< Lucas 19 >

1 Y Jesus terelando chalado andré, nacaba por Jericho.
Yesu analowa mu Yeriko napitirira.
2 Y he acoi manu araquerado Zachéo: y ocona sinaba yeque es mas bares enré os Publícanes, y balbalo:
Kunali munthu kumeneko dzina lake Zakeyu; iye anali mkulu wa wolandira msonkho ndipo anali wolemera.
3 Y orotaba dicar á Jesus, coin sinase: y na le astis pre la baribu sueti, presas sinaba chinoro de trupo.
Iye ankafuna kuona Yesu kuti ndani, koma pokhala wamfupi sanathe chifukwa cha gulu la anthu.
4 Y chalando anglal, se costunó andré carschta bruñi heila somia dicarle, presas por oté terelaba de nacar.
Choncho iye anathamangira patsogolo ndipo anakwera mu mtengo wamkuyu kuti amuone Iye, pakuti Yesu ankadutsa njira imeneyo.
5 Y pur bigoreó Jesus á ocona stano, ardiñelando as aquias, le dicó, y le penó: abillel ostely yescotria, presas jomte ustilarme achibes andré tun quer.
Yesu atafika pa malopo, anayangʼana mmwamba ndipo anati kwa iye, “Zakeyu, tsika msangamsanga. Ine ndiyenera kukhala mʼnyumba mwako lero.”
6 Y ó chaló ostely yescotría, y le ustiló asaselándose.
Ndipo nthawi yomweyo anatsika ndipo anamulandira mosangalala.
7 Y dicando ocono sares, chumasquereláron, penando, que terelaba chalado á sinar andré quer de yeque choro.
Anthu onse ataona zimenezi anayamba kungʼungʼudza, nati, “Iye akupita kuti akakhale mlendo wa wochimwa.”
8 Tami Zachéo, chibandose anglal e Erañoró, le penó: Eraño, a paque de ma terelo diñelo á os chorores: y si andré buchi terelo jonganado á manu, le voltisarelo star tanto butér.
Koma Zakeyu anayimirira ndipo anati kwa Ambuye, “Taonani Ambuye! Theka la chuma changa ndipereka kwa osauka ndipo ngati ndinamubera wina aliyense pa chilichonse, ndidzamubwezera mochulukitsa kanayi.”
9 Y Jesus le penó: Achibes ha abillado golipen á ocona quer: presas ó tambien sinela chaboro de Abraham.
Yesu anati kwa iye, “Lero chipulumutso chafika mʼnyumba ino, chifukwa munthu uyu nayenso ndi mwana wa Abrahamu.
10 Presas o Chaboro e manu abilló á orotar, y á salvar ma sinaba chibado á najabar.
Pajatu Mwana wa Munthu anabwera kudzafunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.”
11 Junelando junos ocono, plastañó penandoles yeque parabola, sat ocasion de sinar sunparal de Jerusalem: y presas penchababan que yescotria se mequelaria dicar o chim de Debél:
Pamene iwo ankamvera izi, Iye anapitiriza kuwawuza fanizo, chifukwa Iye anali kufupi ndi Yerusalemu ndipo anthu ankaganiza kuti ufumu wa Mulungu ukanaoneka nthawi yomweyo.
12 Penó pues: Manu tintin chaló a chim dur, somia ustilar yeque lume oté, y despues limbidiarse.
Iye anati, “Munthu wa banja laufumu anapita ku dziko lakutali kukadzozedwa ufumu ndipo kenaka abwerenso kwawo.
13 Y araquerando á deque de desqueres lacrés, les diñó deque estongrias, y les penó: paruguelad entretanto que abillelo.
Tsono iye anayitana antchito ake khumi ndi kuwapatsa ndalama khumi. Iye anati, ‘Gwiritsani ntchito ndalama izi mpaka nditabwerera.’
14 Tami os de desquero foros na le camelaban, y bichobando palal de ó yeque plastañí, le penáron: Na camelamos que reyne ocona opré de amangue.
“Koma anthu ake anamuda ndipo anatuma nthumwi pambuyo pake kukanena kuti, ‘Sitikufuna munthuyu kuti akhale mfumu yathu.’
15 Y pur limbidió, despues de ustilar o lume, penó araquerar á ocolas lacrés, á coines terelaba diñado o jayere, somia chanelar ma cata yeque terelaba paruguelado.
“Iye analandira ufumuwo ngakhale zinali zotero, ndipo anabwerera kwawo. Kenaka iye anatumiza uthenga kwa antchito ake amene anawapatsa ndalama aja, ndi cholinga chakuti adziwe chimene anapindula nazo.
16 Bigoreó pues o brotobo y penó: Erañó; tiri estongri ha ganisarado deque estongrias.
“Woyamba anabwera ndipo anati, ‘Bwana ndalama zanu zapindula khumi zina.’
17 Y le penó: Sinela mistos, lacho lacró. Presas andré a fremita has sinado cabalico, terelarás ezor opré deque fores.
“Bwana wakeyo anayankha kuti, Wachita bwino wantchito wabwino. ‘Chifukwa wakhulupirika pa zinthu zazingʼono, lamulira mizinda khumi.’
18 Y abilló aver, y penó: Erañó: Tiri estongri ha ganisarado pansch estongrias.
“Wachiwiri anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama zanu zapindula zisanu zina.’
19 Y penó á ocona: Tucue terelalo opré pansch fores.
“Bwana anayankha kuti, ‘Iwe lamulira mizinda isanu.’
20 Y abilló o trincho, y penó: Erañó, acoi terelas tiri estongri, sos he terelado ujarada andré yeque diclo.
“Kenaka wantchito wina anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama yanu nayi; ine ndinayibisa ndi kuyisunga mʼkansalu.
21 Presas terelaba dal de tucue, sos sinelas manu recio de suncai; Ustilelas ma na chitaste, y chinelas ma na chibelaste.
Ine ndimakuopani, chifukwa ndinu munthu wowuma mtima. Inu mumatenga chimene simunachiyike ndi kukolola chimene simunadzale.’
22 Entonces ó le penó: Choro lacró, abrí tiro mui condenelo tucue: Chanelabas que menda sinaba manu recio de suncai, que ustilelo ma na chité, y chinelo ma na chibele.
“Bwana wake anayankha kuti, ‘Ine ndikukuweruza iwe ndi mawu ako omwewo. Ndiwe wantchito woyipa. Kani umadziwa kuti ndine munthu wowuma mtima ndi wotenga chimene sindinasungitse, ndi kukolola chimene sindinadzale?
23 ¿Pues presas na diñaste minrio jayere al banco, somia que pur limbidiase lo ustilára sat ganancia?
Nanga nʼchifukwa chiyani sunasungitse ndalama yanga, kuti ine pobwera, ndidzayitenge ndi chiwongoladzanja?’
24 Y penó á junos sos sinaban oté: Nicabeladle a estongri, y diñadsela al lacró sos terela deque estongrias.
“Ndipo iye anawuza amene anayimirira pafupi kuti, ‘Tengani ndalama yake ndi kumupatsa amene ali ndi ndalama khumiyo!’”
25 Y junos le penáron: Eraño, que terela deque estongrias.
Iwo anati, “Bwana iyeyu ali nazo kale khumi!”
26 Pues menda sangue penelo, que á saro ocola sos terelará, se le diñará, y terelará butér: tami al sos na terela, se le nicobará aun ma terele.
Iye anayankha kuti, “Ndikukuwuzani kuti, aliyense amene ali nazo, adzapatsidwa zambiri, koma amene alibe, adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho.
27 Y en quanto á ocolas minres daschmanuces, sos na cameláron que menda reynase opré junos, laneladmelos acoi, y mareladlos anglal de mangue.
Tsono adani anga aja amene sankafuna kuti ndikhale mfumu yawo, abweretseni pano ndi kuwapha ine ndikuona.”
28 Y penado ocono guillaba anglal costunando á Jerusalém.
Yesu atatha kunena izi, anayendabe kupita ku Yerusalemu.
29 Y anacó, que pur bigoreó sunparal de Bethphage, y de Bethania, al bur, sos se araquerela e Urucal, bichabó dui es desqueres discipules,
Iye atayandikira ku Betifage ndi Betaniya pa phiri lotchedwa Olivi, Iye anatuma awiri a ophunzira nati kwa iwo,
30 Penando: Chalad á ocona gau, sos sinela de mamui: y yescotria que chalareis andré, alachareis ternoro de gel pandado, y opré coin nunca se besteló cayque: despandadlo, y laneladlo.
“Pitani mʼmudzi uli patsogolo panu, mukakalowa mʼmudzimo, mukapeza mwana wabulu womangiriridwa amene wina aliyense sanakwerepo. Mukamumasule ndi kubwera naye kuno.
31 Y si manu puchabelare sangue: ¿Por qué lo despandais? A ó rudelareis andiar: Porque o Erañó terela menester de ó.
Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mukumumasula mwana buluyo?’ Mukamuwuze kuti, ‘Ambuye akumufuna.’”
32 Chaláron pues junos sos habian sinado bichabados, y alacháron o ternoro, sos sinaba sasta les habia penado.
Otumidwawo anapita nakamupeza mwana wabulu monga momwe Yesu anawawuzira.
33 Y pur despandaban al ternoro, les penáron os julais: ¿Por qué despandais al ternoro?
Pamene ankamasula mwana wabuluyo, eni ake anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukumasula mwana wabuluyo?”
34 Y junos rudeláron: Porque o Erañó terela menester de ó.
Iwo anayankha kuti, “Ambuye akumufuna.”
35 Y lo laneláron á Jesus. Y chibando opré o ternoro desqueres talalores: chitáron á Jesus opré.
Iwo anabweretsa buluyo kwa Yesu, naponya zovala zawo pa bulupo ndi kumukwezapo Yesu.
36 Y chalando ó andiar, bucharáron desqueres coneles andré a feda.
Pamene ankapita, anthu anayala zovala zawo mu msewu.
37 Y pur bigoreó sunparal al luchipen e bur e Urucal, sares os discipules en plastañias, perelales de pesquital se chibáron á majarificar á Un-debél á goles bares pre sarias as buchias, sos habian dicado,
Iye atafika pafupi ndi pamene msewu umatsikira ku phiri la Olivi, gulu lonse la ophunzira linayamba kuyamika Mulungu mwachimwemwe ndi mawu ofuwula chifukwa cha zodabwitsa zonse anaziona.
38 Penando: Majarificado o Crallis, sos abillela andré o nao e Erañoró, paz andré o Charos, y chimusolano andré o Tarpe.
“Yodala mfumu imene ikubwera mʼdzina la Ambuye!” “Mtendere kumwamba ndi ulemerero mmwambamwamba!”
39 Y yeques es Phariseyes sos sinaban enré á sueti, le penáron: Duquendio, reprehende á tires discipules.
Ena mwa Afarisi mʼgulumo anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, adzudzuleni ophunzira anu!”
40 O les rudeló: Sangue penelo, que si oconas mequelaren, as baras diñarán goles.
Iye anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani kuti, ngati atakhala chete, miyala idzafuwula.”
41 Y pur bigoreó sunparal, al dicar o Foros, orobó opré ó, penando:
Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira
42 ¡Ysna! si pincharases buchi andré ocona tun chibes, ma astisarela lanelartucue a paz! Tami acana sinela ucharado de tirias aquias.
nati, “Iwe ukanadziwa lero lino zinthu zokubweretsera mtendere, koma tsopano zabisikira maso ako.
43 Presas abillarán chibeses contra tucue, pur tires daschmanuces te chibarán al crugos trincheras, y te chibarán cerco, y te pandarán pre sarias aricatas.
Pakuti masiku adzabwera pamene adani ako adzamanga mitumbira yankhondo nakuzungulira, nadzakutsekereza mbali zonse.
44 Y chibarán tucue ostely, y á tires chabores, sos sinelan andré tucue, y na mequelarán andré tucue bar opré bar; presas na pincharaste o chiros de tiri visitacion.
Iwo adzakugwetsera pansi, iwe, ana ako onse a mʼkati mwako. Iwo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa unzake, chifukwa sunazindikire nthawi ya kubwera kwa Mulungu.”
45 Y chalando andré a cangri se chitó á bucharar abrí á sares junos sos quinaban y binaban andré siró,
Kenaka Iye analowa mʼdera la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kutulutsa kunja amene amachita malonda.
46 Penandoles: Libanado sinela: Minrio quer, quer de beda sinela. Tami sangue lo terelais querdi tunia de randes.
Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzakhala nyumba ya mapemphero, koma inu mwayisadutsa phanga la achifwamba.”
47 Y cata chibes bedaba andré a cangri. Tami os Manclayes es erajais, y os Libanes, y os tintines e sueti le camelaban marar.
Tsiku lililonse amaphunzitsa mʼNyumba ya Mulungu. Koma akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi atsogoleri pakati pa anthu amayesetsa kuti amuphe.
48 Y na chanelaban que querelarse sat ó. Presas sari a sueti sinaba moscabis pur le junelaba.
Komabe iwo sanathe kupeza njira ina iliyonse kuti achite izi, chifukwa anthu onse anakhulupirira mawu ake.

< Lucas 19 >