< 1 Samueli 13 >

1 Sauli analowa ufumu ali ndi zaka makumi atatu, ndipo analamulira Israeli kwa zaka 42.
Kad Saul bi car godinu dana a carova dvije godine nad Izrailjem
2 Nthawi ina Sauli anasankha Aisraeli 3,000. Mwa iwowa, 2,000 anali ndi Sauliyo ku Mikimasi ndi ku dziko la mapiri ku Beteli, ndipo 1,000 anali ndi Yonatani ku Gibeya ku Benjamini. Anthu ena onse otsala anawabweza kwawo.
Izabra sebi Saul tri tisuæe izmeðu sinova Izrailjevih; i bijahu kod Saula dvije tisuæe u Mihmasu i u gori Vetiljskoj, a jedna tisuæa s Jonatanom u Gavaji Venijaminovoj; a ostali narod raspusti u šatore njihove.
3 Yonatani anakantha mkulu wa ankhondo wa Afilisti ku Geba, ndipo Afilisti anamva kuti Aheberi awukira. Tsono Sauli anawuza amithenga kuti alize lipenga mʼdziko lonse la Israeli.
I Jonatan pobi stražu Filistejsku koja bješe u Gavaji, i èuše za to Filisteji. A Saul zapovjedi, te trubiše u trube po svoj zemlji govoreæi: neka èuju Jevreji.
4 Choncho Aisraeli onse anamva kuti Sauli wakantha mkulu wa ankhondo Wachifilisiti ndi kuti Afilisti anayipidwa nawo Aisraeli. Ndiye anthu anayitanidwa kuti abwere kwa Sauli ku Giligala.
I tako èu sav Izrailj gdje rekoše: pobi Saul stražu Filistejsku; i stoga Izrailj omrznu Filistejima. I sazvan bi narod za Saulom u Galgal.
5 Tsono Afilisti anasonkhana kuti amenyane ndi Aisraeli. Iwo anali ndi magaleta 3,000, okwera pa akavalo 2,000 ndiponso asilikali kuchuluka kwake ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Iwo anapita ndi kukamanga misasa yawo ku Mikimasi, kummawa kwa Beti-Aveni.
A Filisteji se skupiše da vojuju na Izrailja, trideset tisuæa kola i šest tisuæa konjika, i mnoštvo naroda kao pijesak na brijegu morskom; i izašavši stadoše u oko u Mihmasu, s istoka od Vet-Avena.
6 Pamene Aisraeli anaona kuti anali pamavuto akulu, poti anali atapanikizidwa kwambiri, anabisala mʼmapanga, mʼmaenje, mʼmatanthwe, mʼmakwalala ndi mʼzitsime.
I Izrailjci se vidješe u nevolji, jer narod bi pritiješnjen; te se sakri u peæine i u èeste i u kamenjake i u rasjeline i u jame.
7 Ahebri ena anawoloka Yorodani mpaka kukafika ku dziko la Gadi ndi ku Giliyadi. Koma Sauli anakhalabe ku Giligala ndipo ankhondo onse amene anali naye anali njenjenje ndi mantha.
A drugi Jevreji prijeðoše preko Jordana u zemlju Gadovu i Galadovu. A Saul još bijaše u Galgalu, i sav narod što iðaše za njim bijaše u strahu.
8 Saulo anadikirira masiku asanu ndi awiri, monga mwa nthawi imene ananena Samueli. Koma Samueli sanabwere ku Giligala, ndipo anthu anayamba kumuthawa Sauli uja.
I poèeka sedam dana do roka Samuilova. Ali Samuilo ne doðe u Galgal; te se narod stade razlaziti od njega.
9 Kotero iye anati, “Bwera nayoni nsembe yopsereza ndi nsembe ya chiyanjano.” Ndipo Sauli anapereka nsembe yopsereza.
Tada reèe Saul: dodajte mi žrtvu paljenicu i žrtve zahvalne. I prinese žrtvu paljenicu.
10 Atangomaliza kupereka nsembe, anangoona Samueli watulukira ndipo Sauli anapita kukamulonjera.
I kad prinese žrtvu paljenicu, gle, doðe Samuilo. I Saul izide mu na susret da ga pozdravi.
11 Samueli anafunsa kuti, “Nʼchiyani chimene wachita?” Sauli anayankha kuti, “Nditaona kuti anthu ayamba kundithawa, ndi kuti inu simunabwere pa nthawi munanena ija, ndiponso kuti Afilisti akusonkhana ku Mikimasi,
A Samuilo mu reèe: šta si uèinio? A Saul odgovori: kad vidjeh gdje se narod razlazi od mene, a ti ne doðe do roka, i Filisteji se skupili u Mihmasu,
12 ndinati, ‘Tsopano Afilisti abwera kudzandithira nkhondo ku Giligala kuno, chonsecho sindinapemphe Yehova kuti andikomere mtima.’ Motero ndinakakamizika kupereka nsembe yopsereza.”
Rekoh: sad æe udariti Filisteji na me u Galgal, a ja se još ne pomolih Gospodu; te se usudih i prinesoh žrtvu paljenicu.
13 Samueli anati, “Mwachita zopusa. Simunatsate zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muchite. Mukanazitsata, Yehova akanawukhazikitsa ufumu wanu mu Israeli mpaka kalekale.
Tada reèe Samuilo Saulu: ludo si radio što nijesi držao zapovijesti Gospoda Boga svojega, koju ti je zapovjedio; jer bi sada Gospod utvrdio carstvo tvoje nad Izrailjem dovijeka.
14 Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”
A sada carstvo tvoje neæe se održati. Gospod je našao sebi èovjeka po srcu svojemu, i njemu je zapovjedio Gospod da bude voð narodu njegovu, jer nijesi držao što ti je zapovjedio Gospod.
15 Kenaka Samueli anachoka ku Giligala ndi kupita ku Gibeyati ku dziko la Benjamini. Saulo anawerenga anthu amene anali naye ndipo analipo 600.
Potom diže se Samuilo i otide iz Galgala u Gavaju Venijaminovu. I Saul izbroji narod koji osta kod njega, i bješe ga do šest stotina ljudi.
16 Sauli ndi mwana wake Yonatani pamodzi ndi asilikali amene anali naye aja amakhala ku Geba ku dziko la Benjamini. Koma Afilisti anamanga misasa yawo ku Mikimasi.
I Saul i sin mu Jonatan i narod što bješe s njima, stajahu u Gavaji Venijaminovoj; a Filisteji stajahu u okolu u Mihmasu.
17 Ankhondo a Afilisti anatuluka mʼmisasa yawo mʼmagulu atatu. Gulu lina linapita ku Ofiri ku dziko la Suwala.
I izidoše tri èete iz okola Filistejskoga da plijene: jedna èeta udari putem k Ofri u zemlju Sovalsku;
18 Gulu lina linalunjika ku Beti-Horoni, ndipo gulu lachitatu linalunjika ku malire oyangʼanana ndi chigwa cha Zeboimu cha ku chipululu.
A druga èeta udari putem k Vet-Oronu; a treæa udari putem k meði koja gleda prema dolini Sevojimskoj u pustinju.
19 Nthawi imeneyo nʼkuti mulibe osula zitsulo mʼdziko lonse la Israeli, pakuti Afilisti anati, “Tisawalole Aheberi kudzipangira okha malupanga kapena mikondo!”
A u cijeloj zemlji Izrailjskoj ne bješe kovaèa, jer Filisteji rekoše: da ne bi gradili Jevreji maèeva ni kopalja.
20 Kotero Aisraeli onse amapita kwa Afilisti kukanoletsa mapulawo, makasu, nkhwangwa ndi zikwakwa zawo.
Zato slažahu svi Izrailjci k Filistejima kad koji šæaše poklepati raonik ili motiku ili sjekiru ili srp.
21 Mtengo wonolera mapulawo ndi makasu unali zigawo ziwiri za sekeli, mtengo wonolera zisonga ndi nkhwangwa unali gawo limodzi la Sekeli.
I bijahu se zatupili raonici i motike i vile troroge i sjekire, i same ostane trebaše zaoštriti.
22 Motero tsiku la nkhondolo panalibe lupanga kapena mkondo mʼdzanja la aliyense amene anatsatira Saulo ndi Yonatani. Koma Saulo ndi Yonatani, iwo okha ndiwo anali ndi zida.
Zato kad doðe vrijeme boju, ne naðe se maèa ni koplja ni u koga u narodu koji bješe sa Saulom i Jonatanom; samo bijaše u Saula i u Jonatana sina njegova.
23 Tsono gulu lina lankhondo la Chifilisti linapita kukalonda mpata wa Mikimasi.
I straža Filistejska izide u klanac kod Mihmasa.

< 1 Samueli 13 >