uškopljenik, vlastelin Kandakije carice Arapske, što bješe nad svima njezinijem riznicama, koji bješe došao u Jerusalim da se moli Bogu,
28 ndipo akubwerera kwawo atakwera pa galeta lake amawerenga buku la mneneri Yesaya.
Pa se vraæaše, i sjedeæi na kolima svojijem èitaše proroka Isaiju.
29 Mzimu anamuwuza Filipo kuti, “Pita pa galeta ilo ndipo ukakhale pafupi nalo.”
A Duh reèe Filipu: pristupi i prilijepi se tijem kolima.
30 Pamenepo Filipo anathamangira ku galeta ndipo anamva munthuyo akuwerenga buku la mneneri Yesaya. Filipo anamufunsa kuti, “Kodi mukumvetsa zimene mukuwerengazi?”
A Filip pritrèavši èu ga gdje èita proroka Isaiju, i reèe: a razumiješ li što èitaš?
31 Iye anayankha kuti, “Ndingamvetse bwanji popanda wina wondimasulira?” Ndipo iye anayitana Filipo kuti abwere ndikukhala naye mʼgaleta.
A on reèe: kako bih mogao ako me ko ne uputi? I umoli Filipa te se pope i sjede s njim.
32 Mawu amene ndunayo imawerenga anali awa: “Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
A mjesto iz pisma koje èitaše bješe ovo: kao ovca na zaklanje odvede se, i nijem kao jagnje pred onijem koji ga striže, tako ne otvori usta svojijeh.
33 Iye ananyozedwa ndipo panalibe chilungamo pa mlandu wake. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo?”
U njegovom poniženju ukide se sud njegov. A rod njegov ko æe iskazati? Jer se njegov život uzima od zemlje.
34 Ndunayo inamufunsa Filipo kuti, “Chonde, uzeni, kodi mneneri akuyankhula za ndani, za iye mwini kapena za munthu wina?”
Onda uškopljenik odgovori Filipu i reèe: molim te, za koga ovo govori prorok? ili za sebe ili za koga drugoga?
35 Pamenepo Filipo anayambira pa malemba omwewo kumuwuza za Uthenga Wabwino wa Yesu.
A Filip otvorivši usta svoja, i poèevši od pisma ovoga, propovjedi mu jevanðelje Isusovo.
36 Akuyenda mu msewu anafika pamalo pamene panali madzi ndipo ndunayo inati, “Taonani madzi awa. Kodi pali chondiletsa kuti ndibatizidwe?”
Kako iðahu putem doðoše na nekaku vodu; i reèe uškopljenik: evo vode, šta brani meni da se krstim?
37 Filipo anati, “Ngati mukhulupirira ndi mtima wanu wonse mukhoza kubatizidwa.” Ndunayo inayankha kuti, “Ine ndikukhulupirira kuti Yesu Khristu ndi Mwana wa Mulungu.”
A Filip mu reèe: ako vjeruješ od svega srca svojega, možeš. A on odgovarajuæi reèe: vjerujem da je Isus Hristos sin Božij.
38 Ndipo analamulira galeta kuti liyime. Onse awiriwo, Filipo ndi Ndunayo anatsika ndi kulowa mʼmadzi ndipo Filipo anamubatiza.
I zapovjedi da stanu kola, i siðoše oba na vodu, i Filip i uškopljenik, i krsti ga.
39 Pamene iwo anatuluka mʼmadzimo, Mzimu wa Ambuye anamukwatula Filipo, ndipo Ndunayo sinamuonenso, koma inapitiriza ulendo wake ikusangalala.
A kad iziðoše iz vode, Duh sveti pade na uškopljenika, a anðeo Gospodnji uze Filipa, i više ga ne vidje uškopljenik; nego otide putem svojijem radujuæi se.
40 Koma Filipo anapezeka kuti ali ku Azoto ndipo anazungulira konse, kulalikira Uthenga Wabwino mʼmizinda yonse mpaka anakafika ku Kaisareya.
A Filip se obrete u Azotu; i prolazeæi propovijedaše jevanðelje svima gradovima, dok ne doðe u Æesariju.

< Machitidwe a Atumwi 8 >