< 2 Mafumu 16 >

1 Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
In the seuententhe yeer of Phacee, sone of Romelie, Achaz, the sone of Joathan, kyng of Juda, regnyde.
2 Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
Achaz was of twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnyde sixtene yeer in Jerusalem; he dide not that, that was plesaunt in the siyt of his Lord God, as Dauid, his fadir dide, but he yede in the weie of the kyngis of Israel.
3 Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
Ferthermore and he halewide his sone, and bar thorouy the fier, bi the idols of hethene men, whiche the Lord distriede bifore the sones of Israel.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
And he offride sacrifices, and brente encense in hiy placis, and in hillis, and vndur ech tree ful of bowis.
5 Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
Thanne Rasyn, kyng of Sirye, and Phacee, sone of Romelie, kyng of Israel, stiede in to Jerusalem to fiyte; and whanne thei bisegide Achaz, thei miyten not ouercome hym.
6 Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
In that tyme Rasyn, kyng of Sirie, restoride Ahila to Sirie, and castide out Jewis fro Ahila; and Ydumeis and men of Sirie camen into Ahila, and dwelliden there til in to this dai.
7 Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
Forsothe Achaz sente messangeris to Teglat Phalasar, kyng of Assiriens, and seide, Y am thi seruaunt and thi sone; stie thou, and make me saaf fro the hond of the kyng of Sirie, and fro the hond of the kyng of Israel, that han rise togidere ayens me.
8 Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
And whanne Achaz hadde gaderide togidere siluer and gold, that myyte be foundun in the hows of the Lord, and in the tresours of the kyng, he sente yiftis to the kyng of Assiriens;
9 Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
whiche assentide to his wille. Sotheli the kyng of Asseriens stiede in to Damask, and wastide it, and translatide the dwelleris therof to Sirenen; sotheli he killide Rasyn.
10 Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
And kyng Achaz yede in to metyng to Teglat Phalasaar, kyng of Assiriens; and whanne kyng Achaz hadde seyn the auter of Damask, he sent to Vrie, the preest, the saumpler and licnesse therof, bi al the werk therof.
11 Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
And Vrie, the preest, bildide an auter bi alle thingis whiche king Achaz hadde comaundid fro Damask, so dide the preest Vrie, til kyng Achaz cam fro Damask.
12 Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
And whanne the king cam fro Damask, he siy the auter, and worschipide it; and he stiede, and offride brent sacrifices, and his sacrifice;
13 Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
and he offride moist sacrifices, and he schedde the blood of pesible thingis, which he hadde offrid on the auter.
14 Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
Forsothe he dide awei the brasun auter, that was bifor the Lord, fro the face of the temple, and fro the place of the auter, and fro the place of the temple of the Lord; and settide it on the side of the auter `at the north.
15 Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
Also kyng Achaz comaundide to Vrie, the preest, and seide, Offre thou on the more auter the brent sacrifice of the morewtid, and the sacrifice of euentid, and the brent sacrifice of the king, and the sacrifice of hym, and the brent sacrifice of al the puple of the lond, and the sacrifices of hem, and the moist sacrifices of hem; and thou schalt schede out on that al the blood of brent sacrifice, and al the blood of slayn sacrifice; sotheli the brasun auter schal be redi at my wille.
16 Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
Therfor Vrie, the preest, dide bi alle thingis whiche kyng Achaz hadde comaundid to hym.
17 Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
Forsothe kyng Achaz took the peyntid foundementis, and the waischyng vessel, that was aboue, and he puttide doun the see, that is, the waischung vessel `for preestis, fro the brasun oxis, that susteyneden it, and he settide on the pawment araied with stoon.
18 Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
Also he turnede the tresorie of sabat, which he hadde bildid in the temple, and `he turnede the entryng of the kyng with outforth, in to the temple of the Lord for the kyng of Assiriens.
19 Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Forsothe the residue of wordis of Achaz, and alle thingis whiche he dide, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kyngis of Juda?
20 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Achaz slepte with hise fadris, and was biried with hem in the citee of Dauid; and Ezechie, his sone, regnede for hym.

< 2 Mafumu 16 >