< Masalimo 87 >

1 Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
His foundation is in the holy mountains.
2 Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
Jehovah loves the gates of Zion more than all the dwellings of Jacob.
3 Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
Glorious things are spoken of thee, O city of God. (Selah)
4 “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
I will make mention of Rahab and Babylon as among those who know me. Behold, Philistia, and Tyre, with Ethiopia: This man was born there.
5 Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
Yea, of Zion it shall be said, this and that man was born in her, and the Most High himself will establish her.
6 Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
Jehovah will count when he writes up the peoples: This man was born there. (Selah)
7 Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
Those who sing as well as those who dance shall say, All my fountains are in thee.

< Masalimo 87 >