< Masalimo 85 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Jehovah, thou have been favorable to thy land. Thou have brought back the captivity of Jacob.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
Thou have forgiven the iniquity of thy people. Thou have covered all their sin. (Selah)
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
Thou have taken away all thy wrath. Thou have turned from the fierceness of thine anger.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Turn us, O God of our salvation, and cause thine indignation toward us to cease.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Will thou be angry with us forever? Will thou draw out thine anger to all generations?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Will thou not revive us again, that thy people may rejoice in thee?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Show us thy loving kindness, O Jehovah, and grant us thy salvation.
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
I will hear what God, Jehovah, will speak, for he will speak peace to his people, and to his sanctified. But let them not turn again to folly.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Surely his salvation is near those who fear him, that glory may dwell in our land.
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
Mercy and truth are met together. Righteousness and peace have kissed each other.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
Truth springs out of the earth, and righteousness has looked down from heaven.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Yea, Jehovah will give that which is good, and our land shall yield its increase.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
Righteousness shall go before him, and shall make his footsteps a path.

< Masalimo 85 >