< Roma 1 >

1 Ni Pablo, maysa nga adipen ni Jesu-Cristo, naayaban nga agbalin nga apostol, ken nailasin para iti ebanghelio ti Dios.
Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
2 Daytoy ti ebanghelio nga inkarina sakbay iti amin babaen kadagiti propetana iti Nasantoan a Sursurat.
umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
3 Maipapan daytoy iti Anakna a naipasngay manipud kadagiti kaputotan ni David no maipapan iti lasag.
Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
4 Naipakaammo isuna nga isu ti Anak ti Dios babaen iti pannakabalin iti Espiritu iti kinasanto babaen iti panagungar manipud iti patay, ni Jesu- Cristo nga Apotayo.
Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
5 Inawattayo ti parabur ken panagbalin nga apostol babaen kenkuana para iti panagtulnog iti pammati kadagiti amin a nasion, a maigapu iti naganna.
ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
6 Kadagitoy a nasion, naayabankayo met nga agbalin a kukua ni Jesu-Cristo.
Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
7 Daytoy a surat ket para kadagiti amin nga adda idiay Roma, dagiti ay-ayaten ti Dios, a naayaban nga agbalin a nasantoan a tattao. Parabor koma ti adda kadakayo, ken kapia manipud iti Dios nga Amatayo ken ni Apo Jesu-Cristo.
Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
8 Umuna, agyamanak iti Diosko babaen kenni Jesu-Cristo gapu kadakayo amin, gapu ta naiwaragawag ti pammatiyo iti entero a lubong.
Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
9 Ta ti Dios ti saksik, a pagserserbiak iti espirituk iti ebanghelio ti Anakna, no kasano nga itultuloyko a dakdakamatenkayo.
Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
10 Kankanayonko a kidkiddawen kadagiti kararagko a babaen iti aniaman a wagas ket agballigi-ak koman ita babaen iti pagayatan ti Dios iti iyuumayko kadakayo.
Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
11 Gapu ta tartarigagayak a makitakayo, tapno mangitedak koma kadagiti naespirituan a sagut, tapno mapapigsakayo.
Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
12 Dayta ket, kalkalikagumak a makipinnabileg kadakayo, babaen iti pammati ti tunggal maysa, pammatiyo ken pammatik.
ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
13 Ita, saanko a kayat a saanyo nga ammo, kakabsat, a masansan a pangpanggepek nga umay kadakayo, ngem malaplappedanak agingga ita. Kayatko daytoy tapno maaddaanak met kadagiti bunga kadakayo a kas met kadagiti nabatbati a Hentil.
Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
14 Adda pagrebbengak kadagiti Griego ken kadagiti gangannaet, kadagiti masirib ken kadagiti maag.
Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
15 Ngarud, no maipapan kaniak, nakasaganaak met a mangiwaragawag iti ebanghelio kadakayo nga adda dita Roma.
Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
16 Gapu ta saanko nga ibain ti ebanghelio, agsipud ta daytoy ti pannakabalin ti Dios a maipaay iti pannakaisalakan iti amin a mamati, umuna ket para kadagiti Judio ket kalpasanna kadagiti Griego.
Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
17 Ta iti daytoy, naipakaammo ti kinalinteg ti Dios manipud pammati agingga iti pammati, a kas naisurat, “Agbiagto dagiti nalinteg babaen iti pammati.”
Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
18 Ta naipakaammo ti pungtot ti Dios manipud langit a maibusor iti amin a saan a nadiosan ken kinakillo dagiti tattao, a babaen iti kinakillo ket igawidna ti kinapudno.
Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
19 Daytoy ket gapu ta makitada ti nammoan maipanggep iti Dios. Ta linawlawagan ida ti Dios.
Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
20 Ta nagbalin a silalawag a makita dagiti saan a makita a kababalinna sipud pay iti pannakaparsua ti lubong. Maawatan dagitoy babaen kadagiti naparsua a banbanag. Dagitoy a saan a makita a kababalinna ket ti agnanayon a pannakabalin ken kinaDiosna. Kas pagbanaganna, awan pagpambar dagitoy a tattao. (aïdios g126)
Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios g126)
21 Daytoy ket gapu ta uray no naammoanda ti maipanggep iti Dios, saanda nga intan-ok isuna a kas Dios, wenno saanda a nagyaman kenkuana. Ngem ketdi, nagbalinda a maag iti panpanunotda, ken limmidem dagiti saan a makarikna a puspusoda.
Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
22 Ibagbagada a masiribda ngem nagbalinda a maag.
Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
23 Insukatda ti dayag ti saan a madadael a Dios iti kaas-asping iti langa iti madadael a tao, kadagiti billit, kadagiti uppat ti sakana nga ayup, ken kadagiti agkarkarayam a banbanag.
Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
24 Ngarud, binaybay-an ida iti Dios kadagiti panaggartem ti pusoda iti kinarugit, para iti pakaibabainan dagiti bagbagida met laeng.
Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
25 Isuda dagiti nangisukat iti kinapudno ti Dios para iti inuulbod, ken nangdayaw ken nagserbi iti naparsua imbes nga iti Namarsua, nga agnanayon a maidaydayaw. Amen. (aiōn g165)
Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
26 Gapu iti daytoy, binaybay-an ida ti Dios kadagiti nakababain a regget, ta insukat dagiti babbaida ti gagangay a pakaaramatanda para iti maibusor iti gagangay a kinasiasinoda.
Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
27 Kasta met, pinanawan met dagiti lallaki ti gagangay a pakaaramatanda kadagiti babbai ket sineggedanda dagiti kinaderrepda iti maysa ken maysa. Dagitoy dagiti lallaki a nangaramid iti saan nga umno kadagiti padada a lallaki, ken nangawat ti rumbeng a dusa kadagiti pannakaiyaw-awanda iti gagangay a nakaiparsuaanda.
Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
28 Gapu ta saanda nga immanamong iti pannakaadda ti Dios iti pannakaammoda, binaybay-an ida ti Dios iti dakes a panunot, tapno aramidenda dagitoy saan a maiparbeng.
Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
29 Napnoda kadagiti amin a kinakillo, kinadangkes, kinaagum ken gura. Napnoanda iti kinaap-apal, kinamammapatay, kinamanagaapa, kinamanangallilaw, ken dakes a pangpanggep.
Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
30 Mannaritada, mammaperdi, ken managgura iti Dios. Naranggasda, natangsit, ken napangas. Isuda dagiti agar-aramid kadagiti dakes a banbanag, ken nasukirda kadagiti nagannakda.
osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
31 Awan iti pannakaawatda; saanda a mapagtalkan, awanan gagangay a panagayat, ken saan a manangngaasi.
alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
32 Maawatanda dagiti annuroten ti Dios, a maikari iti patay dagiti agar-aramid iti kasta a banbanag. Ngem saanda laeng nga ar-aramiden dagitoy a banbanag, anamonganda met dagiti dadduma nga agar-aramid kadagitoy.
Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.

< Roma 1 >