< Masalimo 96 >

1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
O sing to Jehovah a new song. Sing to Jehovah, all the earth.
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Sing to Jehovah, bless his name. Show forth his salvation from day to day.
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Declare his glory among the nations, his marvelous works among all the peoples.
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
For great is Jehovah, and greatly to be praised. He is to be feared above all gods.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
For all the gods of the peoples are idols, but Jehovah made the heavens.
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
Honor and majesty are before him. Strength and beauty are in his sanctuary.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Ascribe to Jehovah, ye kindred of the peoples. Ascribe to Jehovah glory and strength.
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
Ascribe to Jehovah the glory due to his name. Bring an offering, and come into his courts.
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
O worship Jehovah in holy array. Tremble before him, all the earth.
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
Say among the nations, Jehovah reigns! The world also is established that it cannot be moved. He will judge the peoples with equity.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
Let the heavens be glad, and let the earth rejoice. Let the sea roar, and the fullness thereof.
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
Let the field exult, and all that is in it. Then all the trees of the wood shall sing for joy
13 idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
before Jehovah, for he comes. For he comes to judge the earth. He will judge the world with righteousness, and the peoples with his truth.

< Masalimo 96 >