< 1 Mbiri 19 >

1 Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
A poslije toga umrije Nas car sinova Amonovijeh, i zacari se sin njegov na njegovo mjesto.
2 Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
I reèe David: da uèinim milost Anunu sinu Nasovu, jer je otac njegov uèinio meni milost. I posla David poslanike da ga potješe za ocem. I doðoše sluge Davidove u zemlju sinova Amonovijeh k Anunu da ga potješe.
3 atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
A knezovi sinova Amonovijeh rekoše Anunu gospodaru svojemu: misliš da je David zato poslao ljude da te potješe što je rad uèiniti èast ocu tvojemu? a nijesu zato došle sluge njegove k tebi da promotre i uhode i obore zemlju?
4 Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
Tada Anun uhvati sluge Davidove, i obrija ih i otsijeèe im haljine po pole do zadnjice, i opravi ih natrag.
5 Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
A kad neki otidoše, te javiše Davidu za te ljude, on posla pred njih, jer ljudi bijahu grdno osramoæeni, i poruèi im car: sjedite u Jerihonu dok vam naraste brada, pa onda doðite natrag.
6 Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
A kad vidješe sinovi Amonovi gdje se omraziše s Davidom, onda Anun i sinovi Amonovi poslaše tisuæu talanata srebra da najme kola i konjika iz Mesopotamije i iz Sirije Mahe i iz Sove.
7 Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
I najmiše trideset i dvije tisuæe kola i cara od Mahe s narodom njegovijem, koji doðoše i stadoše u oko prema Medevi. A i sinovi Amonovi skupiše se iz gradova svojih i doðoše na boj.
8 Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
A David kad to èu, posla Joava sa svom hrabrom vojskom.
9 Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
I izidoše sinovi Amonovi i uvrstaše se pred vratima gradskim; a carevi koji doðoše bijahu za se u polju.
10 Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
I Joav vidjeæi namještenu vojsku prema sebi sprijed i sastrag, uze odabrane iz sve vojske Izrailjske, i namjesti ih prema Sircima.
11 Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
A ostali narod predade Avisaju bratu svojemu; i namjestiše ih prema sinovima Amonovijem.
12 Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
I reèe: ako Sirci budu jaèi od mene, doði mi u pomoæ; ako li sinovi Amonovi budu jaèi od tebe, ja æu tebi doæi u pomoæ.
13 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
Budi junak i držimo se junaèki za svoj narod i za gradove Boga svojega; a Gospod neka uèini što mu je drago.
14 Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
Tada Joav i narod koji bijaše s njim primakoše se da udare na Sirce; ali oni pobjegoše ispred njih.
15 Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
A sinovi Amonovi kad vidješe gdje pobjegoše Sirci, pobjegoše i oni ispred Avisaja brata njegova i uðoše u svoj grad. Potom se Joav vrati u Jerusalim.
16 Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
Ali Sirci kad vidješe gdje ih nadbiše Izrailjci, poslaše poslanike te dovedoše Sirce ispreko rijeke; a Sofak vojvoda Adar-Ezerov iðaše pred njima.
17 Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
Kad to javiše Davidu, on skupi sve Izrailjce, i prijeðe preko Jordana, i doðe k njima, i namjesti vojsku prema njima; a kad namjesti David vojsku prema njima, pobiše se s njim.
18 Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
Ali pobjegoše Sirci ispred Izrailja, i pobi David Siraca sedam tisuæa kola i èetrdeset tisuæa pješaka, i Sofaka vojvodu pogubi.
19 Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.
I kad vidješe sluge Adar-Ezerove da ih razbi Izrailj, uèiniše mir s Davidom i služahu mu; i ne htješe više Sirci pomagati sinovima Amonovijem.

< 1 Mbiri 19 >