< Filemon 1 >

1 Siak ni Pablo, maysa a balud ni Cristo Jesus, ken ni kabsattayo a Timoteo ket agsursuratkami kenni Felimon, nga ay-ayatenmi a gayyem ken katrabahoan,
Kuchokera kwa Paulo, amene ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu ndi Timoteyo mʼbale wathu. Kulembera Filemoni, bwenzi lathu lokondedwa ndi mtumiki mnzathu.
2 ken ni Apia a kabsatmi a babai, ken ni Arkipo a padami a soldado, ken ti iglesia nga aggimong iti balaymo:
Kwa Apiya mlongo wathu, Arkipo msilikali mnzathu, ndiponso mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwanu.
3 Parabur kadakayo ken kapia manipud iti Dios nga Amatayo ken ni Apo Jesu-Cristo.
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
4 Kankanayon nga agyamanak iti Diosko. Dakdakamatenka kadagiti karkararagko,
Ine ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakukumbukira iwe mʼmapemphero anga.
5 Nangngegko iti ayat ken ti pammati nga adda kenka kenni Apo Jesus ken para kadagiti amin a namati.
Pakuti ndamva za chikondi chako, za chikhulupiriro chako mwa Ambuye Yesu ndiponso za chikondi chako pa oyera mtima onse.
6 Ikararagko a nabunga koma iti pannakiramanmo iti pammati a maipaay iti pannakaammo iti tunggal nasayaat a banag nga adda kadatayo kenni Cristo.
Ine ndikupemphera kuti mgwirizano wako ndi ife mʼchikhulupiriro ukhale opindulitsa pozamitsa nzeru zako zozindikira zinthu zilizonse zabwino zimene timagawana chifukwa cha Khristu.
7 Gapu ta naaddaanak iti kasta unay a rag-o ken liwliwa gapu iti ayatmo, agsipud ta pinaragsakmo dagiti puso dagiti namati, kabsat.
Mʼbale, chikondi chako chandipatsa chimwemwe chachikulu ndi chilimbikitso, chifukwa umatsitsimutsa mitima ya anthu a Ambuye.
8 Ngarud, uray pay no adda kaniak amin a kinatured gapu kenni Cristo tapno bilinenka iti rumbeng nga aramidem,
Tsopano ngakhale kuti mwa Khristu nditha kulimba mtima ndi kulamulira kuti uchite zimene uyenera kuchita,
9 ngem gapu iti ayat, dawdawatek ketdi kenka—Siak, ni Pablo, maysa a nataengan a tao, ken balud ita gapu kenni Cristo Jesus.
komabe ndikupempha mwachikondi. Ine Paulo, munthu wokalamba, ndipo tsopano ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu,
10 Agdawdawatak kenka iti maipapan kenni Onesimo nga anakko, a nagbalinak a pannakaamana iti pannakabaludko.
ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga Onesimo, amene ndamubala ndili mu unyolo.
11 Gapu ta awan idi iti serserbina kenka, ngem napategen isuna ita kadata.
Anali wopanda phindu kwa iwe, koma tsopano wasanduka wa phindu kwa iwe ndi kwa inenso.
12 Pagsubliek isuna kenka—nga isu ti ay-ayatek unay.
Ine ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, koma potero ndikukhala ngati ndikutumiza mtima wanga weniweni.
13 Tarigagayko a pagtalinaedek pay koma isuna kaniak, tapno makatulong kaniak bayat iti kinaawanmo, bayat ti pannakaibaludko gapu iti ebanghelio.
Ndikanakonda ndikanakhala naye kuno kuti iyeyo azinditumikira mʼmalo mwako pamene ndili mu unyolo chifukwa cha Uthenga Wabwino.
14 Ngem saanko a kayat ti agaramid iti aniaman a banag nga awan pammalubosmo. Inaramidko daytoy tapno saan a maaramid ti animan a naimbag gapu ta pinilitka, ngem gapu ta kayatmo nga aramiden daytoy.
Koma sindikufuna kuchita kanthu osakufunsa, nʼcholinga chakuti chilichonse chabwino ungandichitire chikhale mwakufuna kwako osati mokakamiza.
15 Nalabit a ti rason a naisina isuna kenka iti apagbiit, ket tapno agsubli kenka iti agnanayon, (aiōnios g166)
Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse. (aiōnios g166)
16 Tapno saan laengen isuna a kas tagabu, ngem nangatngato pay ngem tagabu, kas maysa nga ay-ayaten a kabsat— nangnangruna kaniak, ken ad-adda pay koma kenka, iti lasag ken iti Apo.
Osati ngati kapolo, koma woposa kapolo, ngati mʼbale wokondedwa. Iyeyu ndi wokondedwa kwambiri kwa ine koma kwa iweyo ndi wokondedwa koposa, ngati munthu komanso ngati mʼbale mwa Ambuye.
17 No ibilangnak ngarud a kas kadua, awatem isuna a kas ti panangawatmo koma kaniak.
Tsono ngati umati ndine mnzako, umulandire iyeyu monga momwe ukanandilandirira ineyo.
18 Ngem no nagbasol isuna kenka, wenno nakautang kenka iti aniaman a banag, siakon ti agbayad iti dayta.
Ngati anakulakwira kapena kukongola kanthu kalikonse, ndidzalipira ineyo.
19 Siak, ni Pablo, isuratko daytoy babaen iti bukodko nga ima: Bayadankanto. Saankon nga ipalagip kenka a bulodmo kaniak ti biagmo.
Ine, Paulo ndikulemba zimenezi ndi dzanja langa. Ine ndidzalipira. Nʼkosafunika kukukumbutsa kuti iweyo ngongole yako kwa ine ndi moyo wakowo.
20 Wen, kabsat, ipalubosmo nga agragsakak iti Apo; pabaroem ti pusok kenni Cristo.
Mʼbale, ndikufuna kuti ndipindule nawe mwa Ambuye; tsono tsitsimutsa mtima wanga mwa Khristu.
21 Adda talgedko maipanggep iti panagtulnogmo, agsuratak kenka, nga ammok nga ad-adu pay ti aramidemto ngem ti dawatek.
Ine ndili ndi chitsimikizo cha kumvera kwako pamene ndikukulembera kalatayi. Ndikulemba ndikudziwa kuti udzachita ngakhale kuposa zimene ndakupemphazi.
22 Maysa pay, mangisaganaka ti siled ti sangaili para kaniak, ta namnamaek a babaen kadagiti karkararagyo ket mapasyarkayonto iti mabiit.
Chinthu chinanso ndi ichi: undikonzere malo, chifukwa ndikukhulupirira kuti Mulungu adzamvera mapemphero anu ndi kundibwezera kwa inu.
23 Kablaawannaka Ni Epafras a padak a balud kenni Cristo Jesus,
Epafra, wamʼndende mnzanga chifukwa cha Khristu Yesu akupereka moni.
24 ken kablaawandakayo met da Marcos, Aristarco, Demas, Lucas, a katrabahoak.
Atumiki anzanga awa, Marko, Aristariko, Dema ndi Luka, akuperekanso moni.
25 Sapay koma ta ti parabur ni Apotayo a Jesu-Cristo ti makikaadda iti espirituyo. Amen.
Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wako.

< Filemon 1 >