< 1 Samueli 16 >

1 Yehova anati kwa Samueli, “Kodi udzamulira Sauli mpaka liti, popeza Ine ndamukana kuti akhale mfumu ya Israeli? Dzaza mafuta mʼbotolo lako ndipo unyamuke kupita kwa Yese wa ku Betelehemu popeza ndadzisankhira mmodzi mwa ana ake kukhala mfumu.”
A Gospod reèe Samuilu: dokle æeš ti plakati za Saulom kad ga ja odbacih da ne caruje više nad Izrailjem? Napuni rog svoj ulja, i hodi da te pošljem k Jeseju Vitlejemcu, jer izmeðu njegovijeh sinova izabrah sebi cara.
2 Koma Samueli anati, “Kodi ndingapite bwanji? Sauli akamva zimenezi adzandipha.” Yehova anayankha, “Tenga ngʼombe yayikazi ndipo ukanene kuti, ‘Ndabwera kudzapereka nsembe kwa Yehova.
A Samuilo reèe: kako da idem? jer æe èuti Saul, pa æe me ubiti. A Gospod odgovori: uzmi sa sobom junicu iz goveda, pa reci: doðoh da prinesem žrtvu Gospodu.
3 Ukamuyitane Yese ku mwambo wa nsembe, ndipo ine ndidzakuwuza choti ukachite. Ukandidzozere amene ndikakulozere.’”
I pozovi Jeseja na žrtvu, a ja æu ti pokazati šta æeš èiniti, i pomaži mi onoga koga ti kažem.
4 Samueli anachita zimene Yehova ananena, ndipo anabweradi ku Betelehemu kuja. Akuluakulu a mu mzindawo anamuchingamira ali njenjenje ndi mantha ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mwabwera mwa mtendere?”
I uèini Samuilo kako mu kaza Gospod, i doðe u Vitlejem; a starješine gradske uplašivši se istrèaše preda nj, i rekoše mu: jesi li došao dobro?
5 Samueli anayankha kuti, “Inde, kwabwino. Ndabwera kudzapereka nsembe kwa Yehova. Mudzipatule ndipo mubwere kudzapereka nsembe pamodzi nane.” Kenaka iye anamupatula Yese ndi ana ake aamuna ndipo anawayitana kudzapereka nsembe.
A on reèe: dobro; došao sam da prinesem žrtvu Gospodu; osveštajte se i hodite sa mnom na žrtvu. Pa osvešta i Jeseja i sinove njegove i pozva ih na žrtvu.
6 Pamene anafika, Samueli anaona Eliabu ndipo anaganiza “Ndithu wodzozedwa wa Yehova uja ndi uyu wayima pamaso pakeyu.”
I kad doðoše vidjevši Elijava reèe: jamaèno je pred Gospodom pomazanik njegov.
7 Koma Yehova anati kwa Samueli, “Usaone maonekedwe ake kapena msinkhu wake, pakuti ndamukana iyeyu. Yehova sapenya zimene munthu amapenya. Anthu amapenya zakunja, koma Mulungu amapenya za mu mtima.”
Ali Gospod reèe Samuilu: ne gledaj na lice njegovo ni na visinu rasta njegova, jer sam ga odbacio; jer ne gledam na što èovjek gleda: èovjek gleda što je na oèima, a Gospod gleda na srce.
8 Kenaka Yese anayitana Abinadabu namubweretsa pamaso pa Samueli. Koma Samueli anati, “Yehova sanamusankhenso ameneyu.”
I dozva Jesej Avinadava, i reèe mu da ide pred Samuila. A on reèe: ni toga nije izabrao Gospod.
9 Ndipo Yese anayitana Sama, koma Samueli anati, “Ngakhale uyu Yehova sanamusankhe.”
Potom Jesej reèe Sami da ide. A on reèe: ni toga nije izabrao Gospod.
10 Pambuyo pake, Yese anayitana ana ake amuna asanu ndi awiri kuti apite kwa Samueli. Koma Samueli anati, “Yehova sanasankhe amenewa.”
Tako reèe Jesej te proðoše sedam sinova njegovijeh pred Samuila; a Samuilo reèe Jeseju: nije Gospod izabrao tijeh.
11 Tsono Samueli anafunsa Yese kuti, “Kodi awa ndi ana ako onse aamuna?” Yese anayankha kuti, “Ayi, alipo wina wamngʼono amene watsala, koma akuweta nkhosa.” Samueli anati, “Apite munthu akamutenge popeza sitipereka nsembe mpaka iye atabwera.”
Potom reèe Samuilo Jeseju: jesu li ti to svi sinovi? A on reèe: ostao je još najmlaði; eno ga, pase ovce. Tada reèe Samuilo Jeseju: pošlji, te ga dovedi, jer neæemo sjedati za sto dokle on ne doðe.
12 Choncho anatuma munthu kukamutenga ndipo anabwera naye. Iye anali wofiirira, wa maonekedwe abwino ochititsa kaso. Ndipo Yehova anati, “Mudzoze popeza ndi ameneyu.”
I posla, te ga dovede. A bijaše smeð, lijepijeh oèiju i lijepa stasa. I Gospod reèe: ustani, pomaži ga, jer je to.
13 Samueli anatenga botolo la mafuta ndi kumudzoza pamaso pa abale ake, ndipo Mzimu wa Yehova unabwera mwamphamvu pa Davide kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo. Pambuyo pake Samueli anabwerera ku Rama.
Tada Samuilo uze rog s uljem, i pomaza ga usred braæe njegove; i siðe duh Gospodnji na Davida i osta na njemu od toga dana. Potom usta Samuilo i otide u Ramu.
14 Nthawi imeneyo Mzimu wa Yehova unamuchokera Sauli, ndipo mzimu woyipa wochokera kwa Yehova unayamba kumuzunza.
A duh Gospodnji otide od Saula, i uznemiravaše ga zao duh od Gospoda.
15 Atumiki a Sauli anati, “Taonani mzimu woyipa wochokera kwa Mulungu ukukuzunzani.
I rekoše Saulu sluge njegove: gle, sada te uznemiruje zli duh Božiji.
16 Ndiyetu, inu mbuye wathu titumeni ife antchito anu kuti tikafune munthu wodziwa bwino kuyimba zeze. Tsono pamene mzimu woyipa wochokera kwa Mulungu wakufikirani, iye azidzayimba ndipo mudzakhala bwino.”
Neka gospodar naš zapovjedi slugama svojim koje stoje pred tobom, da potraže èovjeka koji zna udarati u gusle, pa kad te napadne zli duh Božji, neka udara rukom svojom, i odlakšaæe ti.
17 Choncho Sauli anati kwa atumiki ake, “Chabwino, kandipezereni munthu wodziwa bwino kuyimba ndipo mubwere naye kuno.”
I reèe Saul slugama svojim: potražite èovjeka koji zna dobro udarati u gusle, i dovedite mi ga.
18 Mmodzi mwa antchito ake anati, “Ine ndinaona mwana wa Yese wa ku Betelehemu. Ndiye munthu wodziwa bwino kuyimba, wolimba mtima, ngwazi pa nkhondo, wodziwa kuyankhula ndi wokongola. Ndipotu Yehova ali ndi iye.”
A jedan izmeðu sluga njegovijeh odgovori i reèe: evo, ja znam sina Jeseja Vitlejemca, koji umije dobro udarati u gusle, i hrabar je junak i ubojnik, i pametan je i lijep, i Gospod je s njim.
19 Ndipo Sauli anatumiza amithenga kwa Yese kukanena kuti, “Nditumizireni mwana wanu Davide, amene amaweta nkhosa.”
I Saul posla ljude k Jeseju i poruèi: pošlji mi Davida sina svojega koji je kod ovaca.
20 Choncho Yese anatenga bulu namunyamulitsa buledi, thumba la vinyo ndi mwana wambuzi mmodzi. Zonsezi anamupatsa mwana wake Davide kuti akapereke kwa Sauli.
A Jesej uze magarca i hljeba i mješinu vina i jedno jare, i posla Saulu po Davidu sinu svojemu.
21 Davide anafika kwa Sauli ndipo anayamba ntchito. Sauli anamukonda kwambiri Davide ndipo anamusandutsa wonyamula zida zake za nkhondo.
I David doðe k Saulu i izide preda nj, i omilje Saulu veoma, te ga postavi da mu nosi oružje.
22 Kenaka Sauli anatumiza mawu kwa Yese ndi kuti, “Mulole kuti Davide azinditumikira, pakuti ndamukonda kwambiri.”
Potom posla Saul k Jeseju i poruèi: neka David ostane kod mene, jer je našao milost preda mnom.
23 Nthawi zonse mzimu woyipa wochokera kwa Mulungu umati ukamufikira Sauli, Davide ankatenga zeze wake nʼkumamuyimbira. Choncho Sauli ankapeza bwino, ndipo mzimu woyipa uja unkamusiya.
I kad bi duh Božji napao Saula, David uzevši gusle udarao bi rukom svojom, te bi Saul odahnuo i bilo bi mu bolje, jer bi zli duh otišao od njega.

< 1 Samueli 16 >