< Третья книга Царств 1 >

1 И царь Давид бысть стар прешед дни, и одеваху его ризами (многими), и не согревашеся.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 И реша отроцы его ему: да поищут господину нашему царю девицы юныя, и предстоит цареви, и будет греющи его, и да лежит с ним, и согреется господин наш царь.
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 И искаша отроковицы добрыя от всего предела Израилева, и обретоша Ависагу Сумантяныню, и приведоша ю ко царю.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 И бе отроковица добра видением зело: и бысть греющи царя и служаше ему: царь же не позна ея.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 И Адониа сын Аггифин вознесеся, глаголя: аз имам царствовати. И сотвори себе колесницы и конники, и пятьдесят мужей еже ходити пред ним.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 И не возбрани ему отец его никогда, глаголя: почто сие ты сотворил еси? И бе той красен зраком зело, и того роди по Авессаломе.
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 И беша совети его со Иоавом сыном Саруиным и со Авиафаром иереом, и помогаху вслед Адонии.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Садок же иерей и Ванеа сын Иодаев, и Нафан пророк и Семей, и Рисий и сынове сильнии Давидовы не быша по Адонии.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 И пожре Адониа овцы и телцы и агнцы при камени Зоелефе, иже бе близ источника Рогиля: и призва всю братию свою, сыны царевы, и вся мужы Иудовы, отроки царевы:
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 Нафана же пророка и Ванеа и сильных и Соломона брата своего не зва.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 И рече Нафан ко Вирсавии матери Соломони, глаголя: не слышала ли еси, яко воцарися Адониа сын Аггифин, господин же наш Давид не весть:
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 ныне убо совещаю ти совет, и избавиши душу свою и душу сына твоего Соломона:
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 гряди, вниди к царю Давиду и речеши к нему, глаголющи: не ты ли, господи мой царю, клялся еси рабе твоей, глаголя: яко Соломон сын твой имать царствовати по мне, и той сядет на престоле моем? И что яко воцарися Адониа?
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 И се, еще глаголющей тебе тамо со царем, и аз вниду вслед тебе и дополню словеса твоя.
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 И вниде Вирсавиа ко царю в ложницу. И царь стар зело, и Ависаг Сумантяныня бяше служащи царю.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 И приклонися Вирсавиа и поклонися цареви. И рече царь: что ти есть?
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 Она же рече: господи мой царю, ты клялся еси пред Господем Богом твоим рабе твоей, глаголя: яко сын твой Соломон имать царствовати по мне, и той сядет на престоле моем:
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 и се, ныне Адониа царствует, ты же, господи мой царю, не веси:
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 и пожре телцы и агнцы и овцы во множестве, и созва вся сыны царевы, и Авиафара жерца и Иоава князя силы, Соломона же раба твоего не призва:
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 ты же, господи мой царю, очи всего Израиля к тебе: да возвестиши им, кто сядет на престоле господина моего царя по нем:
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 и будет егда уснет господин мой царь со отцы своими, и буду аз и сын мой Соломон грешни.
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 И се, еще ей глаголющей с царем, и Нафан пророк прииде.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 И возвестиша царю, глаголюще се, Нафан пророк. И вниде пред лице царево, и поклонися царю пред лицем его до земли,
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 и рече Нафан: господи мой царю, ты ли рекл еси: Адониа да царствует по мне, и той да сядет на престоле моем?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 Яко сниде днесь и закла телцы и агнцы и овцы во множестве, и созва вся сыны царевы и князи сильных, и Авиафара иереа: и се, суть ядуще и пиюще пред ним, и реша: да живет царь Адониа:
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 и мене самаго раба твоего, и Садока иереа, и Ванеа сына Иодаева, и Соломона раба твоего не зва:
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 от господина ли царя моего бысть глагол сей? И не сказал еси рабу твоему, кто сядет на престоле господина моего царя по нем?
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 И отвеща царь Давид и рече: призовите ми Вирсавию. И вниде (Вирсавиа) пред царя и ста пред лицем его.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 И клятся царь и рече: жив Господь, иже избави душу мою от всея печали:
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 якоже бо кляхтися пред Господем Богом Израилевым, глаголя: яко Соломон сын твой воцарится по мне, и той сядет на престоле моем вместо мене, яко тако сотворю ему в днешний день.
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 И преклонися Вирсавиа лицем на землю, и поклонися царю и рече: да живет господин мой царь Давид во веки.
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 И рече царь Давид: призовите мне Садока жерца и Нафана пророка, и Ванеа сына Иодаева. И внидоша пред царя.
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 И рече им царь: поимите с собою рабы господина вашего, и всадите сына моего Соломона на мска моего, и ведите его к Гиону,
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 и да помажет его тамо Садок иерей и Нафан пророк в царя над Израилем, и вострубите трубою рожаною и речете: да живет царь Соломон:
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 и изыдите вслед его, и внидет, и сядет на престоле моем, и той воцарится вместо мене: и аз заповедах, да будет властелин над Израилем и Иудою.
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 И отвеща Ванеа сын Иодаев царю и рече: буди тако: да утвердит Господь Бог глагол сей господина моего царя:
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 якоже бе Господь со господином моим царем, тако да будет и с Соломоном, и да возвеличит престол его паче престола господина моего царя Давида.
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 И сниде Садок иерей и Нафан пророк, и Ванеа сын Иодаев, и Хереффи и Фелеффи, и всадиша Соломона на мска царя Давида, и возведоша его к Гиону:
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 и взя Садок иерей рог с елеем от скинии, и помаза Соломона, и воструби трубою рожаною, и реша вси людие: да живет царь Соломон.
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 И взыдоша вси людие вслед его и ликоваша в лицех, и веселяхуся веселием великим, и разседеся земля от гласа их.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 И слыша Адониа и вси званнии его, и тии скончаша уже ядуще. И слыша Иоав глас трубы рожаны и рече: кий глас есть града шумяща?
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 И еще Ему глаголющу, и се, Ионафан сын Авиафара иереа прииде. И рече Адониа: вниди, яко муж силы ты еси, и благая возвести.
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 И отвеща Ионафан и рече: известно, господин наш царь Давид постави Соломона царем:
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 и посла с ним царь Садока иереа и Нафана пророка, и Ванеа сына Иодаева, и Хереффи и Фелеффи, и всадиша его на мска царева:
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 и помазаша его Садок иерей и Нафан пророк на царство в Гионе, и взыдоша оттуду веселящеся, и возшуме град: сей глас, егоже слышасте:
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 и седе Соломон на престоле царстем:
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 и внидоша раби царевы благословити господина нашего царя Давида, глаголюще: да ублажит Бог имя Соломона сына твоего паче имене твоего, и да возвеличит престол его паче престола твоего: и поклонися царь на одре своем,
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 и сице рече царь: благословен Господь Бог Израилев, Иже даде днесь от семене моего седяща на престоле моем, и очи мои видят.
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 И ужасошася ужасом, и восташа вси званнии Адониевы, и отиде кийждо путем своим.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 И Адониа убояся от лица Соломоня, и воста и отиде, и ятся за рог олтаря.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 И возвестиша Соломону, глаголюще: се, Адониа убояся царя Соломона, и держится за рог олтаря, глаголя: да кленетмися днесь царь Соломон, яко не убиет раба своего оружием.
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 И рече Соломон: аще будет сын силы, ни влас главы его упадет на землю: аще же злоба обрящется в нем, умрет.
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 И посла царь Соломон, и сведоша его со олтаря. И вниде, и поклонися царю Соломону. И рече ему Соломон: иди в дом свой.
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< Третья книга Царств 1 >