< 1 Ukorintiyawa 1 >

1 Meng Bulus, uyiculun Kristi Yisa nso unan kadura bara uyinnu Kutellẹ, a Sostanisu gwana bit,
Paulo, woyitanidwa mwachifuniro cha Mulungu kuti akhale mtumwi wa Khristu Yesu ndi mʼbale wathu Sositene.
2 udu kiti na nan tortu Kutellẹ na idi in Korintus, alenge na Kristi Yisa nati nani iso lan, iwa yiwa nani iso anit alau, vat nan na lenge na idin yicu lissan Cikilari bite Yisa Kristi in ko kame kiti, Cikilari mine nini unbit.
Kupita ku mpingo wa Mulungu ku Korinto, kwa oyeretsedwa mwa Khristu Yesu ndi oyitanidwa kukhala opatulika ndiponso kwa onse amene amapemphera mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu mʼdziko lonse lapansi, amene ndi Ambuye wawo ndi wathunso.
3 Na ubolu me nin lissosin lisheu unuzu kitiin Kutellẹ ucif bit a Cikilari Yisa Kristi.
Landirani chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
4 Ndin godu Kutelle ning ko kome kubi bara anughe, nan nyan bolu Kutellẹ na Kristi Yisa nani minu.
Nthawi zonse ndimayamika Mulungu chifukwa cha inu chifukwa cha chisomo chake chopatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu.
5 Ana tti minu anan se nan nya ko lome libau, nan nya nliru nin yiru vat.
Pakuti mwa Iye mwalemekezedwa mʼnjira iliyonse, mʼkuyankhula kwanu konse ndi mʼkudziwa kwanu konse,
6 Ana ti minu ita imon nacara, nafo na ubellee nimon liburu libo litin Kristi, na nuzu kanang nan nya mine.
chifukwa umboni wathu pa za Khristu unatsimikizidwa mwa inu.
7 Bara nani na idiira ufilllu nruhuba, naffo na ina yita nin tok ncaa nnuzu kanang in Cikilari bite Yisa Kristi.
Choncho inu simusowa mphatso yauzimu iliyonse pamene mukudikira mofunitsitsa kuti Ambuye athu Yesu Khristu avumbulutsidwe.
8 Ame ni minu akara tutung udi duri imaline, bara inan so sa alapi lirin Cikilari bite Yisa Kristi.
Adzakulimbikitsani mpaka kumapeto kuti mudzakhale wopanda mlandu pa tsiku lobwera Ambuye athu Yesu Khristu.
9 Kutellẹ di nin yinnu, ame ulenge na ana yicila minu nan nya lissosin ligo nin saunne, Yisa Kristi Cikilari bite.
Mulungu amene wakuyitanani inu mu chiyanjano ndi Mwana wake Yesu Khristu Ambuye athu ngokhulupirika.
10 Nene ndi munu kucukusu, nuana nilime nan nishono, nan nya lissan Cikilari bite Yisa Kristi, na vat mine na yinin, na i wa se uwucu nati nati nan nya mine ba. Ndi kucukusu imunu ati umalizinu kugir kun lo ligowe nin kibinai kirum a udalili urim.
Ndidandaulira inu, abale, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu kuti nonsenu muvomerezane wina ndi mnzake kuti pasakhale kugawikana pakati panu ndi kuti mukhale amodzi kwenikweni mu nzeru ndi mʼmaganizo.
11 Nani anan gan kuluwi na da tyi vet natuf nbeleng nworu uwutuzunu din piun nan nya mine.
Abale anga, ena a ku nyumba ya Kloe andidziwitsa kuti pali mkangano pakati panu.
12 Nene uliru niighe ule: Ko gha mine din su, “Mengg un Bulus ari,” “Meng un Apolos” “Meng un Kefas,” sa, “Mengg un Kristi.”
Chimene ndikutanthauza ndi ichi: wina amati, “Ndimatsatira Paulo,” wina, “Ndimatsatira Apolo,” wina, “Ndimatsatira Kefa,” winanso, “Ndimatsatira Khristu.”
13 Kristẹ nkoso kidowa? iwa kotun Bulus ku kuca bara anughe? Iwa shintin munu nmyen nan nya lissan Bulussa?
Kodi Khristu wagawikana? Kodi Paulo anapachikidwa pa mtanda chifukwa cha inu? Kodi munabatizidwa mʼdzina la Paulo?
14 Ndi nin liburi libo kiti Kutellẹ na nna shintin umon mine nmyen ba, se kiribun nin Gayus.
Ine ndikuyamika kuti sindinabatizepo mmodzi mwa inu kupatula Krispo ndi Gayo,
15 Una so nani bara na umong mine man woru miyari na shintin ghe nmyen nan nya lissa ning ba.
mwakuti palibe amene anganene kuti anabatizidwa mʼdzina langa.
16 Ina kuru nshintino anan gan Istifanus ku. Nbanda nani, nan yiru sa nnakuru nshinto among tutung ba.
(Inde, ine ndinabatizanso a mʼbanja la Stefano, koma sindikumbukira ngati ndinabatizanso wina aliyense).
17 Bara ana Kristi na tuyi nshitu anitari nmyen ba nani nsu uwazi nliru ntucuari na nin nagbulan njinjin nnit ba, bara kuca nkootunu in Kristi wa so imon ihe.
Pakuti Khristu sananditume ine kudzabatiza, koma kudzalalikira Uthenga Wabwino, osati ndi mawu anzeru za umunthu, kuopa kuti mtanda wa Khristu ungakhale wopanda mphamvu.
18 Bara kadura kuca nkotunuee tilalanghari kiti na lenge na i din nan nya nkul. Nani kitii na lenge na Kutellẹ din kacisso mine, likara Kutellẹ ari.
Pakuti uthenga wa mtanda ndi chopusa kwa iwo amene akuwonongeka, koma kwa ife amene tikupulumutsidwa uthengawu ndi mphamvu ya Mulungu.
19 Bara ina nyertin, “Meng ma malu kiti nin dadiu na yinjini” mma canu uyinnu na nan yiru.
Pakuti kwalembedwa kuti, “Ine ndidzawononga nzeru za anthu anzeru; luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
20 Unit ujinjinghe din weri? Unan ni nyerte din we? Unan piziru in yinnu nko kuje din we? Na Kutellẹ na kpilya njinjin in yeh misoo tilalang ba? (aiōn g165)
Munthu wanzeru ali kuti? Munthu wozama ndi maphunziro ali kuti? Munthu wodziwa zakuya zamakono ali kuti? Kodi Mulungu sanazipusitse nzeru za dziko lapansi? (aiōn g165)
21 Bara na uyih vat nin jinjing nnin na una yinnin Kutellẹ ba, una poah Kutellẹ liburi nan nya tilalan nbellu nliru Kutelle kiti na lenge na iyinna.
Tsono poti mwa nzeru za Mulungu dziko lapansi mu nzeru zake silinamudziwe Iye, Mulungu amakondweretsedwa kuti kudzera mu chopusa cha zomwe zinalalikidwa apulumutse iwo amene akhulupirira.
22 A Yahudawa wa piziru imon al'ajibi a Hilinawa pizira njinjing.
Ayuda amafuna zizindikiro zodabwitsa ndipo Agriki amafunafuna nzeru,
23 Nani arik din uwazi nkotunu in Kristi, litala ntizuru na Yahudawa a tilalang kiti na Hilinawa.
koma ife timalalikira Khristu wopachikidwa. Chitsa chokhumudwitsa kwa Ayuda ndi chopusa kwa a mitundu ina.
24 Kiti na lenge na Kutellẹ na yicila, a Yahudawa nin na Hilinawa, ti din su uwazi in Kristi nafo Likara nin kujinjin Kutellẹ.
Koma kwa iwo amene Mulungu anawayitana, Ayuda ndi Agriki omwe, Khristu ndi mphamvu ya Mulungu ndi nzeru za Mulungu.
25 Bara tilalang Kutellẹ katin likara njinjing nanit, a usali likara Kutellẹ katina akara nanit.
Pakuti za Mulungu zooneka ngati zopusa, ndi za nzeru kuposa nzeru za munthu, ndipo za Mulungu zooneka ngati zofowoka, zili ndi mphamvu kuposa mphamvu za munthu.
26 Yenen imusun in yicilue na Kutellẹ na yicila munu mun, nuana nilime nin nishono. Na gbardan mine wa di jinjing ba nan nya yenjun nanit. Na gbardang mine wadi nin gongong mbun nanit ba.
Abale taganizirani mmene munalili musanayitanidwe. Si ambiri a inu munali a nzeru, si ambiri a inu munali a mphamvu zamakopedwe. Si ambiri a inu munali obadwa pa ulemerero.
27 Nani Kutellẹ wa fere imon ilalang in yih ani unit ujinjing ncin. Kutellẹ waa fere imon nsali nakara in yih ani imon nakara in yih ncin mun.
Koma Mulungu anasankha zinthu zopusa za dziko lapansi kuti achititse manyazi anzeru. Mulungu anasankha zinthu zofowoka za dziko lapansi kuti achititse manyazi amphamvu.
28 Kutellẹ wa fere imon igugur na ina filing in yih umunu imon ile na tiyira inin nafo imon ile na arik in yira imon icinari.
Anasankha zinthu zapansipansi ndi zopeputsidwa za dziko la pansi lino, zinthu zimene kulibe, kuti asukulutse zimene zilipo,
29 Ana su nani bara ummong wa se imon for figiri mbun me.
kuti munthu asanyade pamaso pa Mulungu.
30 Bara imon ile na Kutellẹ na su, nene i di nan nyan Kristi Yisa, Ulenge na ana so nari njinjing kiti Kutellẹ katwa kacine bite, nlau bite nin utucu bite.
Nʼchifukwa cha Iye kuti inu muli mwa Khristu Yesu, amene wakhala nzeru ya kwa Mulungu, kwa ife, kunena kuti kulungama kwathu, chiyero ndi chipulumutso.
31 Nafo, na i nyerte nabelin, “Na ulenge na ana fo figiri na a fo nan nyan Cikilari.”
Choncho poti zinalembedwa kuti, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”

< 1 Ukorintiyawa 1 >