< Machitidwe a Atumwi 7 >

1 Kenaka mkulu wa ansembe anafunsa Stefano kuti, “Kodi zimene akukunenerazi ndi zoona?”
A poglavar sveštenièki reèe: je li dakle tako?
2 Stefano anayankha kuti, “Abale ndi makolo, tamverani! Mulungu waulemerero anaoneka kwa kholo lathu Abrahamu pamene ankakhala ku Mesopotamiya, asanakakhale ku Harani.
A on reèe: ljudi braæo i oci! poslušajte. Bog slave javi se ocu našemu Avraamu kad bješe u Mesopotamiji, prije nego se doseli u Haran,
3 Mulungu anati, ‘Tuluka mʼdziko lako, siya abale ako, ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.’
I reèe mu: iziði iz zemlje svoje i od roda svojega i iz doma oca svojega, i doði u zemlju koju æu ti ja pokazati.
4 “Ndipo iye anatulukadi mʼdziko la Akaldeya ndi kukakhala ku Harani. Atamwalira abambo ake, Mulungu anamuchotsa kumeneko ndi kumubweretsa mʼdziko lino limene inu mukukhalamo tsopano.
Tada iziðe iz zemlje Haldejske, i doseli se u Haran; i odande, po smrti oca njegova, preseli ga u ovu zemlju u kojoj vi sad živite.
5 Mulungu sanamupatse cholowa kuno, ngakhale kadera kakangʼono kadziko. Koma Mulungu anamulonjeza kuti adzapereka dziko lino kwa iye ndi kwa zidzukulu zake, ngakhale kuti pa nthawi imeneyi analibe mwana.
I ne dade mu našljedstva u njoj ni stope; i obreèe mu je dati u držanje i sjemenu njegovu poslije njega, dok on još nemaše djeteta.
6 Mulungu anayankhula motere kwa iye: ‘Zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo, ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.’
Ali Bog reèe ovako: sjeme tvoje biæe došljaci u zemlji tuðoj, i natjeraæe ga da služi, i muèiæe ga èetiri stotine godina.
7 Mulungu anati, ‘Ine ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo, ndipo pambuyo pake akadzatuluka mʼdzikolo adzandipembedza Ine pamalo pano.’
I narodu kome æe služiti ja æu suditi, reèe Bog; i potom æe iziæi, i služiæe meni na ovome mjestu.
8 Kenaka Mulungu anachita pangano la mdulidwe ndi Abrahamu. Ndipo Abrahamu, anabereka Isake, namudula ali ndi masiku asanu ndi atatu. Ndipo Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka makolo khumi ndi awiri aja.
I dade mu zavjet obrezanja, i tako rodi Isaka, i obreza ga u osmi dan; i Isak Jakova, i Jakov dvanaest starješina.
9 “Makolo athu anachita nsanje ndi Yosefe ndipo anamugulitsa kuti akakhale kapolo ku Igupto. Koma Mulungu anali naye
I starješine zaviðahu Josifu, i prodadoše ga u Misir; i Bog bješe s njim.
10 ndipo anamupulumutsa iye kumasautso ake onse. Mulungu anamupatsa Yosefe nzeru ndi chisomo pamaso pa Farao mfumu ya ku Igupto, kotero mfumuyo inamuyika iye kukhala nduna yayikulu ya dziko la Igupto ndiponso nyumba yake yonse yaufumu.
I izbavi ga od sviju njegovijeh nevolja, i dade mu milost i premudrost pred Faraonom carem Misirskijem, i postavi ga poglavarom nad Misirom i nad svijem domom svojijem.
11 “Kenaka munalowa njala mʼdziko la Kanaani, kotero kuti anthu anavutika kwambiri, ndipo makolo athu sanathe kupeza chakudya.
A doðe glad na svu zemlju Misirsku i Hanaansku i nevolja velika, i ne nalažahu hrane oci naši.
12 Pamene Yakobo anamva kuti ku Igupto kunali tirigu, iye anatuma makolo athu ulendo woyamba.
A Jakov èuvši da ima pšenice u Misiru posla najprije oce naše.
13 Pa ulendo wawo wachiwiri, Yosefe anadziwulula kwa abale akewo ndipo Farao anadziwa za banja la Yosefe.
I kad doðoše drugi put, poznaše Josifa braæa njegova, i rod Josifov posta poznat Faraonu.
14 Izi zinachitika, Yosefe anayitanitsa abambo ake Yakobo ndi banja lonse, onse pamodzi analipo 75.
A Josif posla i dozva oca svojega Jakova i svu rodbinu svoju, sedamdeset i pet duša.
15 Motero Yakobo anapita ku Igupto, kumene iye ndiponso makolo athu anamwalira.
I Jakov siðe u Misir, i umrije, on i ocevi naši.
16 Mitembo yawo anayinyamula ndi kupita nayo ku Sekemu kumene inayikidwa mʼmanda amene Abrahamu anagula kochokera kwa ana a Hamori ku Sekemuko.
I prenesoše ih u Sihem, i metnuše u grob koji kupi Avraam za novce od sinova Emorovijeh u Sihemu.
17 “Nthawi itayandikira yakuti Mulungu achite zimene analonjeza kwa Abrahamu, mtundu wathu unakula ndi kuchuluka kwambiri mu Igupto.
I kad se približi vrijeme obeæanja za koje se Bog zakle Avraamu, narod se narodi i umnoži u Misiru,
18 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
Dok nasta drugi car u Misiru, koji ne znaše Josifa.
19 Mfumuyo inachita mwachinyengo ndi mtundu wathu ndi kuwazunza kuti ataye ana awo akhanda kuti afe.
Ovaj namisli zlo za naš rod, izmuèi oce naše da svoju djecu bacahu da ne žive.
20 “Pa nthawi imeneyo Mose anabadwa, ndipo anali wokongola kwambiri. Iye analeredwa mʼnyumba ya abambo ake kwa miyezi itatu.
U to se vrijeme rodi Mojsije, i bješe Bogu ugodan, i bi tri mjeseca hranjen u kuæi oca svojega.
21 Atakamutaya, mwana wamkazi wa Farao anamutola nakamulera ngati mwana wake.
A kad ga izbaciše, uze ga kæi Faraonova, i odgaji ga sebi za sina.
22 Mose anaphunzira nzeru zonse za Aigupto, ndipo anali wamphamvu mʼmawu ndi ntchito zake.
I nauèi se Mojsije svoj premudrosti Misirskoj, i bješe silan u rijeèima i u djelima.
23 “Mose ali ndi zaka makumi anayi, anaganizira zokayendera abale ake Aisraeli.
A kad mu se navršivaše èetrdeset godina, doðe mu na um da obiðe braæu svoju, sinove Izrailjeve.
24 Iye ataona mmodzi wa iwo akuzunzidwa ndi Mwigupto, anatchinjiriza Mwisraeliyo, namupha Mwiguptoyo.
I vidjevši jednome gdje se èini nepravda, pomože, i pokaja onoga što mu se èinjaše nepravda, i ubi Misirca.
25 Mose anaganiza kuti abale ake adzazindikira kuti Mulungu anamuyika kuti awapulumutse koma iwo sanazindikire.
Mišljaše pak da braæa njegova razumiju da Bog njegovom rukom njima spasenije dade: ali oni ne razumješe.
26 Mmawa mwake Mose anaona Aisraeli awiri akukangana. Iye anayesa kuwayanjanitsa ponena kuti, ‘Amuna inu, ndinu abale; chifukwa chiyani mukufuna kupwetekana?’
A sjutradan doðe meðu takove koji se bijahu svadili, i miraše ih govoreæi: ljudi, vi ste braæa, zašto èinite nepravdu jedan drugome?
27 “Koma munthu amene amavutitsa mnzakeyo anakankha Mose ndipo anati, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza.
A onaj što èinjaše nepravdu bližnjemu oturi ga govoreæi: ko je tebe postavio knezom i sudijom nad nama?
28 Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja dzulo?’
Ili i mene hoæeš da ubiješ kao što si juèe ubio Misirca?
29 Mose atamva mawu awa anathawira ku Midiyani, kumene anakhala mlendo ndipo anabereka ana amuna awiri.
A Mojsije pobježe od ove rijeèi, i posta došljak u zemlji Madijamskoj, gdje rodi dva sina.
30 “Ndipo patapita zaka makumi anayi mngelo anaonekera kwa Mose mʼmalawi amoto pa chitsamba mʼchipululu pafupi ndi Phiri la Sinai.
I kad se navrši èetrdeset godina, javi mu se u pustinji gore Sinajske anðeo Gospodnji u plamenu ognjenom u kupini.
31 Iye ataona zimenezi, anadabwa. Akupita kuti akaonetsetse pafupi, Mose anamva mawu a Ambuye:
A kad Mojsije vidje, divljaše se utvari. A kad on pristupi da vidi, bi glas Gospodnji k njemu:
32 ‘Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.’ Mose ananjenjemera chifukwa cha mantha ndipo sanalimbe mtima kuyangʼananso.
Ja sam Bog otaca tvojijeh, Bog Avraamov i Bog Isakov i Bog Jakovljev. A Mojsije se bješe uzdrktao i ne smijaše da pogleda.
33 “Ndipo Ambuye anati kwa Mose, ‘Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.
A Gospod mu reèe: izuj obuæu sa svojijeh nogu: jer je mjesto na kome stojiš sveta zemlja.
34 Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse. Tsopano tiye ndikutume ku Igupto.’
Ja dobro vidjeh muku svojega naroda koji je u Misiru, i èuh njihovo uzdisanje, i siðoh da ih izbavim: i sad hodi da te pošljem u Misir.
35 “Uyu ndi Mose yemwe uja amene Aisraeli anamukana ndi kunena kuti, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza?’ Iyeyo anatumidwa ndi Mulungu mwini kuti akakhale wowalamulira ndiponso mpulumutsi, mothandizidwa ndi mngelo amene anamuonekera pa chitsamba.
Ovoga Mojsija, kojega oturiše rekavši: ko te postavi knezom i sudijom? ovoga Bog za kneza i izbavitelja posla rukom anðela koji mu se javi u kupini.
36 Iye anawatulutsa mu Igupto ndipo anachita zodabwitsa ndi zizindikiro zozizwitsa mu Igupto, pa Nyanja Yofiira, ndiponso mʼchipululu kwa zaka makumi anayi.
Ovaj ih izvede uèinivši èudesa i znake u zemlji Misirskoj i u Crvenom Moru i u pustinji èetrdeset godina.
37 “Uyu ndi Mose uja amene anati kwa Aisraeli, ‘Mulungu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine.’
Ovo je Mojsije koji kaza sinovima Izrailjevijem: Gospod Bog vaš podignuæe vam proroka iz vaše braæe, kao mene: njega poslušajte.
38 Iyeyu anali mʼgulu la Aisraeli mʼchipululu pamodzi ndi mngelo amene anamuyankhula pa phiri la Sinai ndiponso makolo athu; ndipo Mose analandira mawu amoyo kuti atipatse ife.
Ovo je onaj što bješe u crkvi u pustinji s anðelom, koji mu govori na gori Sinajskoj, i s ocima našijem; koji primi rijeèi žive da ih nama da;
39 “Koma makolo athu anakana kumumvera iye. Iwo anamukana iye ndipo mʼmitima mwawo anatembenukira ku Igupto.
Kojega ne htješe poslušati oci naši, nego ga odbaciše, i okrenuše se srcem svojijem u Misir,
40 Iwo anati kwa Aaroni, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitsogolera kutuluka mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.
Rekavši Aronu: naèini nam bogove koji æe iæi pred nama, jer ovome Mojsiju, koji nas izvede iz zemlje Misirske, ne znamo šta bi.
41 Iyi ndi nthawi imene anapanga fano la mwana wangʼombe. Anapereka nsembe kwa fanoli nachita chikondwerero kulemekeza ntchito ya manja awo.
I tada naèiniše tele, i prinesoše žrtvu idolu, i radovahu se rukotvorini svojoj.
42 Koma Mulungu anawafulatira, nawapereka kuti apembedze zolengedwa zakumwamba. Zimenezi zikugwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la aneneri kuti, “‘Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?’
A Bog se okrenu od njih, i predade ih da služe vojnicima nebeskijem, kao što je pisano u knjizi proroka: eda zaklanja i žrtve prinesoste mi za èetrdeset godina u pustinji, dome Izrailjev?
43 Ayi, inu mwanyamula tenti ya Moloki ndi nyenyezi ya mulungu wanu Refani, mafano amene munapanga kuti muziwapembedza. Chifukwa chake, Ine ndidzakutumizani kutali, kupitirira dziko la Babuloni.
I primiste èador Molohov, i zvijezdu boga svojega Remfana, kipove koje naèiniste da im se molite; i preseliæu vas dalje od Vavilona.
44 “Makolo athu anali ndi tenti ya msonkhano pakati pawo mʼchipululu. Anayipanga monga momwe Mulungu anawuzira Mose, molingana ndi chithunzi chimene Mose anachiona.
Ocevi naši imahu èador svjedoèanstva u pustinji, kao što zapovjedi onaj koji govori Mojsiju da ga naèini po onoj prilici kao što ga vidje;
45 Makolo athu, atayilandira Tentiyo, anabwera nayo motsogozedwa ndi Yoswa pamene analanda dziko la mitundu imene Mulungu anayipirikitsa pamaso pawo. Tentiyo inakhala mʼdzikomo mpaka nthawi ya Davide,
Koji i primiše ocevi naši i donesoše s Isusom Navinom u zemlju neznabožaca, koje oturi Bog ispred lica našijeh otaca, tja do Davida,
46 amene anapeza chisomo pamaso pa Mulungu ndipo anapempha kuti amʼmangire nyumba Mulungu wa Yakobo.
Koji naðe milost u Boga, i izmoli da naðe mjesto Bogu Jakovljevu.
47 Koma anali Solomoni amene anamanga nyumbayo.
A Solomun mu naèini kuæu.
48 “Komatu, Wammwambamwambayo sakhala mʼnyumba zomangidwa ndi anthu. Monga mneneri akunena kuti,
Ali najviši ne živi u rukotvorenijem crkvama, kao što govori prorok:
49 “‘Kumwamba ndi mpando wanga waufumu, ndipo dziko lapansi ndi chopondapo mapazi anga. Kodi mudzandimangira nyumba yotani? Akutero Ambuye. Kapena malo opumuliramo Ine ali kuti?
Nebo je meni prijestol a zemlja podnožje nogama mojima: kako æete mi kuæu sazidati? govori Gospod; ili koje je mjesto za moje poèivanje?
50 Kodi si dzanja langa linapanga zonsezi?’
Ne stvori li ruka moja sve ovo?
51 “Anthu wokanika inu, osachita mdulidwe wa mu mtima ndi a makutu ogontha! Inu ofanana ndi makolo anu. Nthawi zonse mumakana kumvera Mzimu Woyera:
Tvrdovrati i neobrezanijeh srca i ušiju! vi se jednako protivite Duhu svetome; kako vaši oci, tako i vi.
52 Kodi analipo mneneri amene makolo anu sanamuzunze? Iwo anapha ngakhale amene ananeneratu za kubwera kwa Wolungamayo. Ndipo tsopano inu munamupereka ndi kumupha Iye.
Kojega od proroka ne protjeraše oci vaši? I pobiše one koji naprijed javiše za dolazak pravednika, kojega vi sad izdajnici i krvnici postadoste;
53 Inu amene munalandira Malamulo amene anaperekedwa ndi angelo ndipo simunawamvere.”
Koji primiste zakon naredbom anðelskom, i ne održaste.
54 Atamva zimenezi, iwo anakwiya kwambiri ndipo anamukukutira mano.
Kad ovo èuše, rasrdiše se vrlo u srcima svojima, i škrgutahu zubima na nj.
55 Koma Stefano, wodzaza ndi Mzimu Woyera, anayangʼana kumwamba ndipo anaona ulemerero wa Mulungu ndiponso Yesu atayimirira ku dzanja lamanja la Mulungu.
A Stefan buduæi pun Duha svetoga pogleda na nebo i vidje slavu Božiju i Isusa gdje stoji s desne strane Bogu;
56 Stefano anati, “Taonani, ndikuona kumwamba kotsekuka ndiponso Mwana wa Munthu atayimirira ku dzanja la manja la Mulungu.”
I reèe: evo vidim nebesa otvorena i sina èovjeèijega gdje stoji s desne strane Bogu.
57 Koma iwo anatseka mʼmakutu mwawo, ndipo anafuwula kolimba, onse anathamangira kwa iye,
A oni povikavši iza glasa zatiskivahu uši svoje, i navališe jednodušno na nj.
58 anamukokera kunja kwa mzinda ndipo anayamba kumugenda miyala. Mboni zinasungitsa zovala zawo kwa mnyamata otchedwa Saulo.
I izvedavši ga iz grada stadoše ga zasipati kamenjem, i svjedoci haljine svoje metnuše kod nogu mladiæa po imenu Savla.
59 Akumugenda miyala, Stefano anapemphera kuti, “Ambuye Yesu, landirani mzimu wanga.”
I zasipahu kamenjem Stefana, koji se moljaše Bogu i govoraše: Gospode Isuse! primi duh moj.
60 Ndipo anagwada pansi nafuwula mwamphamvu kuti, “Ambuye musawawerengere tchimoli.” Atanena mawu amenewa anamwalira.
Onda kleèe na koljena i povika iza glasa: Gospode! ne primi im ovo za grijeh. I ovo rekavši umrije.

< Machitidwe a Atumwi 7 >