< 2 Mbiri 24 >

1 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
Bijaše Joasu sedam godina kad se zacari, i carova èetrdeset godina u Jerusalimu. Materi mu bješe ime Sivija iz Virsaveje.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
I èinjaše Joas što je pravo pred Gospodom dokle god bijaše živ Jodaj sveštenik.
3 Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
I Jodaj ga oženi dvjema ženama, te rodi sinove i kæeri.
4 Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
Potom Joas naumi da opravi dom Gospodnji.
5 Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
I sazva sveštenike i Levite, pa im reèe: poðite po gradovima Judinijem i kupite od svega Izrailja novaca da se opravlja dom Boga vašega od godine do godine, i vi pohitajte s tijem. Ali ne hitješe Leviti.
6 Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
Zato car dozva Jodaja poglavara i reèe mu: zašto ne nastojiš da Leviti donose iz Judeje i Jerusalima priloge koje je naredio Mojsije sluga Gospodnji zboru Izrailjevu na šator od sastanka?
7 Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
Jer bezbožna Gotolija i sinovi njezini oplijeniše dom Gospodnji i sve stvari posveæene domu Gospodnjemu obratiše na Vale.
8 Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
I tako zapovjedi car te naèiniše kovèeg, i metnuše ga na vrata doma Gospodnjega spolja.
9 Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
I oglasiše po Judeji i po Jerusalimu da donose Gospodu prilog koji je naredio Mojsije sluga Božji Izrailju u pustinji.
10 Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
I obradovaše se knezovi i sav narod, i donoseæi metahu u kovèeg dokle se ne svrši.
11 Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
I kad donošahu Leviti kovèeg po zapovijesti carevoj, vidjevši da ima mnogo novaca, dolažaše pisar carev i poslanik poglavara sveštenièkoga, te izruèivahu kovèeg, potom ga opet odnošahu i ostavljahu na njegovo mjesto; i tako èinjahu svaki dan, i nakupiše mnogo novaca.
12 Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
I davaše ga car Jodaj nastojnicima nad poslom oko doma Gospodnjega, a oni naimahu kamenare i drvodjelje da se obnovi dom Gospodnji, i kovaèe koji rade od gvožða i od mjedi, da se opravi dom Gospodnji.
13 Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
I poslovahu poslenici, i opravljanje napredovaše pod njihovijem rukama, te povratiše domu Božijemu oblièje njegovo, i utvrdiše ga.
14 Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
A kad svršiše, donesoše pred cara i Jodaja novce što pretekoše; i od toga naèini sudove za dom Gospodnji, sudove za službu i za žrtve, i kadionice, i druge sudove zlatne i srebrne. I tako prinošahu žrtve paljenice u domu Gospodnjem jednako svega vijeka Jodajeva.
15 Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
Potom ostarjevši Jodaj sit života umrije; sto i trideset godina bješe mu kad umrije.
16 Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
I pogreboše ga u gradu Davidovu kod careva; jer èinjaše dobro Izrailju i Bogu i domu njegovu.
17 Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
A kad umrije Jodaj, doðoše knezovi Judini i pokloniše se caru; tada ih posluša car,
18 Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
Te ostaviše dom Gospoda Boga otaca svojih, i stadoše služiti lugovima i idolima; i podiže se gnjev Gospodnji na Judu i na Jerusalim za taj grijeh njihov.
19 Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
I slaše im proroke da ih vrate ka Gospodu, i oni im svedoèahu, ali ih ne poslušaše.
20 Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
I doðe duh Gospodnji na Zahariju sina Jodaja sveštenika, te stade više naroda i reèe im: ovako veli Bog: zašto prestupate zapovijesti Gospodnje? neæete biti sreæni; što ostaviste Gospoda, zato i on vas ostavi.
21 Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
A oni se pobuniše na nj, i zasuše ga kamenjem po zapovijesti carevoj u trijemu doma Gospodnjega.
22 Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
I ne opomenu se Joas milosti koju mu uèini Jodaj otac njegov, nego ubi sina njegova; a on umiruæi reèe: Gospod neka vidi i traži.
23 Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
A kad proðe godina, podiže se na nj vojska Sirska i uðe u zemlju Judejsku i u Jerusalim, i pobiše po narodu sve knezove narodne, i sav plijen od njih poslaše caru u Damasak.
24 Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
Ako i mala bješe vojska Sirska koja doðe, ipak Gospod dade u ruke njihove vrlo veliku vojsku, jer bjehu ostavili Gospoda Boga otaca svojih. I tako na Joasu izvršiše sud.
25 Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
A kad otidoše od njega ostavivši ga u teškoj bolesti, pobuniše se na nj sluge njegove za krv sinova Jodaja sveštenika, i ubiše ga na postelji njegovoj, te pogibe; i pogreboše ga u gradu Davidovu, ali ga ne pogreboše u grobovima carskim.
26 Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
A ovo su što se pobuniše na nj: Zavad sin Simeate Amonke i Jozavad sin Simrite Moavke.
27 Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
A o sinovima njegovijem i o velikoj porezi što bi pod njim, i o graðenju doma Božijega, eto zapisano je u knjizi o carevima. A zacari se na njegovo mjesto Amasija sin njegov.

< 2 Mbiri 24 >