< 1 Mbiri 23 >

1 Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.
Alltså gjorde David Salomo, sin son, till Konung öfver Israel, då han gammal, och af lefvande mätt var.
2 Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi.
Och David församlade alla öfverstar i Israel, och Presterna och Leviterna,
3 Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000.
Att man skulle räkna Leviterna, ifrå tretio år och derutöfver; och deras tal var, ifrå hufvud till hufvud, det starke män voro, åtta och tretio tusend;
4 Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza.
Af hvilkom voro fyra och tjugu tusend, som drefvo arbetet på Herrans hus; och sextusend ämbetsmän och domare;
5 Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”
Och fyratusend dörravaktare; och fyratusend lofsångare Herranom med strängaspel, som jag till lofsång gjort hade.
6 Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
Och David gjorde en ordning ibland Levi barn, nämliga ibland Gerson, Kehath och Merari.
7 Ana a Geresoni: Ladani ndi Simei.
Då Gersoniter voro: Laedan och Simei.
8 Ana a Ladani: Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.
Laedans barn: Den förste Jehiel, Setam och Joel, de tre.
9 Ana a Simei: Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu. Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.
Men Simei barn voro: Selomith, Hasiel och Haran, de tre. Desse voro de ypperste ibland fäderna af Laedan.
10 Ndipo ana a Simei anali: Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya. Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.
Voro också desse Simei barn: Jahath, Sina, Jeus och Beria. Desse fyra voro ock Simei barn.
11 Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.
Jahath var den förste, Sisa den andre. Men Jeus och Beria hade icke mång barn; derföre vordo de räknade för ens faders hus.
12 Ana a Kohati: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.
Kehaths barn voro: Amram, Jizear, Hebron och Ussiel, de fyra.
13 Ana a Amramu: Aaroni ndi Mose. Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya.
Amrams barn voro: Aaron och Mose. Men Aaron vardt afskild, så att han vardt helgad till det aldrahelgasta, han och hans söner, till evig tid, till att röka för Herranom, och till att tjena och välsigna i Herrans Namn i evig tid;
14 Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.
Och Mose, den Guds mansens, barn vordo nämnde ibland de Leviters slägte.
15 Ana a Mose: Geresomu ndi Eliezara.
Mose barn voro: Gersom och Elieser.
16 Zidzukulu za Geresomu: Mtsogoleri anali Subaeli.
Gersoms barn: Den förste var Sebuel.
17 Zidzukulu za Eliezara: Mtsogoleri anali Rehabiya. Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.
Eliesers barn: Den förste var Rehabia. Och Elieser hade inga annor barn; men Rehabia barn voro mycket flere.
18 Ana a Izihari: Mtsogoleri anali Selomiti.
Jizears barn voro: Selomith den förste.
19 Ana a Hebroni: Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.
Hebrons barn voro: Jeria den förste, Amaria den andre, Jahasiel den tredje, och Jekameam den fjerde.
20 Ana a Uzieli: Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.
Ussiels barn voro: Micha den förste, och Jissija den andre.
21 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Ana a Mahili: Eliezara ndi Kisi.
Merari barn voro: Maheli och Musi. Maheli barn voro: Eleazar och Kis.
22 Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.
Men Eleazar blef död, och hade inga söner, utan döttrar; och Kis barn, deras bröder, togo dem.
23 Ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.
Musi barn voro: Maheli, Eder och Jeremoth, de tre.
24 Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova.
Detta äro Levi barn i deras faders hus, och de ypperste af fäderna, som räknade vordo, efter namnens tal efter hufvuden, hvilke gjorde de sysslor i ämbeten i Herrans hus, ifrå tjugu år, och derutöfver.
25 Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya,
Ty David sade: Herren Israels Gud hafver gifvit sino folke ro, och skall bo i Jerusalem till evig tid.
26 sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.”
Leviterna behöfde ock icke bära tabernaklet, med all dess redskap, efter deras ämbete;
27 Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.
Utan, efter Davids yttersta ord, vordo Levi barn räknade ifrå tjugu år, och derutöfver;
28 Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu.
Att de skulle stå under Aarons barnas händer, till att tjena i Herrans hus, i gårdenom, och till kistorna, och till reningen, och till allahanda helgedom, och till alla ämbetens sysslor i Guds hus;
29 Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake.
Och till skådobröd, till semlomjöl, till spisoffer, till osyrade kakor, till pannor, till halster, och till all vigt och mått;
30 Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo,
Och till att stå om morgonen, och tacka och lofva Herran; om aftonen desslikes;
31 ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.
Och till att offra Herranom all bränneoffer på Sabbatherna, nymånadom och högtidom, efter talet och sättet, alltid för Herranom;
32 Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.
Att de skulle taga vara på vaktena vid vittnesbördsens tabernakel, och helgedomens; och Aarons barnas, deras bröders, till att tjena i Herrans hus.

< 1 Mbiri 23 >