< 1 Mafumu 21 >

1 Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
Forsothe after these wordis, in that tyme, the vyner of Naboth of Jezrael, `that was in Jezrael, was bisidis the paleis of Achab, kyng of Samarye.
2 Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
Therfor Achab spak to Naboth, and seide, Yyue thou to me the vyner, that Y make to me a gardyn of wortis, for it is nyy, and nyy myn hows; and Y schal yyue to thee a betere vyner for it; ethir if thou gessist it more profitable to thee, Y schall yyue the prijs of siluer, as myche as it is worth.
3 Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
To whom Naboth answeride, The Lord be merciful to me, that Y yyue not to thee the eritage of my fadris.
4 Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
Therfor Acab cam in to his hows, hauynge indignacioun, and gnastyng on the word which Naboth of Jezrael hadde spoke to him, and seide, Y schal not yyue to thee the eritage of my fadirs. And Achab castide doun him silf in to his bed, and turnede awei his face to the wal, and ete not breed.
5 Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
Forsothe Jezabel, his wijf, entride to hym, and seide to hym, What is this thing, wherof thi soule is maad sory? and whi etist thou not breed?
6 Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
Which answeride to hir, Y spak to Naboth of Jezrael, and Y seide to hym, Yyue thi vyner to me for money takun, ethir if it plesith thee, Y schal yyue to thee a betere vyner for it. And he seide, Y schal not yyue to thee my vyner.
7 Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
Therfor Jezabel, his wijf, seide to hym, Thou art of greet auctorite, and thou gouernest wel Israel; rise thou, and ete breed, and be thou `pacient, ethir coumfortid; Y schal yyue to thee the vyner of Naboth of Jezrael.
8 Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
Therfor sche wroot lettris in the name of Achab, and seelide tho with the ryng of hym; and sche sente to the grettere men in birthe, and to the beste men, that weren in the citee of hym, and dwelliden with Naboth.
9 Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
Sotheli this was the sentence of the lettre; Preche ye fastyng, and make ye Naboth to sitte among the firste men of the puple;
10 Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
and sende ye priueli twei men, the sones of Belial, ayens hym, and sey thei fals witnessyng, Naboth blesside God and the kyng; and lede ye out hym, and stoon ye him, and die he so.
11 Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
Therfor hise citeseyns, the grettere men in birthe, and the beste men that dwelliden with hym in the citee, diden as Jezabel hadde comaundid, and as it was writun in the lettris, whiche sche hadde sent to hem.
12 Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
Thei prechiden fastyng, and maden Naboth to sitte among the firste men of the puple;
13 Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
and whanne twey men, sones of the deuel, weren brouyt, thei maden hem to sitte ayens hym, and thei, that is, as men of the deuel, seiden witnessyng ayens him bifor al the multitude, Naboth blesside God and the kyng; for which thing thei ledden hym with out the citee, and killiden him with stoonys.
14 Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
And thei senten to Jezabel, and seiden, Naboth is stoonyd, and is deed.
15 Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
Forsothe it was doon, whanne Jezabel hadde herd Naboth stonyd and deed, sche spak to Achab, Rise thou, take thou in possessioun the vyner of Naboth of Jezrael, which nolde assente to thee, and yyue it for money takun; for Naboth lyueth not, but is deed.
16 Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
And whanne Achab hadde herd this, that is, Naboth deed, he roos, and yede doun in to the vyner of Naboth of Jezrael, to haue it in possessioun.
17 Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
Therfor the word of the Lord was maad to Elie of Thesbi,
18 “Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
and seide, Rise thou, go doun in to the comyng of Achab, kyng of Israel, which is in Samarie; lo! he goith doun to the vyner of Naboth, that he haue it in possessioun.
19 Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
And thou schalt speke to hym, and `thou schalt seie, The Lord God seith these thingis, Thou hast slayn, ferthermore and thou hast take in possessioun; and aftir these thingis thou schalt adde, In this place, wherynne doggis lickiden the blood of Naboth, thei schulen licke also thi blood.
20 Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
And Achab seyde to Elie, Whether thou hast founde me thin enemy? Which Elie seide, Y haue founde, for thou art seeld that thou schuldist do yuel in the siyt of the Lord.
21 Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
Therfor the Lord seith these thingis, Lo! Y schal brynge yn on thee yuel, and Y schal kitte awey thin hyndrere thingis, and Y schal sle of Achab a pissere to the wal, and prisoned, and the laste in Israel;
22 Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
and Y schal yyue thin hows as the hows of Jeroboam, sone of Naboth, and as the hows of Baasa, sone of Ahia; for thou didist to excite me to wrathfulnesse, and madist Israel to do synne.
23 “Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
But also the Lord spak of Jezabel, and seide, Doggis schulen ete Jezabel in the feeld of Jesrael;
24 “Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
if Achab schal die in the citee, doggis schulen ete hym; sotheli if he schal die in the feeld, briddis of the eyr schulen ete hym.
25 (Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
Therfor noon other was sich as Achab, that was seeld to do yuel in the siyt of the Lord; for Jezabel his wijf excitide hym;
26 Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
and he was maad abhomynable, in so myche that he suede the ydols that Ammorreis maden, which Ammorreis the Lord wastide fro the face of the sones of Israel.
27 Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
Therfor whanne Achab hadde herd these wordis, he to-rente his cloth, and hilide his fleisch with an hayre, and he fastide, and slepte in a sak, and yede with the heed cast doun.
28 Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
The word of the Lord was maad to Elie of Thesbi, and seide,
29 “Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”
Whethir thou hast not seyn Achab maad low bifor me? Therfor for he is maad low for the cause of me, Y schal not brynge yn yuel in hise daies, but in the daies of his sone Y schal bryng yn yuel to his hows.

< 1 Mafumu 21 >