< Masalimo 98 >

1 Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
O sing to Jehovah a new song, for he has done marvelous things. His right hand, and his holy arm, has wrought salvation for him.
2 Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
Jehovah has made known his salvation. He has openly shown his righteousness in the sight of the nations.
3 Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
He has remembered his loving kindness and his faithfulness toward the house of Israel. All the ends of the earth have seen the salvation of our God.
4 Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
Make a joyful noise to Jehovah, all the earth. Break forth and sing for joy, yea, sing praises.
5 Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
Sing praises to Jehovah with the harp. With the harp and the voice of melody,
6 ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
with trumpets and sound of cornet, make a joyful noise before the King-Jehovah.
7 Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
Let the sea roar, and the fullness thereof, the world, and those who dwell in it.
8 Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
Let the floods clap their hands. Let the hills sing for joy together
9 izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.
before Jehovah, for he comes to judge the earth. He will judge the world with righteousness, and the peoples with equity.

< Masalimo 98 >