< 1 Samueli 15 >

1 Samueli anawuza Sauli kuti, “Yehova anandituma ine kuti ndikudzozeni kukhala mfumu ya anthu ake, Aisraeli. Tsopano imvani zimene Yehova akunena.
A Samuilo reèe Saulu: Gospod me je poslao da te pomažem za cara nad narodom njegovijem, nad Izrailjem; slušaj dakle rijeèi Gospodnje.
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzalanga Aamaleki chifukwa cha zimene anawachita Aisraeli. Paja iwo analimbana ndi Aisraeli pa njira pamene Aisraeliwo ankachoka ku Igupto.
Ovako veli Gospod nad vojskama: opomenuh se šta je uèinio Amalik Izrailju, kako mu se opro na putu kad je išao iz Misira.
3 Tsopano pita kathire nkhondo Aamaleki ndi kuwononga kwathunthu zinthu zonse zimene ali nazo. Musakasiyeko munthu ndi mmodzi yemwe. Mukaphe amuna ndi akazi, ana ndi makanda, ngʼombe ndi nkhosa, ngamira ndi abulu.’”
Zato idi, i pobij Amalika, i zatri kao prokleto sve što god ima; ne žali ga, nego pobij i ljude i žene i djecu i što je na sisi i volove i ovce i kamile i magarce.
4 Kotero Sauli anayitana ankhondo ake nawawerenga ku Telaimu. Ankhondo oyenda pansi analipo 200,000 ndipo mwa iwowa 10,000 anali a fuko la Yuda.
Tada Saul sazva narod, i izbroji ih u Telaimu, i bješe ih dvjesta tisuæa pješaka i deset tisuæa ljudi od Jude.
5 Sauli anapita ku mzinda wa Aamaleki nawubisalira mʼkhwawa.
I doðe Saul do grada Amalièkoga, i namjesti zasjedu u potoku.
6 Tsono Sauli anawuza Akeni kuti, “Samukani, muchoke pakati pa Aamaleki kuti ine ndisakuwonongeni pamodzi ndi iwo pakuti inu munaonetsa kukoma mtima kwa Aisraeli onse pamene ankatuluka mʼdziko la Igupto,” Choncho Akeni anachoka pakati pa Aamaleki.
I reèe Saul Kenejima: idite, odvojte se, uklonite se od Amalika, da vas ne bih potro s njima; jer ste vi uèinili milost svijem sinovima Izrailjevijem kad su išli iz Misira. I otidoše Keneji od Amalika.
7 Tsono Sauli anakantha Aamaleki kuchokera ku Havila mpaka ku Suri, kummawa kwa Igupto.
I Saul pobi Amalike od Avile do Sura, koji je prema Misiru.
8 Sauli anatenga Agagi mfumu ya Aamaleki, koma anthu ake onse anawapha ndi lupanga.
I uhvati Agaga cara Amalièkoga živa, a sav narod njegov pobi oštrijem maèem.
9 Koma Sauli ndi ankhondo ake sanaphe Agagi, sanaphenso nkhosa ndi ngʼombe zabwino ngakhalenso ana angʼombe ndi ana ankhosa onenepa. Chilichonse chimene chinali chabwino sanachiphe. Koma zonse zimene zinali zoyipa ndi zachabechabe anaziwononga.
I Saul i narod njegov poštedje Agaga i najbolje ovce i najbolje volove i ugojenu stoku i jaganjce i sve što bijaše dobro, i ne htješe pobiti; nego što bijaše zlo i bez cijene, ono samo pobiše.
10 Kenaka Yehova anawuza Samueli kuti,
Zato doðe rijeè Gospodnja k Samuilu govoreæi:
11 “Ine ndikumva chisoni chifukwa ndinayika Sauli kukhala mfumu. Wabwerera mʼmbuyo, waleka kunditsata ndipo sanamvere malangizo anga.” Samueli anapsa mtima, ndipo analira kwa Yehova usiku wonse.
Kajem se što sam Saula postavio carem, jer je otstupio od mene, i nije izvršio mojih rijeèi. I rasrdi se Samuilo vrlo, i vikaše ka Gospodu svu noæ.
12 Samueli anadzuka mmamawa ndipo anapita kukakumana ndi Sauli. Koma anthu anamuwuza kuti, “Sauli anabwera ku Karimeli, ndipo kumeneko wadziyimikira mwala wachikumbutso cha iye mwini. Tsopano wachokako ndipo wapita ku Giligala.”
I ustavši rano Samuilo poðe pred Saula. I javiše Samuilu govoreæi: Saul doðe u Karmil, i eno podiže sebi spomenik, pa se vrati odande i otide dalje i siðe u Galgal.
13 Samueli atamupeza Sauli, Sauliyo anati kwa Samueli, “Yehova akudalitseni! Ndachita zonse zimene Yehova analamula.”
Kad Samuilo doðe k Saulu, reèe mu Saul: blagosloven da si Gospodu! izvršio sam rijeè Gospodnju.
14 Koma Samueli anati, “Nanga bwanji ndikumva kulira kwa nkhosa ndi ngʼombe?”
A Samuilo reèe: kakva je to bleka ovaca u ušima mojim? i rika volova koju èujem?
15 Sauli anayankha, “Zimenezi Asilikali azitenga kuchokera kwa Aamaleki. Iwo anasungako nkhosa ndi ngʼombe zabwino kuti akapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma zina zonse anaziwononga.”
A Saul reèe: od Amalika dognaše ih; jer narod poštedje najbolje ovce i najbolje volove da prinese na žrtvu Gospodu Bogu tvojemu; ostalo pak pobismo kao prokleto.
16 Koma Samueli anati kwa Sauli, “Khala chete! Ima ndikuwuze zimene Yehova wandiwuza usiku wathawu.” Sauli anayankha kuti, “Ndiwuzeni.”
A Samuilo reèe Saulu: stani da ti kažem što mi je rekao Gospod noæas. Reèe mu: govori.
17 Apo Samueli anati, “Munali wamngʼono pa maso pa anthu, koma tsopano mwasanduka mtsogoleri wa mafuko a Israeli. Yehova anakudzozani kuti mukhale mfumu yolamulira Aisraeli.
Tada reèe Samuilo: nijesi li bio mali sam u svojim oèima, pak si postao glava plemenima Izrailjevijem, i Gospod te pomaza za cara nad Izrailjem?
18 Ndipo Yehova anakutumani kuti, ‘Pitani mukawononge kwathunthu Aamaleki, anthu oyipa aja. Mukachite nawo nkhondo mpaka kuwatheratu.’
I Gospod te posla na ovaj put i reèe: idi, pobij grješne Amalike, i vojuj na njih dokle ih ne istrijebite.
19 Chifukwa chiyani simunamvere mawu a Yehova? Chifukwa chiyani munathamangira zofunkha ndi kuchita choyipira Yehova?”
Zašto dakle ne posluša glasa Gospodnjega, nego se naklopi na plijen, i uèini zlo pred Gospodom?
20 Koma Saulo anawuza Samueli kuti, “Ine ndinamveradi mawu a Yehova. Ndinapita kukachita zimene Yehova anandituma. Ndinabwera naye Agagi, mfumu ya Amaleki, koma Aamaleki ena onse anaphedwa.
A Saul odgovori Samuilu: ta poslušao sam glas Gospodnji, i išao sam putem kojim me posla Gospod, i doveo sam Agaga cara Amalièkoga, a Amalike sam istrijebio.
21 Koma pa zofunkhazo anthu anatengapo nkhosa, ngʼombe ndi zabwino zina zoyenera kuwonongedwa kuti akapereke ngati nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ku Giligala.”
Nego narod uze od plijena ovce i volove, najbolje izmeðu prokletijeh stvari, da prinese na žrtvu Gospodu Bogu tvojemu u Galgalu.
22 Koma Samueli anayankha kuti, “Kodi Yehova amakondwera ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zina kapena kumvera mawu a ake? Taona, kumvera ndi kwabwino kuposa nsembe, ndipo kutchera khutu ndi kwabwino kuposa kupereka mafuta a nkhosa.
Ali Samuilo reèe: zar su mile Gospodu žrtve paljenice i prinosi kao kad se sluša glas njegov? gle, poslušnost je bolja od žrtve i pokornost od pretiline ovnujske.
23 Pakuti kuwukira kuli ngati tchimo lowombeza, ndipo kukhala nkhutukumve kuli ngati tchimo lopembedza mafano. Chifukwa mwakana mawu a Yehova. Iyenso wakukana kuti iweyo ukhale mfumu.”
Jer je neposlušnost kao grijeh od èaranja, i nepokornost kao sujevjerstvo i idolopoklonstvo. Odbacio si rijeè Gospodnju, zato je i on tebe odbacio da ne budeš više car.
24 Tsono Sauli anati kwa Samueli, “Ine ndachimwa. Ndaphwanya malamulo a Yehova ndiponso malangizo anu. Ndinkaopa anthu ndipo ndinawamvera.
Tada reèe Saul Samuilu: zgriješio sam što sam prestupio zapovijest Gospodnju i tvoje rijeèi; jer pobojah se naroda i poslušah glas njegov.
25 Tsopano ndikukupemphani, khululukireni tchimo langa ndipo mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova.”
Nego sada oprosti mi grijeh moj, i vrati se sa mnom da se poklonim Gospodu.
26 Koma Samueli anawuza Sauli kuti, “Ine sindibwerera nawe. Inu mwakana mawu a Yehova. Choncho Iyenso wakukanani kuti musakhale mfumu yolamulira Aisraeli.”
A Samuilo reèe Saulu: neæu se vratiti s tobom, jer si odbacio rijeè Gospodnju, i zato je tebe Gospod odbacio da ne budeš više car nad Izrailjem.
27 Samueli akutembenuka kuti azipita, Sauli anagwira mpendero wa mkanjo wake, ndipo unangʼambika.
I Samuilo se okrete da ide, ali ga Saul uhvati za skut od plašta njegova, te se odadrije.
28 Samueli anati kwa iye, “Yehova wangʼamba ufumu wanu kuchoka kwa inu, ndipo waupereka kwa mnzanu woposa inu.
Tada mu reèe Samuilo: odadro je Gospod carstvo Izrailjevo od tebe danas, i dao ga bližnjemu tvojemu, koji je bolji od tebe.
29 Mulungu wa ulemerero wa Israeli sanama kapena kusintha maganizo ake; pakuti iye si munthu, kuti asinthe maganizo ake.”
I doista junak Izrailjev neæe slagati, niti æe se raskajati; jer nije èovjek da se kaje.
30 Sauli anati, “Ine ndachimwa. Komabe, chonde mundilemekeze pamaso pa akuluakulu, anthu anga, ndiponso pamaso pa Israeli. Mubwerere nane kuti ndikapembedze Yehova Mulungu wanu.”
A on reèe: zgriješio sam; ali mi sad uèini èast pred starješinama naroda mojega i pred Izrailjem, i vrati se sa mnom da se poklonim Gospodu Bogu tvojemu.
31 Pamenepo Samueli anabwerera ndi Sauli, ndipo Sauli anapembedza Yehova.
I vrativši se Samuilo otide za Saulom, i pokloni se Saul Gospodu.
32 Kenaka Samueli anati, “Bwera nayeni kuno Agagi, mfumu ya Amaleki ija.” Choncho Agagi anapita kwa Samueli mokondwa chifukwa ankaganiza kuti, “Ndithu zowawa za imfa zapita.”
Potom reèe Samuilo: dovedite mi Agaga cara Amalièkoga. I doðe k njemu Agag veseo, jer govoraše Agag: zaista, prošla je gorèina smrtna.
33 Koma Samueli anati, “Monga momwe lupanga lako linasandutsira amayi kukhala wopanda ana, momwemonso amayi ako adzakhala opanda mwana pakati pa amayi.” Ndipo Samueli anapha Agagi pamaso pa Yehova ku Giligala.
Ali Samuilo reèe: kako je tvoj maè uèinio te su žene ostale bez djece, tako æe ostati bez djece tvoja majka meðu ženama. I isijeèe Samuilo Agaga pred Gospodom u Galgalu.
34 Ndipo Samueli anapita ku Rama, koma Sauli anapita ku mudzi kwawo ku Gibeya wa Sauli.
Potom otide Samuilo u Ramu, a Saul otide kuæi svojoj u Gavaju Saulovu.
35 Samueli sanamuonenso Sauli mpaka imfa yake ngakhale kuti ankamulira Sauliyo. Yehova anamva chisoni kuti anasankha Sauli kuti akhale mfumu ya Israeli.
I Samuilo više ne vidje Saula do svoje smrti, i plakaše Samuilo za Saulom, što se Gospod pokaja što je postavio Saula carem nad Izrailjem.

< 1 Samueli 15 >