< 1 Mbiri 24 >

1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Forsothe to the sones of Aaron these porciouns schulen be; the sones of Aaron weren Nadab, and Abyud, Eleazar, and Ythamar;
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
but Nadab and Abyud weren deed with out fre children bifor her fadir, and Eleazar and Ythamar weren set in presthod.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
And Dauith departide hem, that is, Sadoch, of the sones of Eleazar, and Achymelech, of the sones of Ithamar, by her whiles and seruyce;
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
and the sones of Eleazar weren founden many mo in the men princes, than the sones of Ythamar. Forsothe he departide to hem, that is, to the sones of Eleazar, sixtene prynces bi meynees; and to the sones of Ythamar eiyte prynces bi her meynees and howsis.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
Sotheli he departide euer eithir meynees among hem silf bi lottis; for there weren princes of the seyntuarye, and princes of the hows of God, as wel of the sones of Eleazar as of the sones of Ithamar.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
And Semeye, the sone of Nathanael, a scribe of the lynage of Leuy, discriuede hem bifore the king and pryncis, and bifor Sadoch, the preest, and Achymelech, the sone of Abiathar, and to the prynces of meynees of the preestis and of the dekenes; he discriuyde oon hows of Eleazar, that was souereyn to othere, and `the tother hows of Ithamar, that hadde othere vndir hym.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
Forsothe the firste lot yede out to Joiarib, the secounde to Jedeie,
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
the thridde to Aharym, the fourthe to Seorym,
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
the fyuethe to Melchie,
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
the sixte to Maynan, the seuenthe to Accos,
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
the eiythe to Abia, the nynthe to Hieusu, the tenthe to Sechema, the elleuenthe to Eliasib,
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
the tweluethe to Jacyn,
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
the thrittenthe to Opha, the fourtenthe to Isbaal,
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
the fiftenthe to Abelga, the sixtenthe to Emmer,
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
the seuententhe to Ezir, the eiytenthe to Ahapses, the nyntenthe to Pheseye,
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
the twentithe to Jezechel,
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
the oon and twentithe to Jachym, the two and twentithe to Gamul, the thre and twentithe to Dalayam,
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
the foure and twentithe to Mazzian.
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
These weren the whilis of hem bi her mynysteries, that thei entre in to the hows of God, and bi her custom vndur the hond of Aaron, her fadir, as the Lord God of Israel comaundide.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
Forsothe Sebahel was prince of the sones of Leuy that weren resydue, of the sones of Amram; and the sone of Sebahel was Jedeie;
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
also Jesie was prince of the sones of Roobie.
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
Sotheli Salomoth was prince of Isaaris; and the sone of Salamoth was Janadiath;
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
and his firste sone was Jeriuans, `Amarie the secounde, Azihel the thridde, `Jethmoan the fourthe.
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
The sone of Ozihel was Mycha; the sone of Mycha was Samyr;
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
the brother of Mycha was Jesia; and the sone of Jesia was Zacharie.
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
The sones of Merary weren Mooli and Musi; the sone of Josyan was Bennon;
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
and the sone of Merarie was Ozian, and Soen, and Zaccur, and Hebri.
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
Sotheli the sone of Mooli was Eleazar, that hadde not fre sones; forsothe the sone of Cys was Jeremyhel;
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
the sones of Musy weren Mooli,
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
Eder, Jerymuth. These weren the sones of Leuy, bi the housis of her meynees.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
Also and thei senten lottis ayens her britheren, the sones of Aaron, bifor Dauid the kyng, and bifor Sadoch, and Achymelech, and the princes of meynees of preestis and of dekenes; lot departide euenli alle, bothe the gretter and the lesse.

< 1 Mbiri 24 >