< 2 Mafumu 1 >

1 Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
Och de Moabiter föllo af ifrån Israel, då Achab död var.
2 Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
Och Ahasia föll genom gallren i sinom sal i Samarien, och vardt krank; och sände ut bådskap, och sade till dem: Går bort, och fråger BaalSebub, den guden i Ekron, om jag skall vederfås af denna krankheten.
3 Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
Men Herrans Ängel sade till Elia den Thisbiten: Statt upp, och gack emot Konungens bådskap i Samarien, och säg till dem: Är nu ingen Gud i Israel, att I behöfven gå bort, och fråga BaalSebub, Ekrons gud?
4 Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
Derföre, så säger Herren: Du skall icke komma utaf sängene, der du dig på lagt hafver; utan skall döden dö. Och Elia gick sin väg.
5 Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
Och då båden igenkommo till honom, sade han till dem: Hvi kommen I igen?
6 Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
De sade till honom: En man kom upp emot oss, och sade till oss: Går tillbaka igen till Konungen, som eder utsändt hafver, och säger till honom: Detta säger Herren: Är nu ingen Gud i Israel, att du skall sända bort, och fråga BaalSebub, Ekrons gud? Derföre skall du icke komma af sängene, der du hafver lagt dig uppå; utan skall döden dö.
7 Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
Han sade till dem: Hurudana var den mannen, som eder mötte, och sade detta till eder?
8 Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
De sade till honom: Mannen var luden, och en lädergjord om hans länder. Han sade: Det är Elia den Thisbiten.
9 Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
Och han sände bort till honom en höfvitsman öfver femtio, med de samma femtio. Och då han kom upp till honom, si, då satt han uppe på bergena; och han sade till honom: Du Guds man, Konungen säger: Du skall komma ned:
10 Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
Elia svarade höfvitsmannen öfver femtio, och sade till honom: Är jag en Guds man, så falle eld af himmelen, och upptäre dig och dina femtio. Då föll eld af himmelen, och upptärde honom och hans femtio.
11 Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
Och han sände åter en: annan höfvitsman öfver femtio till honom, med hans femtio: Han sade till honom: Du Guds man, detta säger Konungen: Kom snarliga ned.
12 Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
Elia svarade, och sade: Är jag en Guds man, så falle eld af himmelen, och upptäre dig och dina femtio. Då föll Guds eld af himmelen, och upptärde honom och hans femtio.
13 Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
Då sände han ännu den tredje höfvitsmannen öfver femtio, med hans femtio. Då han kom upp till honom, böjde han sin knä för Elia, och bad honom, och sade till honom: Du Guds man, låt mina själ, och dina tjenares, dessa femtios själar, något aktade varda för dig.
14 Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
Si, elden är fallen af himmelen, och hafver upptärt de första två höfvitsmän öfver femtio, med deras femtio; men nu låt mina själ något aktad varda för dig.
15 Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
Då sade Herrans Ängel till Elia: Gack ned med honom, och frukta dig intet för honom. Han stod upp, och gick ned med honom till Konungen.
16 Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
Och han sade till honom: Så säger Herren: Derföre, att du sände bådskap bort, och lät fråga BaalSebub, Ekrons gud, likasom ingen Gud vore i Israel, hvilkens ord man fråga kunde, så skall du icke komma af sängene, der du hafver lagt dig uppå; utan skall döden dö.
17 Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
Alltså blef han död, efter Herrans ord, det Elia talat hade. Och Joram vardt Konung i hans stad, i andra årena Jorams, Josaphats sons, Juda Konungs; ty han hade ingen son.
18 Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Hvad nu mer af Ahasia sägandes är, hvad han gjort hafver, si, det är skrifvet i Israels Konungars Chrönico.

< 2 Mafumu 1 >