< 2 Ukorintiyawa 1 >

1 Bulus unan kadura Yesu Kristi nin su Kutelle, nin Timintawus gwana bit, udu kutii kulau korintiyawe, nin vat nanit alau nigbirin na ikilin acaiya.
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, pamodzi ndi mʼbale wathu Timoteyo, Kulembera mpingo wa Mulungu mu Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse mu Akaya monse.
2 Ubolu Kutelle na uda kiti mine kibinayi kisheu unuzu KutelleUcif bite nin Cikilari Yesu Kristi.
Mukhale ndi chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
3 Na mmari Kutelle nin Cif ncikilari Yesu Kristi soo, ule na amereUcif ukunekune nin Kutelle nonko nibinayi,
Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu wachitonthozo chonse.
4 Ulena adin nonkuzu nibinaiyi bite nanya piwu nibinaiyi bite arik nonko among ale na nibinaiyi mine piya nin nonku nibinai na Kutelle na ma nonku nari mun nibinaibit.
Iye amatitonthoza ife mʼmavuto athu onse, kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu.
5 Bara nafo uniyu Kristi karin bara arik nenere ununkuzu nibinayi bite karin nanya Kristi.
Pakuti monga momwe tili mʼmasautso pamodzi ndi Khristu, momwemonso Khristu amatitonthoza kwambiri.
6 Bara nanin tiwa se upiwu nibinaiyi usuu utucunin nin nonku nibinayi nenere. Sa i wa nonku nibinayi bite unfe unon ku nibinayari, ulena udi na uwa da lanza uniuwe nannarik.
Ngati ife tikusautsidwa, nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe ndi kupulumutsidwa. Ngati ife tikutonthozedwa nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe, ndi chitonthozo chimene chimabweretsa mwa inu kupirira kosawiringula pa zosautsa zomwe timasauka nazo ife.
7 Nin nayi akone bite kitife nyisina nin yiru nafo na una neu nan narik tutung nenere unonku nibinaye.
Ndipo chiyembekezo chathu pa inu nʼcholimba chifukwa tikudziwa kuti monga momwe mumamva zowawa pamodzi nafe, momwemonso mumatonthozedwa nafe pamodzi.
8 Bara na ti dinin su tiso sa uyiru ba linwana mbeleng na tiwase nanya Asiya; iwa naulin nari nafo na ti wasa ti tere nibinai ba kan har tiwa nutun nibinai sa tim ati ulai.
Abale, sitikufuna kuti mukhale osadziwa za masautso amene tinakumana nawo mʼchigawo cha Asiya. Tinapanikizidwa koopsa kuposa muyeso woti nʼkutha kupirira, mwakuti sitinkadziwa kuti nʼkukhalabe ndi moyo.
9 Nin nene iwa tinari tishot inkul nati bite bara nanin i wadin yenju nati mase likara kibinai nati bite ba inmaimako kiti Kutelle ulena ana fiya abi.
Zoonadi, tinamva mʼmitima mwathu chilango cha imfa. Koma izi zimachitika kuti tisangodzidalira mwa ife tokha koma Mulungu yemwe amaukitsa akufa.
10 Awa tucu nari nanyang kul nijas, ama kuru atucu nari tutun. Ti kotina ayibit kitene me tutung ama nutu nari
Mulungu watilanditsa ku zoopsa zotere za imfa, ndipo adzatilanditsanso. Ife tayika chiyembekezo chathu pa Iyeyo kuti adzapitiriza kutilanditsabe.
11 Ama su nari nani i wa bun nari nanya nlira anit gbardan ba daduru liburi liboo iyisunu bite bara ubolsu Kutelle na ana ninari nanya nlira na nit gbardan.
Mutithandize potipempherera. Pamenepo ambiri adzathokoza mʼmalo mwathu, chifukwa cha chisomo chake poyankha mapemphero a anthu ambiri.
12 Nene ilelere ti din fo figiri mung ushaida yiru bite ule na arik wa su nin nati bite nanya yi. Tiwa su nanin bara kata yinu nin lau nin kidegere na wa nuzu kiti Kutelle na nafo kujinjin yii ulele bara nanin inuzu ballu Kutelle.
Tsono chonyadira chathu nʼchakuti, chikumbumtima chathu chimatitsimikizira kuti timakhala bwino mʼdziko lapansi, makamaka pa ubale wathu ndi inu. Takhala moona mtima ndi oyera mtima. Sitinachite chomwechi mwa nzeru ya dziko lapansi koma monga mwa chisomo cha Mulungu.
13 Na tidin yarti minu imonile na iwa sa ibele sa uyinin ba indi nin likara kibinai tutung.
Pakuti sitikukulemberani zoti simungawerenge kapena kumvetsetsa.
14 Nafo na ina malin yinu nari likot, lirum au lirin Cilkilari bite Yesu tina yite udalilin fizu nabanda mine nafo na anung ba yitu unbit.
Monga mwamva pangʼono chabe, ndikuyembekeza kuti mudzamvetsa kwenikweni, kuti mutha kutinyadira monga ife tidzakunyadirani, pa tsiku la Ambuye Yesu.
15 Bara nan wadi nin likara kibinai nilele iwa din nin su indak kitefe nin burnu, au unan sere mbang inse na mara aba.
Popeza ndinatsimikiza mtima za ichi, nʼchifukwa chake ndinafuna kuti poyamba, ndidzakuchezereni kuti mupindule pawiri.
16 Iwa di woru inlasin kit fe cindu Umakidaniya inkueu mda yene fi cin sa Unuzu Makidoniya nani fe nin tiyi ndina udu Ujudia.
Ndinafuna kuti ndidzakuchezereni pa ulendo wanga wopita ku Makedoniya ndi kudzakuonaninso pochokera ku Makedoniyako kuti inu mudzandithandize pa ulendo wanga wopita ku Yudeya.
17 Kubi kona iwa din kpilzu nan, iwa belin kibinai fe? sa uwa yinan miu nin kibinai unitan, bara in woro fi ''ee ee” nin “babu babu”kube kurume?
Kodi pamene ndinkakonzekera zimenezi, mukuganiza kuti ndinkachita mwachibwana? Kapena kuti ndinkaganiza ngati mwa dziko lapansi; kuti ndikhoza kumanena kuti, “Inde, Inde,” nthawi yomweyo nʼkumatinso “Ayi, Ayi?”
18 Bara nanin nafo na Kutelle unan yinnu sa uyenu nati wasa ti woro “ee” nin “babu” ba.
Koma zoona monga Mulungu ali wokhulupirika, uthenga wathu kwa inu siwakuti, “Inde” nʼkutinso “Ayi.”
19 Bara gono Kutelle Yesu Kirst, ule na Silvanus Timitawus nin mi na beling naya min, na ame “ee “nin ''babu” ba bara nani ame ee wari vat kubi.
Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.”
20 Bara vat nalikawali Kutelle ''ee' wari nanya me baranani nanya me asa ti wuru uso nani udu uzazu Kutelle.
Pakuti ngakhale malonjezo a Mulungu atachuluka chotani, onsewo ndi “Inde” mwa Khristu. Kotero kuti mwa Iye, ife timati “Ameni” kuchitira Mulungu ulemu.
21 Nene Kutelleri munu nari nanya Kristi nin narik.
Tsono ndi Mulungu amene anachititsa kuti inu ndi ife tiyime molimba mwa Khristu. Anatidzoza ife,
22 Ana tursu nari nin na gilet me na ni nari Ifip nanya nibinai bite minin so kulap ni mele na ama da ninari nin dandaunu.
nayikanso Mzimu wake mʼmitima mwathu kutitsimikizira za mʼtsogolo.
23 Nin nanin ina yicila Kutelle aso unan nizi iba ning bara imele na inati nan daa u Kurintiya ba bara inan unan tucu fiari.
Mulungu ndi mboni yanga kuti sindinabwererenso ku Korinto kuno kuti ndisakumvetseni chisoni.
24 Na bara ti di nin su wuru timiin uyenu sa uyenu b, bara na tidi katwa nin yenu sa uyenu miner, bara mmag min, nayinsin nanya yinnu sa uyenu
Sikuti ife tikufuna kukhala olamulira chikhulupiriro chanu, koma timagwira nanu ntchito pamodzi kuti mukhale achimwemwe, chifukwa ndinu okhazikika kwambiri mʼchikhulupiriro.

< 2 Ukorintiyawa 1 >