< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
O Jehovah, thou God to whom vengeance belongs, thou God to whom vengeance belongs, shine forth.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Lift up thyself, thou judge of the earth. Render to the proud a recompense.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
Jehovah, how long shall the wicked, how long shall the wicked triumph?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
They prate, they speak arrogantly. All the workers of iniquity boast themselves.
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
They break in pieces thy people, O Jehovah, and afflict thy heritage.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
They kill the widow and the sojourner, and murder the fatherless.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
And they say, Jehovah will not see, nor will the God of Jacob consider.
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Consider, ye brutish among the people, and ye fools, when will ye be wise?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
He who planted the ear, shall he not hear? He who formed the eye, shall he not see?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
He who chastises the nations, shall he not correct, even he who teaches man knowledge?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Jehovah knows the thoughts of man, that they are vanity.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Blessed is the man whom thou chasten, O Jehovah, and teach out of thy law,
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
that thou may give him rest from the days of adversity, until the pit is dug for a wicked man.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
For Jehovah will not cast off his people, nor will he forsake his inheritance.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
For judgment shall return to righteousness, and all the upright in heart shall follow it.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Who will rise up for me against the evildoers? Who will stand up for me against the workers of iniquity?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Unless Jehovah had been my help, my soul would have soon dwelt in silence.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
When I said, My foot slips, thy loving kindness, O Jehovah, held me up.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
In the multitude of my thoughts within me thy comforts delight my soul.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Shall the throne of wickedness have fellowship with thee, which frames mischief by statute?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
They gather themselves together against the soul of a righteous man, and condemn innocent blood.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
But Jehovah has been my high tower, and my God the rock of my refuge.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
And he has brought upon them their own iniquity, and will cut them off in their own wickedness. Jehovah our God will cut them off.

< Masalimo 94 >