< 2 Mbiri 23 >

1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
A sedme godine oslobodi se Jodaj, i uze k sebi stotinike Azariju sina Jeroamova i Ismaila sina Joananova i Azariju sina Ovidova i Masiju sina Adajeva i Elisafata sina Zihrijeva, i uhvati vjeru s njima,
2 Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
Te prolazeæi zemlju Judinu sabraše Levite iz svijeh gradova Judinijeh i glavare porodica otaèkih u Izrailju, i doðoše u Jerusalim.
3 msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
I sav zbor uèini vjeru u domu Božijem s carem; i Jodaj im reèe: evo, sin æe carev carovati, kao što je rekao Gospod za sinove Davidove.
4 Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
Ovo uèinite: treæina vas koji dolazite u subotu izmeðu sveštenika i Levita neka budu vratari na pragu;
5 ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
A druga treæina neka bude u carskom dvoru; a ostala treæina na vratima od temelja, a sav narod u trijemovima doma Gospodnjega.
6 Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
Niko da ne ulazi u dom Gospodnji osim sveštenika i onijeh Levita koji služe; oni neka ulaze, jer su posveæeni, a sav narod neka èini što je Gospod zapovjedio da èini.
7 Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
I Leviti neka opkole cara svaki s oružjem svojim u ruci; i ko bi god ušao u dom, da se pogubi; i budite uz cara kad stane ulaziti i izlaziti.
8 Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
I uèiniše Leviti i sav narod Judin sve što zapovjedi sveštenik Jodaj; i uzeše svaki svoje ljude koji dolažahu u subotu i koji odlažahu u subotu; jer Jodaj sveštenik ne otpusti redova.
9 Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
I dade Jodaj sveštenik stotinicima koplja i štitove i štitiæe cara Davida što bijahu u domu Božijem.
10 Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
I postavi sav narod sve s oružjem u ruku, od desne strane doma do lijeve prema oltaru i prema domu, oko cara.
11 Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
Tada izvedoše sina careva, i metnuše mu na glavu vijenac, i daše mu svjedoèanstvo, i zacariše ga, i Jodaj i sinovi njegovi pomazaše ga i rekoše: da živi car!
12 Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
A kad Gotolija èu viku naroda koji se stjecaše i hvaljaše cara, doðe k narodu u dom Gospodnji.
13 Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
I pogleda, i gle, car stajaše kod svojega stupa na ulasku, a knezovi i trube oko cara, i sav narod zemaljski radovaše se i trube trubljahu i pjevaèi pjevahu uz oruða muzièka i oni koji poèinjahu u pjevanju. Tada razdrije Gotolija haljine svoje i povika: buna! buna!
14 Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
A Jodaj sveštenik zapovjedi da izidu stotinici koji bijahu nad vojskom, i reèe im: izvedite je iz vrsta napolje, i ko poðe za njom neka se pogubi maèem; jer reèe sveštenik: nemojte je ubiti u domu Gospodnjem.
15 choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
I naèiniše joj mjesto, te otide kako se ide vratima konjskim u dom carev, i ondje je pogubiše.
16 Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
Tada Jodaj uèini vjeru meðu sobom i svijem narodom i carem da æe biti narod Gospodnji.
17 Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
Potom sav narod otide u dom Valov, i raskopaše ga, i oltare njegove i likove njegove izlomiše, a Matana sveštenika Valova ubiše pred oltarima.
18 Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
I Jodaj uredi opet službu u domu Gospodnjem meðu sveštenicima i Levitima, koje David bješe odredio domu Gospodnjemu, da bi prinosili žrtve paljenice Gospodu, kao što piše u zakonu Mojsijevu, s veseljem i pjesmama po naredbi Davidovoj.
19 Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
Postavi i vratare na vratima doma Gospodnjega da ne bi ulazio neèist oda šta mu drago.
20 Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
I uze stotinike i znatnije ljude i koji upravljahu narodom, sav narod zemaljski, i izvede cara iz doma Gospodnjega i uðoše visokim vratima u dom carski, i posadiše cara na carski prijesto.
21 ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.
I radovaše se sav narod zemaljski, i grad se umiri, kad Gotoliju ubiše maèem.

< 2 Mbiri 23 >