< 1 Samueli 12 >

1 Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani.
Tada reèe Samuilo svemu Izrailju: eto, poslušao sam glas vaš u svemu što mi rekoste, i postavih cara nad vama.
2 Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero.
I sada eto, car ide pred vama, a ja sam ostario i osijedio; i sinovi moji eto su meðu vama; i ja sam išao pred vama od mladosti svoje do danas.
3 Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”
Evo me; odgovorite mi pred Gospodom i pred pomazanikom njegovijem. Kome sam uzeo vola ili kome sam uzeo magarca? kome sam uèinio nasilje? kome sam uèinio krivo? ili iz èije sam ruke uzeo poklon, da bih stiskao oèi njega radi? pak æu vam vratiti.
4 Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”
A oni rekoše: nijesi nam uèinio sile niti si kome uèinio krivo, niti si uzeo što iz èije ruke.
5 Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.” Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”
Jošte im reèe: svjedok je Gospod na vas, i svjedok je pomazanik njegov danas, da nijeste našli ništa u mojim rukama. I rekoše: svjedok je.
6 Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto.
Tada reèe Samuilo narodu: Gospod je koji je postavio Mojsija i Arona, i koji je izveo oce vaše iz zemlje Misirske.
7 Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.
Sada dakle stanite da se prem s vama pred Gospodom za sva dobra što je èinio Gospod vama i vašim ocima.
8 “Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.
Pošto doðe Jakov u Misir, vikaše oci vaši ka Gospodu, i Gospod posla Mojsija i Arona, koji izvedoše oce vaše iz Misira i naseliše ih na ovom mjestu.
9 “Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu.
Ali zaboraviše Gospoda Boga svojega, te ih dade u ruke Sisari vojvodi Asorskom, i u ruke Filistejima, i u ruke caru Moavskomu, koji vojevaše na njih.
10 Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’
Ali vikaše ka Gospodu i rekoše: sagriješismo što ostavismo Gospoda i služismo Valima i Astarotama; ali sada izbavi nas iz ruku neprijatelja naših, pa æemo ti služiti.
11 Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.
I Gospod posla Jerovala i Vedana i Jeftaja i Samuila, i ote vas iz ruku neprijatelja vaših unaokolo, te živjeste bez straha.
12 “Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu.
Ali kad vidjeste Nasa cara Amonskoga gdje doðe na vas, rekoste mi: ne, nego car neka caruje nad nama, premda Gospod Bog vaš bješe car vaš.
13 Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu.
Sada dakle, eto cara kojega izabraste, kojega iskaste; evo, Gospod je postavio cara nad vama.
14 Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino.
Ako se uzbojite Gospoda, i njemu uzaslužite, i uzaslušate glas njegov i ne usprotivite se zapovijesti Gospodnjoj, tada æete i vi i car vaš koji caruje nad vama iæi za Gospodom Bogom svojim.
15 Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.
Ako li ne uzaslušate glasa Gospodnjega, nego se usprotivite zapovijesti Gospodnjoj, tada æe biti ruka Gospodnja protiv vas kao što je bila protiv otaca vaših.
16 “Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu!
Ali stanite sada jošte, i vidite ovu stvar veliku koju æe uèiniti Gospod pred vašim oèima.
17 Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”
Nije li danas žetva pšenièna? Ja æu prizvati Gospoda, i spustiæe gromove i dažd, da razumijete i vidite koliko je zlo što uèiniste pred Gospodom iskavši sebi cara.
18 Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
Tada Samuilo zavapi ka Gospodu, i Gospod spusti gromove i dažd u taj dan; i sav se narod poboja vrlo Gospoda i Samuila.
19 Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”
I reèe sav narod Samuilu: moli se za sluge svoje Gospodu Bogu svojemu da ne pomremo; jer dodasmo k svijem grijesima svojim zlo ištuæi sebi cara.
20 Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse.
Tada reèe Samuilo narodu: ne bojte se, vi ste uèinili sve ovo zlo; ali ne otstupajte od Gospoda, nego služite Gospodu svijem srcem svojim.
21 Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe.
Ne otstupajte; jer biste pošli za ništavim stvarima, koje ne pomažu, niti izbavljaju, jer su ništave.
22 Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake.
Jer Gospod neæe ostaviti naroda svojega radi velikoga imena svojega; jer Gospodu bi volja da vas uèini svojim narodom.
23 Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.
A meni ne dao Bog da zgriješim Gospodu i prestanem moliti se za vas; nego æu vas upuæivati na put dobar i prav.
24 Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani.
Samo se Bojte Gospoda i služite mu istinito, svijem srcem svojim, jer vidite, kakve je velike stvari uèinio za vas.
25 Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”
Ako li zlo ušèinite, propašæete i vi i car vaš.

< 1 Samueli 12 >