< 1 Mafumu 11 >

1 Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti.
Forsothe kyng Salomon louyde brennyngli many alien wymmen, and the douytir of Pharao, and wymmen of Moab, and Amonytis, and Ydumeis, and Sydoneis, and Etheis;
2 Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa.
of the folkis of whiche the Lord seide to the sones of Israel, Ye schulen not entre to tho folkis, nether ony of hem schulen entre to you; for most certeynli thei schulen turne awei youre hertis, that ye sue the goddis of hem. Therfor kyng Salomon was couplid to these wymmen, bi moost brennyng loue.
3 Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa.
And wyues as queenys weren seuene hundrid to hym, and thre hundrid secundarie wyues; and the wymmen turneden awey his herte.
4 Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake.
And whanne he was thanne eld, his herte was bischrewid bi wymmen, that he suede alien goddis; and his herte was not perfit with his Lord God, as the herte of Dauid, his fadir, `was perfit.
5 Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni.
But Salomon worschipide Astartes, the goddesse of Sidoneis, and Chamos, the god of Moabitis, and Moloch, the idol of Amonytis;
6 Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.
and Salomon dide that, that pleside not bifor the Lord, and he fillide not that he suede the Lord, as Dauid, his fadir, dide.
7 Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni.
Thanne Salomon bildide a temple to Chamos, the idol of Moab, in the hil which is ayens Jerusalem, and to Moloch, the idol of the sones of Amon.
8 Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.
And bi this maner he dide to alle hise alien wyues, that brenten encencis, and offriden to her goddis.
9 Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse.
Therfor the Lord was wrooth to Salomon, for his soule was turned awei fro the Lord God of Israel; that apperide to Salomon the secounde tyme,
10 Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova.
and comaundide of this word, that he schulde not sue alien goddis; and he kepte not tho thingis, whiche the Lord comaundide to hym.
11 Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako.
Therfor the Lord seide to Salomon, For thou haddist this thing anentis thee, and keptist not my couenaunt, and myn heestis, whiche Y comaundide to thee, Y schal breke, and Y schal departe thi rewme, and Y schal yyue it to thi seruaunt.
12 Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako.
Netheles Y schal not do in thi daies, for Dauid, thi fadir; Y schal kitte it fro the hond of thi sone;
13 Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”
nether Y schal do a wey al the rewme, but Y schal yyue o lynage to thi sone, for Dauid, my seruaunt, and for Jerusalem, which Y chess.
14 Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu.
Forsothe the Lord reiside to Solomon an aduersarie, Adad Ydumey, of the kyngis seed, that was in Edom.
15 Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu.
For whanne Dauid was in Ydumee, and Joab, the prince of chyualrie, hadde stied to birie hem that weren slayn, and he hadde slayn ech male kynde in Ydumee;
16 Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu.
for Joab, and al Israel dwelliden there bi sixe monethis, til thei killiden ech male kynde in Ydumee; Adad hym silf fledde,
17 Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake.
and men of Ydumee, of `the seruauntis of his fadir, with hym, that he schulde entre in to Egipt; sotheli Adad was a litil child.
18 Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.
And whanne thei hadden rise fro Madian, thei camen in to Faran; and thei token with hem men of Faran, and entriden in to Egipt, to Pharao, kyng of Egipt; which Farao yaf an hows to hym, and ordeynede metis, and assignede lond.
19 Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi.
And Adad foond grace bifor Farao greetli, in so myche that Farao yaf to hym a wijf, the sister of his wijf, sister of the queen, of Taphnes.
20 Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.
And the sistir of Taphnes gendrid to hym a sone, Genebath; and Taphnes nurschide hym in the hows of Farao; and Genebath dwellide bifor Farao, with hise sones.
21 Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”
And whanne Adad hadde herd in Egipt, that Dauid slepte with hise fadris, and that Joab, the prince of chyualrie, was deed, he seide to Farao, Suffre thou me, that Y go in to my lond.
22 Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?” Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”
And Farao seide to hym, For of what thing hast thou nede at me, that thou sekist to go to thi lond? And he answeride, Of no thing; but Y biseche thee, that thou `delyuere me.
23 Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
Also God reiside an aduersarie to Salomon, Rason, sone of Eliadam, that fledde Adadezer, kyng of Soba, his lord;
24 Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira.
and gaderide men ayens hym, and was maad the prince of theuys, whanne Dauid killide hem; and thei yeden to Damask, and dwelliden there; and thei maden hym kyng in Damask.
25 Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.
And he was aduersarie of Israel in alle the daies of Salomon; and this is the yuel of Adad, and the hatrede ayens Israel; and he regnede in Sirie.
26 Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
Also Jeroboam, sone of Nabath, of Effraym of Saredera, the seruaunt of Salomon, of which Jeroboam, a womman widewe, Serua bi name, was modir, reisyde hond ayens the kyng.
27 Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake.
And this was cause of rebelte ayens the kyng; for Salomon bildide Mello, and made euene the swolowe of the citee of Dauid, his fadir.
28 Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.
Forsothe Jeroboam was a miyti man and strong; and Salomon siy the yong wexynge man of good kynrede, and witti in thingis to be doon, and Salomon made hym `prefect, ether souereyn, on the tributis of al the hows of Joseph.
29 Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko,
Therfor it was doon in that tyme, that Jeroboam yede out of Jerusalem; and Ahias of Sylo, a profete, hilid with a newe mentil, foond hym in the weie; sotheli thei tweyne weren oneli in the feeld.
30 ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12.
And Ahias took his newe mentil, with which he was hilid, and kittide in to twelue partis;
31 Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
and seide to Jeroboam, Take to thee ten kyttyngis; for the Lord God of Israel seith these thingis, Lo! Y schal kytte the rewme fro the hond of Salomon, and Y schal yyue to thee ten lynagis;
32 Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha.
forsothe o lynage schal dwelle to hym, for Dauid, my seruaunt, and for Jerusalem, the citee which Y chees of alle the lynagis of Israel;
33 Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.
this kittyng schal be; for Salomon forsook me, and worschipide Astartes, goddesse of Sidoneis, and Chamos, the god of Moab, and Moloch, the god of the sones of Amon; and yede not in my weies, that he dide riytwisnesse bifor me, and myn heestis, and my domes, as Dauid, his fadir, dide.
34 “‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga.
And Y schal not take awey al the rewme fro `his hond, but Y schal putte hym duyk in alle the daies of his lijf, for Dauid, my seruaunt, whom Y chees, which Dauid kepte myn heestis, and my comaundementis.
35 Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
Sotheli Y schal take awey the rewme fro the hond of `his sone, and Y schal yyue ten lynagis to thee;
36 Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa.
forsothe Y schal yyue o lynage to `his sone, that a lanterne dwelle to Dauid, my seruaunt, in alle daies bifor me in Jerusalem, the citee which Y chees, that my name schulde be there.
37 Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli.
Forsothe Y schal take thee, and thou schalt regne on alle thingis whiche thi soule desirith, and thou schalt be kyng on Israel.
38 Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli.
Therfor if thou schalt here alle thingis whiche Y schal comaunde to thee, and if thou schalt go in my weies, and if thou schalt do that, that is riytful bifore me, and if thou schalt kepe my comaundementis, and myn heestis, as Dauid, my seruaunt, dide, Y schal be with thee, and Y schal bilde a feithful hows to thee, as Y bildide an hows to Dauid, and Y schal yyue Israel to thee;
39 Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’”
and Y schal turmente the seed of Dauid on this thing, netheles not in alle daies.
40 Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.
Therfor Salomon wolde sle Jeroboam, which roos, and fledde in to Egipt, to Susach, kyng of Egipt; and he was in Egipt `til to the deeth of Salomon.
41 Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni?
Forsothe the residue of the wordis of Salomon, and alle thingis whiche he dide, and his wisdom, lo! alle thingis ben writun in the book of wordis of daies of Salomon.
42 Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi.
Sotheli the daies bi whiche Salomon regnede in Jerusalem on al Israel, ben fourti yeer.
43 Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.
And Salomon slepte with hise fadris, and was biriede in the citee of Dauid, his fadir; and Roboam, his sone, regnede for hym.

< 1 Mafumu 11 >