< Zefaniya 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
Woe to her who is rebellious and polluted, to the oppressing city!
2 Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
She obeyed not the voice. She received not correction. She trusted not in Jehovah. She did not draw near to her God.
3 Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Her rulers in the midst of her are roaring lions. Her judges are evening wolves. They leave nothing till the morrow.
4 Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
Her prophets are airy and treacherous men. Her priests have profaned the sanctuary. They have done violence to the law.
5 Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
Jehovah in the midst of her is righteous. He will not do iniquity. Every morning he brings his justice to light. He does not fail, but the unjust man knows no shame.
6 “Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
I have cut off nations. Their battlements are desolate. I have made their streets waste, so that none passes by. Their cities are destroyed, so that there is no man, so that there is no inhabitant.
7 Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
I said, Only fear thou me. Receive correction, so her dwelling shall not be cut off, according to all that I have appointed concerning her. But they rose early and corrupted all their doings.
8 Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
Therefore wait ye for me, says Jehovah, until the day that I rise up to the prey. For my determination is to gather the nations, that I may assemble the kingdoms, to pour upon them my indignation, even all my fierce anger. For all the earth shall be devoured with the fire of my jealousy.
9 “Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
For then I will turn to the peoples of a pure language, that they may all call upon the name of Jehovah, to serve him with one consent.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
From beyond the rivers of Ethiopia, my suppliants, even the daughter of my dispersed, shall bring my offering.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
In that day thou shall not be put to shame for all thy doings, in which thou have transgressed against me. For then I will take away out of the midst of thee those who rejoice in thy pride, and thou shall no more be haughty in my holy mountain.
12 Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
But I will leave in the midst of thee an afflicted and poor people, and they shall take refuge in the name of Jehovah.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
The remnant of Israel shall not do iniquity, nor speak lies, nor shall a deceitful tongue be found in their mouth. For they shall feed and lie down, and none shall make them afraid.
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Sing, O daughter of Zion. Shout, O Israel. Be glad and rejoice with all the heart, O daughter of Jerusalem.
15 Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
Jehovah has taken away thy judgments. He has cast out thine enemy. The King of Israel, even Jehovah, is in the midst of thee. Thou shall not fear evil any more.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
In that day it shall be said to Jerusalem, Fear thou not, O Zion. Let not thy hands be slack.
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
Jehovah thy God is in the midst of thee, a mighty one who will save. He will rejoice over thee with joy. He will rest in his love. He will joy over thee with singing.
18 “Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
I will gather those who sorrow for the solemn assembly, who were of thee, to whom the burden upon her was a reproach.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
Behold, at that time I will deal with all those who afflict thee. And I will save that which is lame, and gather that which was driven away, and I will make them a praise and a name, whose shame has been in all the earth.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.
At that time I will bring you in, and at that time I will gather you. For I will make you a name and a praise among all the peoples of the earth when I bring back your captivity before your eyes, says Jehovah.

< Zefaniya 3 >