< Четвертая книга Царств 18 >

1 И бысть в лето третие Осии сына Илы царя Израилева, воцарися Езекиа сын Ахаза царя Иудина:
Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu.
2 сын двадесяти пяти лет бе егда нача царствовати, и двадесять девять леть царствова во Иерусалиме. Имя же матере его Авуфа дщи Захариина.
Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya.
3 И сотвори правое пред очима Господнима, по всем елика сотвори отец его Давид:
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
4 той разруши высокая, и сокруши вся капища, и искорени дубравы и змию медяную, юже сотвори Моисей, яко и до дний тех сынове Израилевы беху кадяще ей: и назва имя ей Неестан.
Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).
5 На Господа Бога Израилева упова, и но нем не бысть подобен ему в царех Иудиных и в бывших прежде его:
Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu.
6 и прилепися Господеви, не отступи от Него, и сохрани заповеди Его, елики заповеда Моисей:
Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose.
7 и бе Господь с ним, и во всех, яже творяше, смысляше. И сопротивися царю Ассирийскому и не поработа ему:
Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso.
8 той победи иноплеменники даже до Газы и до предел ея, от столпа стрегущих и даже и града тверда.
Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.
9 И бысть в лето четвертое царя Езекии, сие же лето седмое Осии, сыну Илы, царю Израилеву, взыде Саламанассар царь Ассирийск на Самарию и обседе ю,
Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga
10 и взя ю при концы триех лет, в шестое лето Езекиево, сие лето девятое Осии царя Израилева, и пленена бысть Самариа.
Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli.
11 И преведе царь Ассирийский Самаряны во Ассирию, и посади я на Алаи и на Аворе, реках Гозанских, и в пределех Мидских:
Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
12 понеже не послушаша гласа Господа Бога своего и преступиша завет Его, вся елика заповеда Моисей раб Господень, и не послушаша, и не сотвориша.
Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.
13 И в четвертоенадесять лето царя Езекии, взыде Сеннахирим царь Ассирийский на грады Иудины твердыя и взят я.
Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda.
14 И посла Езекиа царь Иудин послы к царю Ассирийску в Лахис, глаголя: согреших, возвратися от мене: еже аще возложиши на мя, то понесу. И возложи царь Ассирийский на Езекию царя Иудина триста талант сребра и тридесять талантов злата.
Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000.
15 И даде Езекиа все сребро обретшееся в дому Господни и в сокровищих дому царева.
Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.
16 Во время оно ссече Езекиа царь Иудин двери храма Господня и утвержения, яже позлати Езекиа царь Иудин, и даде их царю Ассирийску.
Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.
17 И посла царь Ассирийск Фарфана и Равосаиа и Рапсака от Лахиса на Иерусалим к царю Езекии с силою тяжкою зело. И взыдоша, и приидоша ко Иерусалиму, и сташа у водотечи купели вышния, яже есть на пути села белилнаго,
Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa.
18 и возопиша ко Езекии. И изыде к ним Елиаким сын Хелкиев строитель, и Сомнас книгочий, и Иоас сын Сафатов воспоминатель.
Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.
19 И рече к ним Рапсак: рцыте ныне ко Езекии: сице глаголет царь великий, царь Ассирийский: что упование сие, на неже уповаеши?
Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’
20 Рекл еси: токмо словеса устен, совет и сила на брань: ныне убо на кого надежду отвергл еси мене?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
21 Ныне с, надеешися ты на жезл тростяный сломленый сей, на Египет ли? Наньже аще опрется муж, внидет в руку его и пронзет ю: тако фараон царь Египетский всем надеющымся нань:
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’”
22 и аще мне речете: на Господа Бога надеемся: не той ли сей, егоже и отстави Езекиа высокая его и жертвенники его, и рече Иуде и Иерусалиму: поклонитеся пред жертвенником сим во Иерусалиме?
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”
23 И ныне соединитеся с господином моим царем Ассирийским, и дам тебе две тысящы коней, аще можеши имети всадники на ня:
“‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
24 и како отвратиши лице топарха единаго от рабов господина моего малейших, и уповал еси сам на Египет, на колесницы и кони?
Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo?
25 И ныне убо еда без Господа взыдохом на место сие, еже потребити и рече бо Господь ко мне: взыди на землю сию и потреби ю.
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’”
26 И рече Елиаким сын Хелкиин и Сомнас и Иоас ко Рапсаку: глаголи ныне ко отроком твоим сирски, яко слышим мы, а не глаголи к нам иудейски, и почто глаголеши во ушы людий, иже на стене?
Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
27 И рече к ним Рапсак: еда к господину твоему и к тебе посла мя господин мой глаголати словеса сия? Не к мужем ли седящым на стене, еже ясти им гной свой и пити им сечь свою с вами вкупе?
Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
28 И ста Рапсак, и возопи гласом великим иудейски, и глагола, и рече: слышите словеса великаго царя Ассирийска:
Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
29 сице глаголет царь: да не возносит вас царь Езекиа словесы, понеже не возможет вас изяти из руки моея:
Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa.
30 и да не обнадеживает вас Езекиа Господем, глаголя: изимая измет вы Господь, и не имать предатися град сей в руце царя Ассирийска:
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
31 не послушайте Езекии, яко сице глаголет царь Ассирийский: сотворите со мною благословение и изыдите ко мне, и да пиет муж от винограда своего, и муж вкусит от смоквей своих, и да пиет воду от рова своего,
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
32 дондеже прииду и поиму вы в землю (такову) якоже земля ваша, земля пшеницы и вина, и хлебов и виноградов, земля масличин елеа и меда, и живи будете и не умрете: и не послушайте Езекии, яко прельщает вы, глаголя: Господь ны избавит:
mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa! “Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’
33 еда избавляюще избавиша бози языков кийждо их свою страну из руки царя Ассирийска?
Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
34 Где есть бог Емафа и Арфада? Где есть бог Сепфаруима, Ана и Ава? Еда избавиша Самарию из руку моею?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
35 Кто во всех бозех земных, иже избавиша земли и от руки моея? И како измет Господь Иерусалима из руки моея?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
36 И умолкоша людие и не отвещаша ему слова, яко заповеда им царь глаголя: не отвещайте ему.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
37 И вниде Елиаким сын Хелкиин строитель, и Сомнас книгочий, и Иоас сын Сафатов воспоминатель ко Езекии, раздравше ризы своя, и возвестиша ему словеса Рапсакова.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.

< Четвертая книга Царств 18 >